< Job 9 >

1 Y RESPONDIÓ Job, y dijo:
Ndipo Yobu anayankha kuti,
2 Ciertamente yo conozco que es así: ¿y cómo se justificará el hombre con Dios?
“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
3 Si quisiere contender con él, no le podrá responder á una [cosa] de mil.
Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
4 El es sabio de corazón, y poderoso en fortaleza: ¿quién se endureció contra él, y quedó en paz?
Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
5 Que arranca los montes con su furor, y no conocen quién los trastornó:
Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
6 Que remueve la tierra de su lugar, y hace temblar sus columnas:
Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
7 Que manda al sol, y no sale; y sella las estrellas:
Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
8 El que extiende solo los cielos, y anda sobre las alturas de la mar:
Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
9 El que hizo el Arcturo, y el Orión, y las Pléyadas, y los lugares secretos del mediodía:
Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
10 El que hace cosas grandes é incomprensibles, y maravillosas, sin número.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
11 He aquí que él pasará delante de mí, y yo no lo veré; y pasará, y no lo entenderé.
Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
12 He aquí, arrebatará; ¿quién le hará restituir? ¿Quién le dirá, Qué haces?
Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
13 Dios no tornará atrás su ira, y debajo de él se encorvan los que ayudan á los soberbios.
Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
14 ¿Cuánto menos le responderé yo, y hablaré con él palabras estudiadas?
“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
15 Que aunque fuese yo justo, no responderé; antes habré de rogar á mi juez.
Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
16 Que si yo le invocase, y él me respondiese, aun no creeré que haya escuchado mi voz.
Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
17 Porque me ha quebrado con tempestad, y ha aumentado mis heridas sin causa.
Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
18 No me ha concedido que tome mi aliento; mas hame hartado de amarguras.
Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
19 Si [habláremos] de [su] potencia, fuerte por cierto es; si de juicio, ¿quién me emplazará?
Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
20 Si yo me justificare, me condenará mi boca; si [me dijere] perfecto, esto me hará inicuo.
Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
21 [Bien que] yo [fuese] íntegro, no conozco mi alma: reprocharé mi vida.
“Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
22 Una cosa resta que yo diga: Al perfecto y al impío él los consume.
Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
23 Si azote mata de presto, ríese de la prueba de los inocentes.
Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
24 La tierra es entregada en manos de los impíos, y él cubre el rostro de sus jueces. Si no [es él], ¿quién [es]? ¿dónde está?
Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
25 Mis días han sido más ligeros que un correo; huyeron, y no vieron el bien.
“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
26 Pasaron cual navíos veloces: como el águila que se arroja á la comida.
Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
27 Si digo: Olvidaré mi queja, dejaré mi aburrimiento, y esforzaréme:
Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
28 Contúrbanme todos mis trabajos; sé que no me darás por libre.
ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
29 Yo soy impío, ¿para qué trabajaré en vano?
Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
30 Aunque me lave con aguas de nieve, y limpie mis manos con la misma limpieza,
Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
31 Aun me hundirás en el hoyo, y mis propios vestidos me abominarán.
mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
32 Porque no es hombre como yo, para que yo le responda, y vengamos juntamente á juicio.
“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
33 No hay entre nosotros árbitro que ponga su mano sobre nosotros ambos.
Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
34 Quite de sobre mí su vara, y su terror no me espante.
munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
35 Entonces hablaré, y no le temeré: porque así no estoy en mí mismo.
Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.

< Job 9 >