< Job 8 >

1 Y RESPONDIÓ Bildad Suhita, y dijo:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 ¿Hasta cuándo hablarás tales cosas, y las palabras de tu boca serán [como] un viento fuerte?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 ¿Acaso pervertirá Dios el derecho, ó el Todopoderoso pervertirá la justicia?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Si tus hijos pecaron contra él, él los echó en el lugar de su pecado.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Si tú de mañana buscares á Dios, y rogares al Todopoderoso;
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Si fueres limpio y derecho, cierto luego se despertará sobre ti, y hará próspera la morada de tu justicia.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Y tu principio habrá sido pequeño, y tu postrimería acrecerá en gran manera.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Porque pregunta ahora á la edad pasada, y disponte para inquirir de sus padres de ellos;
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 Pues nosotros somos de ayer, y no sabemos, siendo nuestros días sobre la tierra como sombra.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 ¿No te enseñarán ellos, te dirán, y de su corazón sacarán palabras?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 ¿Crece el junco sin lodo? ¿crece el prado sin agua?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Aun él en su verdor no será cortado, y antes de toda hierba se secará.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Tales son los caminos de todos los que olvidan á Dios: y la esperanza del impío perecerá:
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Porque su esperanza será cortada, y su confianza es casa de araña.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Apoyaráse él sobre su casa, mas no permanecerá en pie; atendráse á ella, mas no se afirmará.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 [A manera de un árbol], está verde delante del sol, y sus renuevos salen sobre su huerto;
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Vanse entretejiendo sus raíces junto á [una] fuente, y enlazándose hasta un lugar pedregoso.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Si le arrancaren de su lugar, éste negarále entonces, [diciendo]: Nunca te vi.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Ciertamente éste será el gozo de su camino; y de la tierra de donde se [traspusiere], nacerán otros.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 He aquí, Dios no aborrece al perfecto, ni toma la mano de los malignos.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Aun henchirá tu boca de risa, y tus labios de júbilo.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Los que te aborrecen, serán vestidos de confusión; y la habitación de los impíos perecerá.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >