< Job 33 >

1 POR tanto, Job, oye ahora mis razones, y escucha todas mis palabras.
“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga; mutcherere khutu zonse zimene ndinene.
2 He aquí yo abriré ahora mi boca, y mi lengua hablará en mi garganta.
Tsopano ndiyamba kuyankhula; mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.
3 Mis razones [declararán] la rectitud de mi corazón, y mis labios proferirán pura sabiduría.
Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama; pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.
4 El espíritu de Dios me hizo, y la inspiración del Omnipotente me dió vida.
Mzimu wa Mulungu wandiwumba, mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.
5 Si pudieres, respóndeme; dispón [tus palabras], está delante de mí.
Mundiyankhe ngati mungathe; konzekani tsopano kuti munditsutse.
6 Heme aquí á mí en lugar de Dios, conforme á tu dicho: de lodo soy yo también formado.
Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu; nanenso ndinachokera ku dothi.
7 He aquí que mi terror no te espantará, ni mi mano se agravará sobre ti.
Musachite mantha ndipo musandiope ayi, Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.
8 De cierto tú dijiste á oídos míos, y yo oí la voz de tus palabras [que decían]:
“Koma inu mwayankhula ine ndikumva, ndamva mawu anuwo onena kuti,
9 Yo soy limpio y sin defecto; y soy inocente, y no hay maldad en mí.
‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo; ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.
10 He aquí que él buscó achaques contra mí, y me tiene por su enemigo;
Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo; Iye akundiyesa ngati mdani wake.
11 Puso mis pies en el cepo, y guardó todas mis sendas.
Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo, akulonda mayendedwe anga onse.’
12 He aquí en esto no has hablado justamente: yo te responderé que mayor es Dios que el hombre.
“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi, pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.
13 ¿Por qué tomaste pleito contra él? Porque él no da cuenta de ninguna de sus razones.
Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?
14 Sin embargo, en una ó en dos [maneras] habla Dios; [mas el hombre] no entiende.
Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana, ngakhale munthu sazindikira zimenezi.
15 Por sueño de visión nocturna, cuando el sueño cae sobre los hombres, cuando se adormecen sobre el lecho;
Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku, pamene anthu ali mʼtulo tofa nato pamene akungosinza chabe pa bedi,
16 Entonces revela al oído de los hombres, y les señala su consejo;
amawanongʼoneza mʼmakutu ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,
17 Para quitar al hombre de [su] obra, y apartar del varón la soberbia.
kumuchotsa munthu ku zoyipa, ndi kuthetseratu kunyada kwake,
18 Detendrá su alma de corrupción, y su vida de que pase á cuchillo.
kumulanditsa munthu ku manda, kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.
19 También sobre su cama es castigado con dolor fuerte en todos sus huesos,
“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake, nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,
20 Que le hace que su vida aborrezca el pan, y su alma la comida suave.
kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya, ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.
21 Su carne desfallece sin verse, y sus huesos, que antes no se veían, aparecen.
Thupi lake limawonda ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.
22 Y su alma se acerca al sepulcro, y su vida á los que causan la muerte.
Munthuyo amayandikira ku manda, moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.
23 Si tuviera cerca de él [algún] elocuente anunciador muy escogido, que anuncie al hombre su deber;
“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi, mmodzi mwa ambirimbiri oterewa, adzafotokoza zimene zili zoyenera,
24 Que le diga que [Dios] tuvo de él misericordia, que lo libró de descender al sepulcro, que halló redención:
kudzamukomera mtima ndi kunena kuti, ‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda; ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’
25 Enterneceráse su carne más que de niño, volverá á los días de su mocedad.
pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana; ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.
26 Orará á Dios, y le amará, y verá su faz con júbilo: y él restituirá al hombre su justicia.
Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa. Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.
27 El mira sobre los hombres; y [el que] dijere: Pequé, y pervertí lo recto, y no me ha aprovechado;
Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti, ‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama, koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.
28 [Dios] redimirá su alma, que no pase al sepulcro, y su vida se verá en luz.
Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda, ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’
29 He aquí, todas estas cosas hace Dios dos y tres veces con el hombre;
“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu kawirikawiri,
30 Para apartar su alma del sepulcro, y para iluminarlo con la luz de los vivientes.
kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda, kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.
31 Escucha, Job, y óyeme; calla, y yo hablaré.
“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere; khalani chete kuti ndiyankhule.
32 Que si tuvieres razones, respóndeme: habla, porque yo te quiero justificar.
Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni; yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.
33 Y si no, óyeme tú á mí; calla, y enseñarte he sabiduría.
Koma ngati sichoncho, mundimvere; khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

< Job 33 >