< Job 32 >

1 Y CESARON estos tres varones de responder á Job, por cuanto él era justo en sus ojos.
Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
2 Entonces Eliú hijo de Barachêl, Bucita, de la familia de Ram, se enojó con furor contra Job: enojóse con furor, por cuanto justificaba su vida más que á Dios.
Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
3 Enojóse asimismo con furor contra sus tres amigos, porque no hallaban qué responder, aunque habían condenado á Job.
Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
4 Y Eliú había esperado á Job en la disputa, porque eran más viejos de días que él.
Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
5 Empero viendo Eliú que no había respuesta en la boca de aquellos tres varones, su furor se encendió.
Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
6 Y respondió Eliú hijo de Barachêl, Bucita, y dijo: Yo soy menor de días, y vosotros viejos; he tenido por tanto miedo, y temido declararos mi opinión.
Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
7 Yo decía: Los días hablarán, y la muchedumbre de años declarará sabiduría.
Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
8 Ciertamente espíritu hay en el hombre, é inspiración del Omnipotente los hace que entiendan.
Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
9 No los grandes son los sabios, ni los viejos entienden el derecho.
Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
10 Por tanto yo dije: Escuchadme; declararé yo también mi sabiduría.
“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
11 He aquí yo he esperado á vuestras razones, he escuchado vuestros argumentos, en tanto que buscabais palabras.
Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
12 Os he pues prestado atención, y he aquí que no hay de vosotros quien redarguya á Job, y responda á sus razones.
ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
13 Porque no digáis: Nosotros hemos hallado sabiduría: lanzólo Dios, no el hombre.
Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
14 Ahora bien, Job no enderezó á mí sus palabras, ni yo le responderé con vuestras razones.
Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
15 Espantáronse, no respondieron más: fuéronseles los razonamientos.
“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
16 Yo pues he esperado, porque no hablaban, antes pararon, y no respondieron más.
Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
17 Por eso yo también responderé mi parte, también yo declararé mi juicio.
Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
18 Porque lleno estoy de palabras, y el espíritu de mi vientre me constriñe.
Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
19 De cierto mi vientre está como el vino que no tiene respiradero, y se rompe como odres nuevos.
mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
20 Hablaré pues y respiraré; abriré mis labios, y responderé.
Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
21 No haré ahora acepción de personas, ni usaré con hombre de lisonjeros títulos.
Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
22 Porque no sé hablar lisonjas: [de otra manera] en breve mi Hacedor me consuma.
pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”

< Job 32 >