< Job 34 >

1 ADEMÁS respondió Eliú, y dijo:
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 Oid, sabios, mis palabras; y vosotros, doctos, estadme atentos.
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 Porque el oído prueba las palabras, como el paladar gusta para comer.
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Escojamos para nosotros el juicio, conozcamos entre nosotros cuál [sea] lo bueno:
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 Porque Job ha dicho: Yo soy justo, y Dios me ha quitado mi derecho.
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 ¿He de mentir yo contra mi razón? Mi saeta es gravosa sin [haber yo] prevaricado.
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 ¿Qué hombre hay como Job, que bebe el escarnio como agua?
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 Y va en compañía con los que obran iniquidad, y anda con los hombres maliciosos.
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 Porque ha dicho: De nada servirá al hombre el conformar su voluntad con Dios.
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 Por tanto, varones de seso, oidme: Lejos esté de Dios la impiedad, y del Omnipotente la iniquidad.
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 Porque él pagará al hombre según su obra, y él le hará hallar conforme á su camino.
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Sí, por cierto, Dios no hará injusticia, y el Omnipotente no pervertirá el derecho.
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 ¿Quién visitó por él la tierra? ¿y quién puso en orden todo el mundo?
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 Si él pusiese sobre el [hombre] su corazón, y recogiese así su espíritu y su aliento,
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 Toda carne perecería juntamente, y el hombre se tornaría en polvo.
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 Si pues [hay en ti] entendimiento, oye esto: escucha la voz de mis palabras.
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 ¿Enseñorearáse el que aborrece juicio? ¿y condenarás tú al que es tan justo?
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 ¿Hase de decir al rey: Perverso; y á los príncipes: Impíos?
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 ¿[Cuánto menos á] aquel que no hace acepción de personas de príncipes, ni el rico es de él más respetado que el pobre? porque todos son obras de sus manos.
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 En un momento morirán, y á media noche se alborotarán los pueblos, y pasarán, y sin mano será quitado el poderoso.
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 Porque sus ojos están sobre los caminos del hombre, y ve todos sus pasos.
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 No hay tinieblas ni sombra de muerte donde se encubran los que obran maldad.
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 No carga pues él al hombre más [de lo justo], para que vaya con Dios á juicio.
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 El quebrantará á los fuertes sin pesquisa, y hará estar otros en su lugar.
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 Por tanto él hará notorias las obras de ellos, cuando los trastornará en la noche, y serán quebrantados.
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 Como á malos los herirá en lugar donde sean vistos:
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 Por cuanto así se apartaron de él, y no consideraron todos sus caminos;
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 Haciendo venir delante de él el clamor del pobre, y que oiga el clamor de los necesitados.
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 Y si él diere reposo, ¿quién inquietará? si escondiere el rostro, ¿quién lo mirará? [Esto] sobre una nación, y lo mismo sobre un hombre;
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 Haciendo que no reine el hombre hipócrita para vejaciones del pueblo.
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 De seguro conviene se diga á Dios: Llevado he ya [castigo], no [más] ofenderé:
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 Enséñame tú lo que yo no veo: que si hice mal, no lo haré más.
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 ¿[Ha de ser eso] según tu mente? El te retribuirá, ora rehuses, ora aceptes, y no yo: di si no, lo que tú sabes.
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 Los hombres de seso dirán conmigo, y el hombre sabio me oirá:
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 Que Job no habla con sabiduría, y que sus palabras no son con entendimiento.
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 Deseo yo que Job sea probado ampliamente, á causa de sus respuestas por los hombres inicuos.
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 Porque á su pecado añadió impiedad: bate las manos entre nosotros, y contra Dios multiplica sus palabras.
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

< Job 34 >