< Бытие 44 >

1 И заповеда Иосиф домостроителю своему, глаголя: наполните вретища мужем пищи, елико могут понести: и вложите комуждо сребро верху устия вретища:
Pambuyo pake Yosefe analamulira wantchito wa mʼnyumba mwake kuti, “Adzazire chakudya anthuwa mʼmatumba mwawo monga mmene anganyamulire, ndipo uwayikire ndalama zawo pakamwa pa matumba awowo.
2 и чашу мою сребряную вложите во вретище меншаго, и цену пшеницы его. Бысть же по словеси Иосифову, якоже рече.
Tsono uyike chikho changa cha siliva chija, pakamwa pa thumba la wamngʼono kwambiriyu pamodzi ndi ndalama zake za chakudya” Ndipo iye anachita monga Yosefe ananenera.
3 Утро возсия, и мужие отпустишася сами, и ослята их.
Mmawa kutacha anthu aja analoledwa kuti apite ndi abulu awo.
4 Изшедше же они из града, не отидоша далече: и рече Иосиф домостроителю своему: востав гони вслед мужей и постигни их, и рцы им: что яко воздасте (ми) злая за благая?
Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino?
5 Вскую украдосте чашу мою сребряну? Не сия ли есть, из неяже пиет господин мой? Он же и волхвованием волхвует в ней: злая совершисте, яже сотвористе.
Mwaberanji chikho chimene mbuye wanga amamweramo ndi kugwiritsa ntchito akafuna kuwombeza? Chimene mwachitachi ndi chinthu choyipa.’”
6 Обрет же их, рече им по словесем сим.
Wantchito uja atawapeza ananena mawu anawuzidwa aja.
7 Они же реша ему: вскую глаголет господин словеса сия? Не буди рабом твоим сотворити по словеси сему:
Koma iwo anati kwa iye, “Kodi mbuye wanga mukuneneranji zimenezi? Sizingatheke ndi pangʼono pomwe kuti antchito anufe nʼkuchita zoterozo ayi!
8 аще сребро, еже обретохом во вретищах наших, возвратихом к тебе от земли Ханаани, како быхом украли из дому господина твоего сребро или злато?
Paja ife pobwera kuchokera ku Kanaani tinatenga ndalama kubwezera zimene tinazipeza mʼmatumba mwathu. Ndiye pali chifukwa chanji kuti tikabe siliva kapena golide mʼnyumba mwa mbuye wanu?
9 У негоже аще обрящеши чашу от раб твоих, да умрет: и мы будем раби господину нашему.
Ngati wantchito wanu wina pano atapezeka nacho chikhocho, ameneyo aphedwe ndipo ena tonsefe tidzakhala akapolo anu, mbuye wathu.”
10 Он же рече: и ныне, якоже глаголете, тако будет: у негоже аще обрящется чаша, будет мой раб, вы же будете чисти.
Iye anati, “Chabwino, tsono zikhale monga mwaneneramu. Komatu aliyense amene angapezeke nacho chikhocho adzakhala kapolo wanga, ndipo ena nonsenu muzipita mwaufulu.”
11 И потщашася, и сверже кийждо вретище свое на землю, и отверзоша кийждо вретище свое.
Tsono onse anafulumira kutsitsa pansi aliyense thumba lake ndi kulitsekula.
12 Изыска же от старейшаго зачен, дондеже прииде до меншаго, и обрете чашу во вретищи Вениамини.
Kenaka anayamba kufufuza, kuyambira pa wamkulu mpaka pa wamngʼono. Ndipo chikhocho chinapezeka mʼthumba mwa Benjamini.
13 И растерзаша ризы своя, и возложиша кийждо вретище свое на осля свое, и возвратишася во град.
Apo onse anangʼamba zovala zawo ndi chisoni. Ndipo anasenzetsa abulu katundu wawo nabwerera ku mzinda konkuja.
14 Вниде же Иуда и братия его ко Иосифу, еще ему сущу ту, и падоша пред ним на землю.
Pamene Yuda ndi abale ake ankafika ku nyumba kwa Yosefe nʼkuti Yosefe akanali komweko. Ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pake.
15 Рече же им Иосиф: что дело сие сотвористе? Не ведасте ли, яко несть волхвователь человек, якоже аз?
Yosefe anafunsa kuti, “Nʼchiyani mwachitachi? Kodi simudziwa kuti munthu ngati ine ndikhoza kuona zinthu mwakuwombeza?”
16 Рече же Иуда: что отвещаем господину, или что возглаголем, или чим оправдимся? Бог же обрете неправду рабов твоих: се, мы есмы раби господину нашему, и мы, и у негоже обретеся чаша.
Yuda anayankha, “Kodi tinganenenji kwa mbuye wanga? Tinena chiyani? Tingadzilungamitse bwanji? Mulungu waulula kulakwa kwa antchito anu. Ndipo tsopano ndife akapolo a mbuye wanga, ife tonse pamodzi ndi amene wapezeka ndi chikhocho.”
17 Рече же Иосиф: не буди ми сотворити глагол сей: муж, у негоже обретеся чаша, той будет ми раб: вы же поидите в целости ко отцу своему.
Koma Yosefe anati, “Sindingachite choncho ayi! Yekhayo amene wapezeka ndi chikhocho ndi amene akhale kapolo wanga. Ena nonsenu, bwererani kwa abambo anu mu mtendere.”
18 Приступив же к нему Иуда, рече: молю тя, господине, да речет раб твой слово пред тобою, и не прогневайся на раба твоего, яко ты еси по фараоне:
Ndipo Yuda anamuyandikira iye nati, “Chonde mbuye wanga mulole kapolo wanune ndinene mawu pangʼono kwa mbuye wanga. Musandipsere mtima, kapolo wanune, popeza inu muli ngati Farao yemwe.
19 господине, ты вопрошал еси рабов твоих, глаголя: аще имате отца, или брата?
Mbuye wanga munafunsa akapolo anufe kuti, ‘Kodi muli ndi abambo anu kapena mʼbale wanu?’
20 И рехом господину: есть нам отец стар, и отрочищь на старость менший ему, а брат его умре, он же един остася у матере своея, отец же возлюби его.
Ndipo ife tinayankha, ‘Inde mbuye wathu, ife tili ndi abambo athu wokalamba, ndipo pali mwana wamwamuna wamngʼono amene anabadwa abambo athu atakalamba kale. Mʼbale wake anafa ndipo ndi yekhayo mʼmimba mwa amayi ake amene watsala ndipo abambo ake amamukonda.’
21 Ты же рекл еси рабом твоим: приведите его ко мне, да вижду его.
“Ndipo inu munatiwuza kuti, ‘Mubwere naye kwa ine kuti ndidzamuone ndekha.’
22 И рехом господину: не возможет отрочищь оставити отца своего: аще же оставит отца, умрет.
Ife tinati, ‘Mbuye wathu, mnyamatayo sangasiye abambo ake, akawasiya ndiye kuti abambo akewo adzafa.’
23 Ты же рекл еси рабом твоим: аще не приидет брат ваш менший с вами, не приложите ктому видети лица моего.
Koma inu munatichenjeza kuti, ‘Pokhapokha mutabwera naye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri, simudzandionanso.’
24 Бысть же егда приидохом к рабу твоему отцу нашему, поведахом ему словеса господина нашего,
Ndiye pamene tinafika kwa kapolo wanu, abambo athu tinawawuza zonse zimene munanena.
25 рече же нам отец наш: идите паки и купите нам мало пищи.
“Abambo athu anatiwuza kuti, ‘Pitaninso mukagule kachakudya pangʼono.’
26 Мы же рекохом: не возможем ити: но аще брат наш менший идет с нами, пойдем: ибо не возможем видети лице мужа, брату нашему меншему не сущу с нами.
Koma tinati, ‘Sitingathe kupitanso. Sitingapite pokhapokha mngʼono wathuyu apite nafe chifukwa munthu uja anati sitingaonane naye ngati mngʼono wathuyu sakhala nafe.’
27 Рече же раб твой, отец наш к нам: вы весте, яко двоих роди мне жена:
“Koma kapolo wanu, abambo athu anatiwuza kuti, ‘Inu mukudziwa kuti mkazi wanga anandiberekera ana aamuna awiri.
28 и отиде един от мене, и рекосте, яко зверем снеден бысть, и не видех его даже до ныне:
Mmodzi wa iwo anandisiya. Ine ndimati anadyedwa ndi chirombo popeza sindinamuonenso mpaka lero.
29 аще убо поймете и сего от лица моего, и случится ему зло на пути, и сведете старость мою с печалию во ад. (Sheol h7585)
Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’ (Sheol h7585)
30 Ныне убо аще пойду к рабу твоему, отцу же нашему, и отрочища не будет с нами: (душа же его связана есть с душею сего, )
“Tsono ngati tizibwerera kwa mtumiki wanu, abambo athu popanda mnyamatayu, amene moyo wa abambo ake uli pa iyeyu,
31 и будет егда увидит он не суща отрочища с нами, умрет: и сведут раби твои старость раба твоего, отца же нашего, с печалию во ад: (Sheol h7585)
ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. (Sheol h7585)
32 раб бо твой от отца взя отрочища, глаголя: аще не приведу его к тебе и поставлю его пред тобою, грешен буду ко отцу вся дни.
Ndiponsotu ine ndinadzipereka kwa abambo anga kukhala chikole chotsimikiza kuti mnyamatayu ndidzamuteteza, ndipo ndinati, ‘Ngati sindibwerera naye mnyamatayu kwa inu, ndiye kuti ndidzakhala wochimwira inu abambo anga moyo wanga wonse.’
33 Ныне убо пребуду тебе раб вместо отрочища, раб господину: отрочищь же да идет с братиею своею:
“Tsono, chonde mulole kuti ine kapolo wanu nditsalire kuno kukhala kapolo wa mbuye wathu mʼmalo mwa mnyamatayu. Koma iye apite pamodzi ndi abale akewa.
34 како бо пойду ко отцу, отрочищу не сущу с нами? Да не вижду злых, яже обрящут отца моего.
Ndingabwerere bwanji kwa abambo anga ngati sindingapite ndi mnyamatayu? Ayi! Sindifuna kukaona tsoka limene lingakagwere abambo anga.”

< Бытие 44 >