< От Матфея святое благовествование 3 >

1 Во дни же оны прииде Иоанн Креститель, проповедая в пустыни Иудейстей
Mʼmasiku amenewo, Yohane Mʼbatizi anadza nalalikira mʼchipululu cha Yudeya
2 и глаголя: покайтеся, приближибося Царствие Небесное.
kuti, “Tembenukani mtima chifukwa ufumu wakumwamba wayandikira.”
3 Сей бо есть реченный Исаием пророком, глаголющим: глас вопиющаго в пустыни: уготовайте путь Господень, правы творите стези Его.
Uyu ndi amene mneneri Yesaya ananena za iye kuti, “Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
4 Сам же Иоанн имяше ризу свою от влас велблуждь и пояс усмен о чреслех своих: снедь же его бе пружие и мед дивий.
Zovala za Yohane zinali zopangidwa ndi ubweya wa ngamira, ndipo amamangira lamba wachikopa mʼchiwuno mwake. Chakudya chake chinali dzombe ndi uchi wa kuthengo.
5 Тогда исхождаше к нему Иерусалима, и вся Иудеа, и вся страна Иорданская,
Anthu ankapita kwa iye kuchokera ku Yerusalemu ndi ku Yudeya konse ndi ku madera onse a Yorodani.
6 и крещахуся во Иордане от него, исповедающе грехи своя.
Ndipo akavomereza machimo awo ankabatizidwa mu mtsinje wa Yorodani.
7 Видев же (Иоанн) многи фарисеи и саддукеи грядущыя на крещение его, рече им: рождения ехиднова, кто сказа вам бежати от будущаго гнева?
Koma iye ataona Afarisi ndi Asaduki ambiri akubwera kumene ankabatiza, anawawuza kuti, “Ana a njoka inu! Ndani anakuchenjezani kuthawa mkwiyo umene ukubwera?
8 Сотворите убо плод достоин покаяния,
Onetsani chipatso cha kutembenuka mtima.
9 и не начинайте глаголати в себе: отца имамы Авраама: глаголю бо вам, яко может Бог от камения сего воздвигнути чада Аврааму:
Ndipo musaganize ndi kunena mwa inu nokha kuti, ‘Tili nawo abambo athu Abrahamu.’ Ndinena kwa inu kuti Mulungu akhoza kusandutsa miyala iyi kukhala ana a Abrahamu.
10 уже бо и секира при корени древа лежит: всяко убо древо, еже не творит плода добра, посекаемо бывает и во огнь вметаемо:
Tikukamba pano nkhwangwa yayikidwa kale pa mizu ya mitengo, ndipo mtengo umene subala chipatso chabwino udulidwa ndi kuponyedwa pa moto.
11 аз убо крещаю вы водою в покаяние: Грядый же по мне креплий мене есть, Емуже несмь достоин сапоги понести: Той вы крестит Духом Святым и огнем:
“Ine ndikubatizani ndi madzi kusonyeza kutembenuka mtima. Koma pambuyo panga akubwera wina amene ali ndi mphamvu kuposa ine, amene sindiyenera kunyamula nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani ndi Mzimu Woyera ndi moto.
12 емуже лопата в руце Его, и отребит гумно Свое, и соберет пшеницу Свою в житницу, плевы же сожжет огнем негасающим.
Mʼdzanja lake muli chopetera ndipo adzayeretsa popunthirapo pake nadzathira tirigu wake mʼnkhokwe ndi kutentha zotsalira zonse ndi moto wosazima.”
13 Тогда приходит Иисус от Галилеи на Иордан ко Иоанну креститися от него.
Pamenepo Yesu anabwera kuchokera ku Galileya kudzabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
14 Иоанн же возбраняше Ему, глаголя: аз требую Тобою креститися, и Ты ли грядеши ко мне?
Koma Yohane anayesetsa kumukanira nati, “Ndiyenera kubatizidwa ndi Inu, bwanji Inu mubwera kwa ine?”
15 Отвещав же Иисус рече к нему: остави ныне: тако бо подобает нам исполнити всяку правду. Тогда остави Его.
Yesu anayankha kuti, “Zibatero tsopano, ndi koyenera kwa ife kuchita zimenezi kukwaniritsa chilungamo chonse.” Ndipo Yohane anavomera.
16 И крестився Иисус взыде абие от воды: и се, отверзошася Ему небеса, и виде Духа Божия сходяща яко голубя и грядуща на Него.
Yesu atangobatizidwa, nthawi yomweyo potuluka mʼmadzi, kumwamba kunatsekuka ndipo taonani, Mzimu wa Mulungu anatsika ngati nkhunda natera pa Iye.
17 И се, глас с небесе глаголя: Сей есть Сын Мой возлюбленный, о Немже благоволих.
Ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Uyu ndiye mwana wanga wokondedwa amene ndikondwera naye.”

< От Матфея святое благовествование 3 >