< Књига пророка Амоса 2 >

1 Овако вели Господ: За три зла и за четири што учини Моав, нећу му опростити, јер сажеже кости цара едомског у креч.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Mowabu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu, mpaka kuwasandutsa phulusa,
2 Него ћу пустити огањ на Моава, те ће прождрети дворове у Кариоту, и Моав ће погинути с вревом, с виком и с гласом трубним.
Ine ndidzatumiza moto pa Mowabu, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Keriyoti. Mowabu adzafera pakati pa nkhondo yoopsa, mʼkati mwa mfuwu wa nkhondo ndi kuliza malipenga.
3 И истребићу судију из њега и све кнезове његове побићу с њим, вели Господ.
Ndidzawononga wolamulira wake ndi kupha akuluakulu onse amene ali pamodzi ndi iye,” akutero Yehova.
4 Овако вели Господ: За три зла и за четири што учини Јуда, нећу му опростити, јер презреше закон Господњи и уредбе Његове не држаше, и преварише се лажима својим, за којима ходише оци њихови.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Yuda akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo akana lamulo la Yehova ndipo sanasunge malangizo ake, popeza asocheretsedwa ndi milungu yabodza, milungu imene makolo awo ankayitsatira,
5 Него ћу пустити огањ у Јуду, те ће прождрети дворе јерусалимске.
Ine ndidzatumiza moto pa Yuda, umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu.”
6 Овако вели Господ: За три зла и за четири што учини Израиљ, нећу му опростити, јер продаваше праведника за новце и убогог за једне опанке.
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Israeli akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Iwo amagulitsa anthu olungama ndi siliva, ndi osauka ndi nsapato.
7 Чезну за прахом земаљским на глави сиромасима, и превраћају пут смернима; и син и отац одлазе к једној девојци да скврне свето име моје.
Amapondereza anthu osauka ngati akuponda fumbi, ndipo sawaweruza mwachilungamo anthu oponderezedwa. Abambo ndi mwana wawo amagonana ndi mtsikana mmodzi yemweyo, ndipo potero amanyozetsa dzina langa loyera.
8 И на хаљинама у залогу узетим леже код сваког олтара, и вино оглобљених пију у кући богова својих.
Anthuwo amakagonana mʼmbali mwa guwa lililonse la nsembe pa zovala zimene anatenga ngati chikole. Mʼnyumba ya mulungu wawo amamweramo vinyo amene analipiritsa anthu pa milandu.
9 А ја истребих испред њих Амореје, који беху високи као кедри и јаки као храстови, и потрх род њихов озго и жиле њихове оздо.
“Ine ndinawononga Aamori pamaso pawo, ngakhale iwo anali anthu ataliatali ngati mikungudza ndiponso amphamvu ngati mitengo ya thundu. Ndinawononga zipatso zawo ndiponso mizu yawo.
10 И ја вас изведох из земље мисирске, и водих вас по пустињи четрдесет година да бисте наследили земљу аморејску.
“Ine ndinakutulutsani ku Igupto, ndipo ndinakutsogolerani mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kudzakupatsani dziko la Aamori.
11 И подизах између синова ваших пророке и између младића ваших назиреје. Није ли тако? Синови Израиљеви, говори Господ.
Ine ndinawutsanso ena mwa ana ako kuti akhale aneneri, ndi ena mwa anyamata ako kuti akhale anaziri. Kodi si choncho, inu Aisraeli?” akutero Yehova.
12 А ви појисте назиреје вином, и пророцима забрањивасте говорећи: Не пророкујте.
“Koma inu munawamwetsa vinyo anaziri aja, ndipo munalamula aneneri kuti asanenere.
13 Ево, ја ћу вас притиснути на месту вашем као што се притискају кола пуна снопља.
“Tsono Ine ndidzakupsinjani monga imapsinjikira ngolo imene yadzaza ndi tirigu.
14 И неће бити бега брзоме, и јаки неће утврдити крепости своје, и храбри неће спасти душу своје.
Munthu waliwiro sadzatha kuthawa, munthu wamphamvu sadzakhalanso ndi nyonga, wankhondo sadzapulumutsa moyo wake.
15 И стрелац неће се одржати, и лаки на ногу неће се избавити, нити ће коњаник спасти душе своје.
Munthu wa uta sadzalimbika, msilikali wothamanga kwambiri sadzapulumuka, ndipo wokwera pa akavalo sadzapulumutsa moyo wake.
16 Него ће најхрабрији међу јунацима го побећи у онај дан, говори Господ.
Ngakhale asilikali olimba mtima kwambiri adzathawa ali maliseche pa tsikulo,” akutero Yehova.

< Књига пророка Амоса 2 >