< Књига пророка Авдије 1 >

1 Утвара Авдијева. Овако вели Господ Господ за едомску: Чусмо глас од Господа, и гласник би послан к народима: Устајте, да устанемо на њу у бој.
Masomphenya a Obadiya. Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti, Tamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti, “Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
2 Гле, учинићу те малим међу народима, бићеш врло презрен.
“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina; udzanyozedwa kwambiri.
3 Понос срца твог превари те, тебе, који живиш у раселинама каменим, у високом стану свом, и говориш у срцу свом: Ко ће ме оборити на земљу?
Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali, iwe amene umanena mu mtima mwako kuti, ‘Ndani anganditsitse pansi?’
4 Да подигнеш високо као орао и међу звезде да метнеш гнездо своје, оданде ћу те оборити, говори Господ.
Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
5 Како си оплењен?! Да су дошли к теби крадљивци или лупежи ноћу, не би ли покрали колико им је доста? Да су дошли к теби берачи виноградски, не би ли оставили пабирака?
“Anthu akuba akanabwera kwa iwe, kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku, aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe! Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha? Ngati anthu othyola mphesa akanafika, kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
6 Како се претражи Исав, како се нађоше потаје његове!
Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa!
7 До границе те одведоше сви који беху с тобом у вери, преварише те и надвладаше те који беху у миру с тобом; који једу хлеб твој подметнуше ти замку, да се не опази.
Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire; abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa; amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha, koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
8 У онај дан, говори Господ, нећу ли погубити мудре у земљи едемској и разумне у гори Исавовој?
Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo, kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu, anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
9 И твоји ће се јунаци уплашити, Темане, да се истребе покољем сви из горе Исавове.
Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha, ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau adzaphedwa pa nkhondo.
10 За насиље учињено брату твом Јакову покриће те стид и истребићеш се засвагда.
Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo, udzakhala wamanyazi; adzakuwononga mpaka muyaya.
11 Онај дан, кад ти стајаше насупрот; онај дан, кад иностранци одвођаху у ропство војску његову, и туђинци улажаху на врата његова и бацаху жреб за Јерусалим, беше и ти као који од њих.
Pamene adani ankamulanda chuma chake pamene alendo analowa pa zipata zake ndi kuchita maere pa Yerusalemu, pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
12 Али ти не требаше гледати дана брата свог, дана, кад се одвођаше у туђу земљу, нити се радовати синовима Јудиним у дан кад пропадаху, нити разваљивати уста у дан невоље њихове.
Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako pa nthawi ya tsoka lake, kapena kunyogodola Ayuda chifukwa cha chiwonongeko chawo, kapena kuwaseka pa nthawi ya mavuto awo.
13 Не требаше ти ући на врата народа мог у дан погибли њихове, не требаше да и ти гледаш зло њихово у дан погибли њихове, ни да се дохваташ добра њихова у дан погибли њихове.
Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga pa nthawi ya masautso awo, kapena kuwanyogodola pa tsiku la tsoka lawo, kapena kulanda chuma chawo pa nthawi ya masautso awo.
14 Нити требаше да станеш на распутицу да убијаш бежан њихову, нити да издајеш оних који осташе у дан невоље.
Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu kuti uphe Ayuda othawa, kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka pa nthawi ya mavuto awo.”
15 Јер је дан Господњи близу свим народима: како си чинио, тако ће ти бити, плата ће ти се вратити на главу твоју.
“Tsiku la Yehova layandikira limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu. Adzakuchitira zomwe unawachitira ena; zochita zako zidzakubwerera wekha.
16 Јер као што сте ви пили на светој гори мојој, тако ће пити сви народи вазда, пиће, и ждреће, и биће као да их није било.
Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
17 А на гори ће Сиону бити спасење, и биће света, и дом ће Јаковљев наследити наследство своје.
Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso; phirilo lidzakhala lopatulika, ndipo nyumba ya Yakobo idzalandira cholowa chake.
18 И дом ће Јаковљев бити огањ и дом Јосифов пламен, а дом Исавов стрњика; и разгореће се на њих, и спалиће их; и неће бити остатака дому Исавовом, јер Господ рече.
Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.
19 И наследиће југ, гору Исавову, и равницу, Филистеје; и наследиће поље Јефремово и поље самаријско и Венијаминово и Галад;
Anthu ochokera ku Negevi adzakhala ku mapiri a Esau, ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri adzatenga dziko la Afilisti. Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya, ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
20 И заробљена војска синова Израиљевих наследиће шта је било хананејско до Сарепте; а робље јерусалимско, што је у Сефараду, наследиће јужне градове.
Aisraeli amene ali ku ukapolo adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati; a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi adzalandira mizinda ya ku Negevi.
21 И избавитељи ће изаћи на гору Сион да суде гори Исавовој, и царство ће бити Господње.
Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni ndipo adzalamulira mapiri a Esau. Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.

< Књига пророка Авдије 1 >