< 1-е Коринфянам 11 >

1 Будьте подражателями мне, как я Христу.
Tsatirani chitsanzo changa, monga inenso nditsatira chitsanzo cha Khristu.
2 Хвалю вас, братия, что вы все мое помните и держите предания так, как я передал вам.
Ndikukuyamikani chifukwa chondikumbukira pa zonse ndiponso posunga ziphunzitso monga ndinakuphunzitsirani.
3 Хочу также, чтобы вы знали, что всякому мужу Глава Христос, жене Глава - муж, а Христу Глава - Бог.
Tsopano ndikufuna muzindikire kuti Khristu ndiye mutu wa munthu aliyense, ndipo mwamuna ndiye mutu wamkazi, ndipo mutu wa Khristu ndi Mulungu.
4 Всякий муж, молящийся или пророчествующий с покрытою головою, постыжает свою голову.
Mwamuna aliyense wopemphera kapena kunenera ataphimba mutu wake akunyoza mutu wakewo.
5 И всякая жена, молящаяся или пророчествующая с открытою головою, постыжает свою голову, ибо это то же, как если бы она была обритая.
Ndipo mkazi aliyense wopemphera kapena kunenera asanaphimbe mutu wake sakulemekeza mutu wakewo. Kuli chimodzimodzi kumeta mutu wake.
6 Ибо если жена не хочет покрываться, то пусть и стрижется; а если жене стыдно быть остриженной или обритой, пусть покрывается.
Ngati mkazi saphimba kumutu kwake, ndiye kuti amete tsitsi lake. Ngati nʼchamanyazi kwa mkazi kungoyepula kapena kumeta mpala, ndiye kuti aphimbe kumutu kwake.
7 Итак муж не должен покрывать голову, потому что он есть образ и слава Божия; а жена есть слава мужа.
Mwamuna sayenera kuphimba kumutu popeza ndi chifaniziro ndi ulemerero wa Mulungu; pamene mkazi ndi ulemerero wa mwamuna.
8 Ибо не муж от жены, но жена от мужа;
Pakuti mwamuna sachokera kwa mkazi, koma mkazi kwa mwamuna.
9 и не муж создан для жены, но жена для мужа.
Ndipo mwamuna sanalengedwe chifukwa cha mkazi, koma mkazi analengedwera mwamuna.
10 Посему жена и должна иметь на голове своей знак власти над нею, для Ангелов.
Pa chifukwa ichi, ndiponso pa chifukwa cha angelo, mkazi akuyenera kukhala ndi chizindikiro cha ulamuliro wake.
11 Впрочем, ни муж без жены, ни жена без мужа, в Господе.
Komabe mwa Ambuye, mkazi amadalira mwamuna ndipo mwamuna amadalira mkazi.
12 Ибо как жена от мужа, так и муж через жену; все же - от Бога.
Pakuti monga mkazi anachokera kwa mwamuna, momwemonso mwamuna anabadwa mwa mkazi. Koma zonse zichokera kwa Mulungu.
13 Рассудите сами, прилично ли жене молиться Богу с непокрытою головою?
Dziweruzeni. Kodi nʼchabwino kuti mkazi apemphere kwa Mulungu wopanda chophimba kumutu?
14 Не сама ли природа учит вас, что если муж растит волосы, то это бесчестье для него,
Kodi chikhalidwe chathu sichitiphunzitsa kuti nʼchamanyazi kuti mwamuna akhale ndi tsitsi lalitali,
15 но если жена растит волосы, для нее это честь, так как волосы даны ей вместо покрывала?
koma mkazi akakhala ndi tsitsi lalitali ndi ulemerero wake? Pakuti mkazi anapatsidwa tsitsi lalitali monga chophimba kumutu.
16 А если бы кто захотел спорить, то мы не имеем такого обычая, ни церкви Божии.
Ngati wina akufuna kutsutsapo pa zimenezi, ife ndiponso mipingo ya Mulungu tilibe machitidwe ena apadera koma ndi omwewa.
17 Но, предлагая сие, не хвалю вас, что вы собираетесь не на лучшее, а на худшее.
Koma popereka malangizo awa sindikufuna kukuyamikirani popeza mʼmisonkhano yanu mumachita zoyipa kuposa zabwino.
18 Ибо, во-первых, слышу, что, когда вы собираетесь в церковь, между вами бывают разделения, чему отчасти и верю.
Choyamba, ndikumva kuti mukasonkhana mu mpingo mumasankhana ndipo ndikukhulupirira kuti zimenezi kwinaku nʼzoona.
19 Ибо надлежит быть и разномыслиям между вами, дабы открылись между вами искусные.
Nʼzosakayikitsa kuti pali kugawikana pakati panu kuti adziwike amene ndi ovomerezeka ndi Mulungu.
20 Далее, вы собираетесь, так, что это не значит вкушать вечерю Господню;
Tsono, mukasonkhana pamodzi, chimene mumadya si Mgonero wa Ambuye.
21 ибо всякий поспешает прежде других есть свою пищу, так что иной бывает голоден, а иной упивается.
Pakuti mukamadya, aliyense amangodzidyera zomwe anakonza. Wina amakhala ndi njala pamene wina amaledzera.
22 Разве у вас нет домов на то, чтобы есть и пить? Или пренебрегаете церковь Божию и унижаете неимущих? Что сказать вам? Похвалить ли вас за это? Не похвалю.
Kodi mulibe nyumba zanu kumene mungamadyere ndi kumwa? Kapena mumapeputsa mpingo wa Mulungu ndi kuchititsa manyazi amene alibe kalikonse? Ndikunena chiyani kwa inu? Moti ndikuyamikireni pa zimenezi? Ayi, pa zinthu izi sindingakuyamikireni.
23 Ибо я от Самого Господа принял то, что и вам передал, что Господь Иисус в ту ночь, в которую предан был, взял хлеб
Pakuti zimene ndinalandira kwa Ambuye ndi zomwe ndinakupatsani. Ambuye Yesu, usiku umene anaperekedwa uja, anatenga buledi.
24 и, возблагодарив, преломил и сказал: приимите, ядите, сие есть Тело Мое, за вас ломимое; сие творите в Мое воспоминание.
Atayamika ndi kumunyema ananena kuti, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.”
25 Также и чашу после вечери, и сказал: сия чаша есть новый завет в Моей Крови; сие творите, когда только будете пить, в Мое воспоминание.
Chimodzimodzi, atatha kudya, anatenga chikho, nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga; imwani nthawi zonse pokumbukira Ine.”
26 Ибо всякий раз, когда вы едите хлеб сей и пьете чашу сию, смерть Господню возвещаете, доколе Он придет.
Pakuti nthawi zonse pamene mudya bulediyu ndikumwa chikhochi, mukulalikira imfa ya Ambuye mpaka Iye adzabweranso.
27 Посему кто будет есть хлеб сей или пить чашу Господню недостойно, виновен будет против Тела и Крови Господней.
Chifukwa chake, aliyense amene adya buledi kapena kumwa chikho cha Ambuye mʼnjira yosayenera adzachimwira thupi ndi magazi a Ambuye.
28 Да испытывает же себя человек, и таким образом пусть ест от хлеба сего и пьет из чаши сей.
Munthu adzisanthule yekha asanadye buledi kapena kumwa chikhochi.
29 Ибо кто ест и пьет недостойно, тот ест и пьет B осуждение себе, не рассуждая о Теле Господнем.
Popeza aliyense amene adya kapena kumwa mosazindikira thupi la Ambuye, amadya ndi kumwa chiweruzo chake chomwe.
30 Оттого многие из вас немощны и больны и немало умирает.
Nʼchifukwa chake pakati panu ambiri mwa inu ndi ofowoka ndi odwala, ndipo ambirinso agona tulo.
31 Ибо если бы мы судили сами себя, то не были бы судимы.
Koma tikanadziyesa tokha sitikaweruzidwanso.
32 Будучи же судимы, наказываемся от Господа, чтобы не быть осужденными с миром.
Pamene tiweruzidwa ndi Ambuye, ndiye kuti akukonza khalidwe lathu kupewa kuti tingatsutsidwe pamodzi ndi anthu osakhulupirira.
33 Посему, братия мои, собираясь на вечерю, друг друга ждите.
Ndiye tsono abale anga, pamene musonkhana pa chakudya, mudikirirane.
34 А если кто голоден, пусть ест дома, чтобы собираться вам не на осуждение. Прочее устрою, когда приду.
Ngati wina ali ndi njala, adye ku nyumba kwake kuti pamene musonkhana pamodzi zisafike poti muweruzidwe nazo. Ndipo ndikabwera ndidzakupatsani malangizo ena owonjezera.

< 1-е Коринфянам 11 >