< 1-е Коринфянам 12 >

1 Не хочу оставить вас, братия, в неведении и о дарах духовных.
Tsopano abale anga okondedwa, sindikufuna mukhale osadziwa za mphatso za Mzimu.
2 Знаете, что когда вы были язычниками, то ходили к безгласным идолам, так, как бы вели вас.
Inu mukudziwa kuti pamene munali akunja, ankakusocheretsani mʼnjira zosiyanasiyana ndi kukukokerani ku mafano osayankhula.
3 Потому сказываю вам, что никто, говорящий Духом Божиим, не произнесет анафемы на Иисуса и никто не может назвать Иисуса Господом, как только Духом Святым.
Nʼchifukwa chake ndikuwuzani kuti palibe munthu amene ali ndi Mzimu wa Mulungu angayankhule kuti, “Yesu atembereredwe,” ndiponso palibe munthu anganene kuti “Yesu ndi Ambuye,” popanda kutsogozedwa ndi Mzimu Woyera.
4 Дары различны, но Дух один и тот же;
Pali mphatso zosiyanasiyana, koma Mzimu yemweyo.
5 и служения различны, а Господь один и тот же;
Pali mautumiki osiyanasiyana koma Ambuye yemweyo.
6 и действия различны, а Бог один и тот же, производящий все во всех.
Pali magwiridwe antchito osiyanasiyana, koma Mulungu yemweyo amagwira ntchito monsemo mwa anthu onse.
7 Но каждому дается проявление Духа на пользу.
Tsono Mzimu amapereka mphatso kwa aliyense kuti ipindulire onse.
8 Одному дается Духом слово мудрости, другому слово знания, тем же Духом;
Mzimu amapereka kwa munthu wina mawu anzeru, Mzimu yemweyonso amapereka kwa wina mawu achidziwitso.
9 иному вера, тем же Духом; иному дары исцелений, тем же Духом;
Kwa wina, Mzimu yemweyo amapereka chikhulupiriro, kwa wina mphatso zamachiritso, Mzimu yemweyo.
10 иному чудотворения, иному пророчество, иному различение духов, иному разные языки, иному истолкование языков.
Kwa wina mphamvu zochita zodabwitsa, kwa wina mawu a uneneri, kwa wina mphatso yozindikira mizimu, kwa wina malilime osiyanasiyana, ndiponso kwa wina kutanthauzira malilimewo.
11 Все же сие производит один и тот же Дух, разделяя каждому особо, как Ему угодно.
Zonsezi ndi ntchito za Mzimu mmodzi yemweyo, ndipo amapereka kwa munthu aliyense monga momwe Mzimuyo wafunira.
12 Ибо, как тело одно, но имеет многие члены, и все члены одного тела, хотя их и много, составляют одно тело, - так и Христос.
Thupi ndi limodzi, ngakhale kuti lapangidwa ndi ziwalo zambiri. Ndipo ngakhale ziwalo zake zonse ndi zambiri, zimapanga thupi limodzi. Momwemonso ndi mmene alili Khristu.
13 Ибо все мы одним Духом крестились в одно тело, Иудеи или Еллины, рабы или свободные, и все напоены одним Духом.
Pakuti tonse tinabatizidwa ndi Mzimu mmodzi mʼthupi limodzi. Myuda kapena Mgriki, kapolo kapena mfulu tonse tinapatsidwa kuti timwe Mzimu mmodzi yemweyo.
14 Тело же не из одного члена, но из многих.
Tsopano thupi silinapangidwe ndi chiwalo chimodzi koma ndi ziwalo zambiri.
15 Если нога скажет: я не принадлежу к телу, потому что я не рука, то неужели она потому не принадлежит к телу?
Ngati phazi litanena kuti, “Pakuti sindine dzanja, sindine chiwalo cha thupi.” Chifukwa chimenechi sichingachititse phazi kuti lisakhale chiwalo cha thupi.
16 И если ухо скажет: я не принадлежу к телу, потому что я не глаз, то неужели оно потому не принадлежит к телу?
Ndipo ngati khutu litanena kuti, “Pakuti sindine diso, sindine chiwalo cha thupi.” Chifukwa chimenechi sichingachititse khutu kuti lisakhale chiwalo cha thupi.
17 Если все тело глаз, то где слух? Если все слух, то где обоняние?
Kodi thupi lonse likanakhala diso, tikanamamva bwanji? Nanga thupi lonse likanakhala khutu, tikanamanunkhiza bwanji?
18 Но Бог расположил члены, каждый в составе тела, как Ему было угодно.
Koma zoona nʼzakuti, Mulungu anayika ziwalo mʼthupi, chilichonse monga momwe Iye anafunira.
19 А если бы все были один член, то где было бы тело?
Nanga zonse zikanakhala chiwalo chimodzi, ndiye thupi likanakhala lotani?
20 Но теперь членов много, а тело одно.
Mmene zililimu, pali ziwalo zambiri koma thupi ndi limodzi lokha.
21 Не может глаз сказать руке: ты мне не надобна; или также голова ногам: вы мне не нужны.
Diso silingawuze dzanja kuti, “Iwe sindikukufuna!” Ndipo mutu sungawuze phazi kuti “Iwe sindikukufuna!”
22 Напротив, члены тела, которые кажутся слабейшими, гораздо нужнее,
Mʼmalo mwake, ziwalo zathupi zimene zimaoneka ngati zofowoka ndizo zili zofunikira kwambiri,
23 и которые нам кажутся менее благородными в теле, о тех более прилагаем попечения;
ndipo ziwalo zathupi zimene timaziyesa zopanda ulemu, ndizo timazilemekeza kwambiri. Ndipo ziwalo zosaoneka bwino ndizo zimalandira ulemu wapadera.
24 и неблагообразные наши более благовидно покрываются, а благообразные наши не имеют в том нужды. Но Бог соразмерил тело, внушив о менее совершенном большее попечение,
Koma ziwalo zooneka bwino, nʼkosafunika kuti tizisamalire mwapadera. Mulungu polumikiza ziwalo zathupi, anapereka ulemu wopambana kwa ziwalo zimene zimafunadi ulemuwo
25 дабы не было разделения в теле, а все члены одинаково заботились друг о друге.
kuti pasakhale kugawikana mʼthupi koma kuti ziwalo zonse zisamalirane.
26 Посему страдает ли один член, страдают с ним все члены; славится ли один член, с ним радуются все члены.
Ngati chiwalo chimodzi chikumva kuwawa, ziwalo zonse zimamvanso kuwawa. Ngati chiwalo chimodzi chilandira ulemu, ziwalo zonse zimakondwera nawo.
27 И вы - тело Христово, а порознь - члены.
Tsopano inu ndinu thupi la Khristu, ndipo aliyense wa inu ndi chiwalo cha thupilo.
28 И иных Бог поставил в Церкви, во-первых, Апостолами, во-вторых, пророками, в-третьих, учителями; далее, иным дал силы чудодейственные, также дары исцелений, вспоможения, управления, разные языки.
Ndipo Mulungu mu mpingo anayika poyamba atumwi, kachiwiri aneneri, kachitatu aphunzitsi, kenaka ochita zozizwitsa, ena a mphatso zamachiritso, ena a mphatso yothandiza anzawo, ena a mphatso yotsogolera ndiponso ena a mphatso ya malilime.
29 Все ли Апостолы? Все ли пророки? Все ли учители? Все ли чудотворцы?
Kodi onse ndi atumwi? Kodi onse ndi aneneri? Kodi onse ndi aphunzitsi? Kodi onse amachita zozizwitsa?
30 Все ли имеют дары исцелений? Все ли говорят языками? Все ли истолкователи?
Kodi onse ali ndi mphatso zamachiritso? Kodi onse amayankhula malilime? Kodi onse amatanthauzira malilime?
31 Ревнуйте о дарах больших, и я покажу вам путь еще превосходнейший.
Koma funitsitsani mphatso zopambana. Tsopano ndikuonetsani njira yopambana kwambiri.

< 1-е Коринфянам 12 >