< 1-е Коринфянам 10 >

1 Не хочу оставить вас, братия, в неведении, что отцы наши все были под облаком, и все прошли сквозь море;
Pakuti sindikufuna kuti inu mukhale osadziwa zenizeni, abale, kuti makolo athu anatsogozedwa ndi mtambo ndikuti onse anawoloka nyanja.
2 и все крестились в Моисея в облаке и в море;
Ndipo onse anabatizidwa mwa Mose mu mtambo ndi mʼnyanja.
3 и все ели одну и ту же духовную пищу;
Onse anadya chakudya chimodzi chauzimu
4 и все пили одно и то же духовное питие: ибо пили из духовного последующего камня; камень же был Христос.
ndipo anamwa chakumwa chimodzi chauzimu; popeza anamwa kuchokera mʼthanthwe lomwe anayenda nalo, ndipo thanthwe limeneli linali Khristu.
5 Но не о многих из них благоволил Бог, ибо они поражены были в пустыне.
Ngakhale zinali choncho, Mulungu sanakondwere ndi ambiri a iwo, motero ambiri mwa iwo anafera mʼchipululu.
6 А это были образы для нас, чтобы мы не были похотливы на злое, как они были похотливы.
Tsono zinthu izi zinachitika kuti zikhale chitsanzo, kuti ife tisayike mitima yathu pa zinthu zoyipa monga anachitira makolo athuwo.
7 Не будьте также идолопоклонниками, как некоторые из них, о которых написано: народ сел есть и пить, и встал играть.
Musakhale anthu opembedza mafano, monga analili ena mwa iwo. Pakuti zalembedwa kuti, “Anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.”
8 Не станем блудодействовать, как некоторые из них блудодействовали, и в один день погибло их двадцать три тысячи.
Tisachite chigololo monga ena mwa iwo anachitira ndipo tsiku limodzi anafapo anthu 23,000.
9 Не станем искушать Христа, как некоторые из них искушали и погибли от змей.
Tisamuyese Khristu, monga ena mwa iwo anachitira ndipo anaphedwa ndi njoka.
10 Не ропщите, как некоторые из них роптали и погибли от истребителя.
Ndipo osamawiringula, monga ena mwa iwo anachitira naphedwa ndi mngelo wowononga.
11 Все это происходило с ними, как образы; а описано в наставление нам, достигшим последних веков. (aiōn g165)
Zinthu izi zinawachitikira kuti zikhale chitsanzo ndipo zinalembedwa kuti zikhale chenjezo kwa ife, amene tiyandikira nthawi ya kutha kwa zonse. (aiōn g165)
12 Посему кто думает, что он стоит, берегись, чтобы не упасть.
Choncho, ngati mukuganiza kuti mwayima mwamphamvu, samalani mungagwe!
13 Вас постигло искушение не иное, как человеческое; и верен Бог, Который не попустит вам быть искушаемыми сверх сил, но при искушении даст и облегчение, так чтобы вы могли перенести.
Palibe mayesero amene mwakumana nawo oposa amene anthu ena onse anakumana nawo. Mulungu ngokhulupirika; sadzalola kuti inu muyesedwe koposa muyeso umene mutha kupirira. Koma pamene mwayesedwa, Iyenso adzakupatsani njira yopambanira mayeserowo.
14 Итак, возлюбленные мои, убегайте идолослужения.
Choncho abwenzi anga okondedwa, lekani kupembedza mafano.
15 Я говорю вам как рассудительным; сами рассудите о том, что говорю.
Ndikuyankhula kwa a anthu anzeru zawo, nokha muweruze pa zimene ndikunenazi.
16 Чаша благословения, которую благословляем, не есть ли приобщение Крови Христовой? Хлеб, который преломляем, не есть ли приобщение Тела Христова?
Pamene tidalitsa chikho cha Mgonero wa Ambuye, mothokoza Mulungu, kodi sitikugawana magazi a Khristu? Nanga buledi amene timanyemayo, kodi sitikugawana thupi la Khristu?
17 Один хлеб, и мы многие одно тело; ибо все причащаемся от одного хлеба.
Pakuti buledi ndi mmodzi yekha, ifenso ngakhale tili ambiri, ndife thupi limodzi, popeza tonse timagawana buledi mmodzi yemweyo.
18 Посмотрите на Израиля по плоти: те, которые едят жертвы, не участники ли жертвенника?
Taganizirani zimene amachita Aisraeli. Kodi onse amene amadya zoperekedwa nsembe, samachita nawo miyambo ya pa guwapo?
19 Что же я говорю? То ли, что идол есть что-нибудь или идоложертвенное значит что-нибудь?
Kodi ndikutanthauza kuti nsembe zoperekedwa kwa mafano ndi kanthu konse, kapena kuti mafano ndi kanthu konse?
20 Нет, но что язычники, принося жертвы, приносят бесам, а не Богу. Но я не хочу, чтобы вы были в общении с бесами.
Ayi. Nsembe za osakhulupirira zimaperekedwa kwa ziwanda, osati kwa Mulungu, ndipo sindikufuna kuti muziyanjana ndi ziwandazo.
21 Не можете пить чашу Господню и чашу бесовскую; не можете быть участниками в трапезе Господней и в трапезе бесовской.
Simungamwe chikho cha Ambuye, ndi kukamweranso chikho cha ziwanda. Simungadyere pa tebulo la Ambuye ndiponso la ziwanda.
22 Неужели мы решимся раздражать Господа? Разве мы сильнее Его?
Kodi tikufuna kuwutsa mkwiyo wa Ambuye? Kodi ndife amphamvu kuposa Iye?
23 Все мне позволительно, но не все полезно; все мне позволительно, но не все назидает.
Mutha kunena kuti, “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zili za phindu. “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zimathandiza.
24 Никто не ищи своего, но каждый пользы другого.
Munthu aliyense asafunefune zokomera iye yekha, koma zokomeranso ena.
25 Все, что продается на торгу, ешьте без всякого исследования, для спокойствия совести;
Idyani nyama iliyonse imene amagulitsa pa msika, osafunsa mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu.
26 ибо Господня земля и что наполняет ее.
Popeza kuti, “Dziko lapansi ndi la Ambuye ndi zonse za mʼmenemo ndi zake.”
27 Если кто из неверных позовет вас, и вы захотите пойти, то все, предлагаемое вам, ешьте без всякого исследования, для спокойствия совести.
Ngati wosakhulupirira akuyitanani kuti mukadye naye, inuyo ndi kuvomera kupitako, mukadye chilichonse chimene akakupatseni ndipo musakafunse mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu.
28 Но если кто скажет вам: это идоложертвенное - то не ешьте ради того, кто объявил вам, и ради совести. Ибо Господня земля и что наполняет ее.
Koma ngati wina akuwuzani kuti, “Izi zaperekedwa nsembe,” musadye zimenezo, pofuna kuthandiza amene wakuwuzaniyo komanso chifukwa cha chikumbumtima.
29 Совесть же разумею не свою, а другого: ибо для чего моей свободе быть судимой чужою совестью?
Ndikunena za chikumbumtima cha winayo osati chanu. Tsono mungafunse kuti, nʼchifukwa chiyani ufulu wanga ukuphwanyidwa chifukwa cha chikumbumtima cha munthu wina?
30 Если я с благодарением принимаю пищу, то для чего порицать меня за то, за что я благодарю?
Ngati ndikuyamika Mulungu chifukwa cha chakudya, nanga munthu angandinyoze bwanji pa zinthu zomwe ndayamikira nazo Mulungu?
31 Итак, едите ли, пьете ли или иное что делаете, все делайте в славу Божию.
Nʼchifukwa chake chilichonse mungadye kapena kumwa, kapena chimene mungachite, chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu.
32 Не подавайте соблазна ни Иудеям, ни Еллинам, ни церкви Божией,
Musakhumudwitse aliyense, kaya ndi Myuda, Mgriki, kapena mpingo wa Mulungu.
33 так, как и я угождаю всем во всем, ища не своей пользы, но пользы многих, чтобы они спаслись.
Mu zonse ndikuyesetsa kukondweretsa aliyense mʼnjira iliyonse. Popeza sindikufunafuna zokondweretsa ine ndekha koma zokomera ambiri kuti apulumutsidwe.

< 1-е Коринфянам 10 >