< Luc 3 >

1 Or en la quinzième année de l'empire de Tibère César, lorsque Ponce Pilate était Gouverneur de la Judée, et qu'Hérode était Tétrarque en Galilée, et son frère Philippe Tétrarque dans la contrée d'Iturée et de Trachonite, et Lysanias Tétrarque en Abilène;
Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
2 Anne et Caïphe étant souverains Sacrificateurs, la parole de Dieu fut adressée à Jean fils de Zacharie, au désert.
Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
3 Et il vint dans tout le pays des environs du Jourdain, prêchant le Baptême de repentance, pour la rémission des péchés;
Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
4 Comme il est écrit au Livre des paroles d'Esaïe le Prophète, disant: la voix de celui qui crie dans le désert, est: Préparez le chemin du Seigneur, aplanissez ses sentiers.
Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
5 Toute vallée sera comblée, et toute montagne et toute colline sera abaissée, et les choses tortues seront redressées, et les chemins raboteux seront aplanis;
Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
6 Et toute chair verra le salut de Dieu.
Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
7 Il disait donc à la foule de ceux qui venaient pour être baptisés par lui: Race de vipères, qui vous a avertis de fuir la colère à venir?
Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
8 Faites des fruits convenables à la repentance, et ne vous mettez point à dire en vous-mêmes: nous avons Abraham pour père; car je vous dis, que Dieu peut faire naître, même de ces pierres, des enfants à Abraham.
Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
9 Or la cognée est déjà mise à la racine des arbres; tout arbre donc qui ne fait point de bon fruit, s'en va être coupé, et jeté au feu.
Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
10 Alors les troupes l'interrogèrent, disant: que ferons-nous donc?
Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
11 Et il répondit, et leur dit: que celui qui a deux robes en donne une à celui qui n'en a point; et que celui qui a de quoi manger en fasse de même.
Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
12 Il vint aussi à lui des péagers pour être baptisés, qui lui dirent: maître, que ferons-nous?
Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
13 Et il leur dit: n'exigez rien au-delà de ce qui vous est ordonné.
Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
14 Les gens de guerre l'interrogèrent aussi, disant: et nous, que ferons-nous? Il leur dit: n'usez point de concussion, ni de fraude contre personne, mais contentez-vous de vos gages.
Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
15 Et comme le peuple était dans l'attente, et raisonnait en soi-même si Jean n'était point le Christ,
Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
16 Jean prit la parole, et dit à tous: pour moi, je vous baptise d'eau; mais il en vient un plus puissant que moi, duquel je ne suis pas digne de délier la courroie des souliers; celui-là vous baptisera du Saint-Esprit et de feu.
Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
17 Il a son van en sa main, et il nettoiera entièrement son aire, et assemblera le froment dans son grenier, mais il brûlera la paille au feu qui ne s'éteint point.
Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
18 Et en faisant plusieurs autres exhortations, il évangélisait au peuple.
Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
19 Mais Hérode le Tétrarque étant repris par lui au sujet d'Hérodias, femme de Philippe son frère, et à cause de tous les maux qu'il avait faits,
Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
20 Ajouta encore à tous les autres celui de mettre Jean en prison.
Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
21 Or il arriva que comme tout le peuple était baptisé, Jésus aussi étant baptisé, et priant, le ciel s'ouvrit.
Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
22 Et le Saint-Esprit descendit sur lui sous une forme corporelle, comme celle d'une colombe; et il y eut une voix du ciel, qui lui dit: tu es mon Fils bien-aimé, j'ai pris en toi mon bon plaisir.
Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
23 Et Jésus commençait d'avoir environ trente ans, fils (comme on l'estimait) de Joseph, [qui était fils] de Héli,
Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
24 [Fils] de Matthat, [fils] de Lévi, [fils] de Melchi, [fils] de Janna, [fils] de Joseph,
mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
25 [Fils] de Mattathie, [fils] d'Amos, [fils] de Nahum, [fils] d'Héli, [fils] de Naggé,
mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
26 [Fils] de Maath, [fils] de Mattathie, [fils] de Sémei, [fils] de Joseph, [fils] de Juda,
mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
27 [Fils] de Johanna, [fils] de Rhésa, [fils] de Zorobabel, [fils] de Salathiel, [fils] de Néri,
mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
28 [Fils] de Melchi, [fils] d'Addi, [fils] de Cosam, [fils] d'Elmodam, [fils] d'Er,
mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
29 [Fils] de José, [fils] d'Eliézer, [fils] de Jorim, [fils] de Matthat, [fils] de Lévi,
mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
30 [Fils] de Siméon, [fils] de Juda, [fils] de Joseph, [fils] de Jonan, [fils] d'Eliakim,
mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
31 [Fils] de Melca, [fils] de Maïnan, [fils] de Matthata, [fils] de Nathan, [fils] de David,
mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
32 [Fils] de Jessé, [fils] d'Obed, [fils] de Booz, [fils] de Salmon, [fils] de Naasson,
mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
33 [Fils] d'Aminadab, [fils] d'Aram, [fils] d'Esrom, [fils] de Pharès, [fils] de Juda,
mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
34 [Fils] de Jacob, [fils] d'Isaac, [fils] d'Abraham, [fils] de Thara, [fils] de Nachor,
mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
35 [Fils] de Sarug, [fils] de Ragau, [fils] de Phaleg, [fils] d'Héber, [fils] de Sala,
mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
36 [Fils] de Caïnan, [fils] d'Arphaxad, [fils] de Sem, [fils] de Noé, [fils] de Lamech,
mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
37 [Fils] de Mathusala, [fils] d'Hénoc, [fils] de Jared, [fils] de Mahalaléel, [fils] de Caïnan,
mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
38 [Fils] d'Enos, [fils] de Seth, [fils] d'Adam, [fils] de Dieu.
mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.

< Luc 3 >