< Jean 1 >

1 Au commencement était la Parole, et la Parole était avec Dieu; et cette parole était Dieu:
Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
2 Elle était au commencement avec Dieu.
Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
3 Toutes choses ont été faites par elle, et sans elle rien de ce qui a été fait, n'a été fait.
Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa.
4 En elle était la vie, et la vie était la Lumière des hommes.
Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
5 Et la Lumière luit dans les ténèbres, mais les ténèbres ne l'ont point reçue.
Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
6 Il y eut un homme appelé Jean, qui fut envoyé de Dieu.
Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane.
7 Il vint pour rendre témoignage, pour rendre, dis-je, témoignage à la Lumière, afin que tous crûssent par lui.
Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire.
8 Il n'était pas la Lumière, mais il [était envoyé] pour rendre témoignage à la Lumière.
Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika.
9 [Cette] Lumière était la véritable, qui éclaire tout homme venant au monde.
Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
10 Elle était au monde, et le monde a été fait par elle; mais le monde ne l'a point connue.
Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye.
11 Il est venu chez soi; et les siens ne l'ont point reçu;
Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
12 Mais à tous ceux qui l'ont reçu, il leur a donné le droit d'être faits enfants de Dieu, [savoir] à ceux qui croient en son Nom;
Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu;
13 Lesquels ne sont point nés de sang, ni de la volonté de la chair, ni de la volonté de l'homme; mais ils sont nés de Dieu.
ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
14 Et la Parole a été faite chair, elle a habité parmi nous, et nous avons contemplé sa gloire, [qui a été] une gloire, comme la gloire du Fils unique du Père, pleine de grâce et de vérité.
Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
15 Jean a [donc] rendu témoignage de lui, et a crié, disant: c'est celui duquel je disais: celui qui vient après moi m'est préféré, car il était avant moi.
Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’”
16 Et nous avons tous reçu de sa plénitude, et grâce pour grâce.
Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso.
17 Car la Loi a été donnée par Moïse; la grâce et la vérité est venue par Jésus-Christ.
Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
18 Personne ne vit jamais Dieu; le Fils unique qui est au sein du Père, est celui qui nous l'a révélé.
Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
19 Et c'est ici le témoignage de Jean, lorsque les Juifs envoyèrent de Jérusalem des Sacrificateurs et des Lévites pour l'interroger, [et lui dire]: toi qui es-tu?
Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani.
20 Car il l'avoua, et ne le nia point, il l'avoua, dis-je, [en disant]: ce n'est pas moi qui suis le Christ.
Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
21 Sur quoi ils lui demandèrent: qui es-tu donc? Es-tu Elie? Et il dit: je ne le suis point. Es-tu le Prophète? Et il répondit: non.
Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?” Iye anati, “Sindine.” “Kodi ndiwe Mneneri?” Iye anayankha kuti, “Ayi.”
22 Ils lui dirent donc: qui es-tu, afin que nous donnions réponse à ceux qui nous ont envoyés; que dis-tu de toi-même?
Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
23 Il dit: je suis la voix de celui qui crie dans le désert: aplanissez le chemin du Seigneur, comme a dit Esaïe le Prophète.
Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’”
24 Or ceux qui avaient été envoyés [vers lui] étaient d'entre les Pharisiens.
Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa
25 Ils l'interrogèrent encore, et lui dirent: pourquoi donc baptises-tu si tu n'es point le Christ, ni Elie, ni le Prophète?
anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
26 Jean leur répondit, et leur dit: pour moi, je baptise d'eau; mais il y en a un au milieu de vous, que vous ne connaissez point;
Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa.
27 C'est celui qui vient après moi, qui m'est préféré, et duquel je ne suis pas digne de délier la courroie du soulier.
Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
28 Ces choses arrivèrent à Bethabara, au-delà du Jourdain, où Jean baptisait.
Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
29 Le lendemain Jean vit Jésus venir à lui, et il dit: voilà l'Agneau de Dieu, qui ôte le péché du monde.
Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
30 C'est celui duquel je disais: après moi vient un personnage qui m'est préféré; car il était avant moi.
Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’
31 Et pour moi, je ne le connaissais point; mais afin qu'il soit manifesté à Israël, je suis venu à cause de cela baptiser d'eau.
Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
32 Jean rendit aussi témoignage, en disant: j'ai vu l'Esprit descendre du ciel comme une colombe, et s'arrêter sur lui.
Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye.
33 Et pour moi, je ne le connaissais point; mais celui qui m'a envoyé baptiser d'eau, m'avait dit: celui sur qui tu verras l'Esprit descendre, et se fixer sur lui, c'est celui qui baptise du Saint-Esprit.
Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’
34 Et je l'ai vu, et j'ai rendu témoignage, que c'est lui qui est le Fils de Dieu.
Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
35 Le lendemain encore Jean s'arrêta, et [avec lui] deux de ses disciples;
Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake.
36 Et regardant Jésus qui marchait, il dit: voilà l'Agneau de Dieu.
Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
37 Et les deux disciples l'entendirent tenant ce discours, et ils suivirent Jésus.
Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu.
38 Et Jésus se retournant, et voyant qu'ils le suivaient, il leur dit: que cherchez-vous? Ils lui répondirent: Rabbi, c'est-à-dire, Maître, où demeures-tu?
Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
39 Il leur dit: venez, et le voyez. Ils y allèrent, et ils virent où il demeurait; et ils demeurèrent avec lui ce jour-là; car il était environ dix heures.
Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.” Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
40 Or André, frère de Simon Pierre, était l'un des deux qui [en] avaient ouï parler à Jean, et qui l'avaient suivi.
Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu.
41 Celui-ci trouva le premier Simon son frère, et il lui dit: nous avons trouvé le Messie; c'est-à-dire, le Christ.
Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
42 Et il le mena vers Jésus, et Jésus ayant jeté la vue sur lui, dit: tu es Simon, fils de Jonas, tu seras appelé Céphas; c'est-à-dire, Pierre.
Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
43 Le lendemain Jésus voulut aller en Galilée, et il trouva Philippe, auquel il dit: suis-moi.
Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
44 Or Philippe était de Bethsaïda, la ville d'André et de Pierre.
Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida.
45 Philippe trouva Nathanaël, et lui dit: nous avons trouvé Jésus, qui est de Nazareth, fils de Joseph, celui duquel Moïse a écrit dans la Loi, et [duquel] aussi les Prophètes [ont écrit].
Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
46 Et Nathanaël lui dit: peut-il venir quelque chose de bon de Nazareth? Philippe lui dit: viens, et vois.
Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?” Filipo anati, “Bwera udzaone.”
47 Jésus aperçut Nathanaël venir vers lui, et il dit de lui: voici vraiment un Israëlite en qui il n'y a point de fraude.
Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
48 Nathanaël lui dit: d'où me connais-tu? Jésus répondit, et lui dit: avant que Philippe t'eût appelé quand tu étais sous le figuier, je te voyais.
Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?” Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
49 Nathanaël répondit, et lui dit: Maître, tu es le Fils de Dieu; tu es le Roi d'Israël.
Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
50 Jésus répondit, et lui dit: parce que je t'ai dit que je te voyais sous le figuier, tu crois; tu verras bien de plus grandes choses que ceci.
Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.”
51 Il lui dit aussi: en vérité, en vérité je vous dis: désormais vous verrez le ciel ouvert, et les Anges de Dieu montant et descendant sur le Fils de l'homme.
Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”

< Jean 1 >