< Jean 2 >

1 Or trois jours après on faisait des noces à Cana de Galilée, et la mère de Jésus était là.
Pa tsiku lachitatu munali ukwati mu Kana wa ku Galileya. Amayi ake a Yesu anali komweko,
2 Et Jésus fut aussi convié aux noces, avec ses Disciples.
ndipo Yesu ndi ophunzira ake anayitanidwanso ku ukwatiwo.
3 Et le vin étant venu à manquer, la mère de Jésus lui dit: ils n'ont point de vin.
Vinyo atatha, amayi a Yesu anati kwa Iye, “Wawathera vinyo.”
4 Mais Jésus lui répondit: qu'y a-t-il entre moi et toi, femme? mon heure n'est point encore venue.
Yesu anayankha kuti, “Amayi, chifukwa chiyani mukundiwuza Ine? Nthawi yanga sinakwane.”
5 Sa mère dit aux serviteurs: faites tout ce qu'il vous dira.
Amayi ake anati kwa antchito, “Inu muchite chilichonse chimene akuwuzeni.”
6 Or il y avait là six vaisseaux de pierre, mis selon l'usage de la purification des Juifs, dont chacun tenait deux ou trois mesures.
Pamenepo panali mitsuko yamiyala yothiramo madzi isanu ndi umodzi, imene Ayuda amagwiritsa ntchito pa mwambo wodziyeretsa. Uliwonse unali ndi malita 100 kapena kupitirirapo.
7 Et Jésus leur dit: emplissez d'eau ces vaisseaux. Et ils les emplirent jusques au haut.
Yesu anati kwa antchitowo, “Dzazani madzi mʼmitsukoyi,” ndipo iwo anadzaza ndendende.
8 Puis il leur dit: versez-en maintenant, et portez-en au maître d'hôtel. Et ils lui en portèrent.
Ndipo Iye anatinso kwa iwo, “Tsopano tungani ndipo kaperekeni kwa mkulu waphwando.” Iwo anachita momwemo.
9 Quand le maître d'hôtel eut goûté l'eau qui avait été changée en vin, (or il ne savait pas d'où cela venait, mais les serviteurs qui avaient puisé l'eau, le savaient bien, ) il s'adressa à l'époux.
Mkulu waphwando analawa madziwo amene anasandulika vinyo, ndipo sanazindikire kumene vinyoyo anachokera, ngakhale kuti antchito amene anatunga madziwo amadziwa. Kenaka anayitanira mkwati pambali
10 Et lui dit: tout homme sert le bon vin le premier, et puis le moindre après qu'on a bu plus largement; [mais] toi, tu as gardé le bon vin jusqu'à maintenant.
ndipo anati, “Aliyense amatulutsa vinyo wokoma kwambiri poyambirira ndipo kenaka vinyo wosakoma pamene oyitanidwa atamwa kale wambiri; koma iwe wasunga wokoma mpaka tsopano.”
11 Jésus fit ce premier miracle à Cana de Galilée, et il manifesta sa gloire, et ses Disciples crurent en lui.
Ichi chinali chizindikiro chodabwitsa choyamba chimene Yesu anachita ku Kana wa ku Galileya. Potero Iye anawulula ulemerero wake, ndipo ophunzira ake anamukhulupirira Iye.
12 Après cela il descendit à Capernaüm avec sa mère, et ses frères, et ses Disciples; mais ils y demeurèrent peu de jours.
Zitatha izi Iye anatsikira ku Kaperenawo pamodzi ndi amayi ake, abale ake ndi ophunzira ake. Iwo anakhala kumeneko masiku owerengeka.
13 Car la Pâque des Juifs était proche; c'est pourquoi Jésus monta à Jérusalem.
Nthawi ya Paska ya Ayuda itayandikira, Yesu anapita ku Yerusalemu.
14 Et il trouva dans le Temple des gens qui vendaient des bœufs, et des brebis, et des pigeons; et les changeurs qui y étaient assis.
Mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu Iye anapeza anthu akugulitsa ngʼombe, nkhosa ndi nkhunda ndipo ena akusintha ndalama pa matebulo.
15 Et ayant fait un fouet avec de petites cordes, il les chassa tous du Temple, avec les brebis, et les bœufs; et il répandit la monnaie des changeurs, et renversa les tables.
Chifukwa cha zimenezi Iye anapanga chikwapu cha zingwe ndipo anatulutsa onse mʼbwalo la Nyumbayo, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe; Iye anamwaza ndalama zawo ndi kugudubuza matebulo.
16 Et il dit à ceux qui vendaient des pigeons: ôtez ces choses d'ici, [et] ne faites pas de la Maison de mon Père un lieu de marché.
Kwa amene amagulitsa nkhunda, Iye anati, “Tulutsani izi muno! Osasandutsa Nyumba ya Atate anga msika!”
17 Alors ses Disciples se souvinrent qu'il était écrit: le zèle de ta Maison m'a rongé.
Ophunzira ake anakumbukira kuti zinalembedwa kuti, “Kudzipereka kwanga ku nyumba yanu kudzandiphetsa.”
18 Mais les Juifs prenant la parole, lui dirent: quel miracle nous montres-tu, pour entreprendre de faire de telles choses?
Kenaka Ayuda anamufunsa Yesu kuti, “Kodi mungationetse chizindikiro chodabwitsa chotani chotsimikizira ulamuliro wanu wochitira izi?”
19 Jésus répondit, et leur dit: abattez ce Temple, et en trois jours je le relèverai.
Yesu anawayankha kuti, “Gwetsani Nyumba ya Mulunguyi ndipo Ine ndidzayimanganso mʼmasiku atatu.”
20 Et les Juifs dirent: on a été quarante-six ans à bâtir ce Temple, et tu le relèveras dans trois jours!
Ayuda anayankha kuti, “Zinatenga zaka makumi anayi kumanga Nyumbayi, kodi Inu mungayimange masiku atatu?”
21 Mais il parlait du Temple, de son corps.
Koma Nyumba ya Mulungu imene amanena linali thupi lake.
22 C'est pourquoi lorsqu'il fut ressuscité des morts, ses Disciples se souvinrent qu'il leur avait dit cela, et ils crurent à l'Ecriture, et à la parole que Jésus avait dite.
Iye ataukitsidwa kwa akufa, ophunzira ake anakumbukira zimene Iye ananena ndipo anakhulupirira Malemba ndi mawu amene Yesu anayankhula.
23 Et comme il était à Jérusalem le [jour de] la fête de Pâque, plusieurs crurent en son Nom, contemplant les miracles qu'il faisait.
Tsopano Iye ali mu Yerusalemu pa phwando la Paska, anthu ambiri anaona zizindikiro zodabwitsa zimene amachita ndipo anakhulupirira dzina lake.
24 Mais Jésus ne se fiait point à eux, parce qu'il les connaissait tous;
Koma Yesu sanawakhulupirire iwo, pakuti amadziwa anthu onse.
25 Et qu'il n'avait pas besoin que personne lui rendit témoignage d'[aucun] homme; car lui-même savait ce qui était dans l'homme.
Iye sanafune umboni wa wina aliyense popeza amadziwa zomwe zinali mʼmitima mwa anthu.

< Jean 2 >