< Marc 15 >

1 Et d'abord au matin les principaux Sacrificateurs avec les Anciens et les Scribes, et tout le Consistoire, ayant tenu conseil, firent lier Jésus, et l'emmenèrent, et le livrèrent à Pilate.
Mmamawa, akulu a ansembe pamodzi ndi akuluakulu, aphunzitsi amalamulo ndi olamulira onse anamanga fundo. Anamumanga Yesu, namutenga ndi kukamupereka kwa Pilato.
2 Et Pilate l'interrogea, disant: es-tu le Roi des Juifs? Et [Jésus] répondant lui dit: tu le dis.
Pilato anafunsa kuti, “Kodi Iwe ndi Mfumu ya Ayuda?” Yesu anayankha kuti, “Mwatero ndinu.”
3 Or les principaux Sacrificateurs l'accusaient de plusieurs choses, mais il ne répondit rien.
Akulu a ansembe anamunenera zinthu zambiri.
4 Et Pilate l'interrogea encore, disant: ne réponds-tu rien? vois combien de choses ils déposent contre toi.
Ndipo Pilato anamufunsanso Iye kuti, “Kodi Iwe suyankhapo kanthu? Tamva zinthu zambiri akukunenerazi.”
5 Mais Jésus ne répondit rien non plus; de sorte que Pilate s'en étonnait.
Koma Yesu sanayankhebe, ndipo Pilato anadabwa.
6 Or il leur relâchait à la Fête un prisonnier, lequel que ce fût qu'ils demandassent.
Pa nthawi ya Phwando, panali chizolowezi chomasula munthu wamʼndende amene anthu amupempha.
7 Et il y en avait un, nommé Barabbas, qui était prisonnier avec ses complices pour une sédition, dans laquelle ils avaient commis un meurtre.
Munthu wotchedwa Baraba anali mʼndende pamodzi ndi anthu owukira amene anapha anthu pa nthawi ya chipolowe.
8 Et le peuple criant tout haut, se mit à demander [à Pilate qu'il fît] comme il leur avait toujours fait.
Gulu la anthu linabwera kwa Pilato ndi kumufunsa kuti awachitire zimene amachita nthawi zonse.
9 Mais Pilate leur répondit, en disant: voulez-vous que je vous relâche le Roi des Juifs?
“Kodi mukufuna kuti ndikumasulireni mfumu ya Ayuda?” Pilato anafunsa,
10 (Car il savait bien que les principaux Sacrificateurs l'avaient livré par envie.)
podziwa kuti akulu a ansembe anamupereka Yesu kwa iye chifukwa cha nsanje.
11 Mais les principaux Sacrificateurs excitèrent le peuple à demander que plutôt il relâchât Barabbas.
Koma akulu a ansembe anasonkhezera anthu kuti Pilato amasule Baraba mʼmalo mwa Yesu.
12 Et Pilate répondant, leur dit encore: que voulez-vous donc que je fasse de celui que vous appelez Roi des Juifs?
Pilato anawafunsa kuti, “Kodi nanga ndichite chiyani ndi uyu amene mukumutcha mfumu ya Ayuda?”
13 Et ils s'écrièrent encore: crucifie-le.
Anafuwula kuti, “Mpachikeni!”
14 Alors Pilate leur dit: mais quel mal a-t-il fait? et ils s'écrièrent encore plus fort: crucifie-le.
Pilato anafunsa kuti, “Chifukwa chiyani? Wapalamula mlandu wotani?” Koma anafuwula kwambiri, “Mpachikeni!”
15 Pilate donc voulant contenter le peuple, leur relâcha Barabbas; et après avoir fait fouetter Jésus, il le livra pour être crucifié.
Pilato pofuna kuwakondweretsa anthuwo, anawamasulira Baraba. Analamula kuti Yesu akwapulidwe mwankhanza, ndipo anamupereka kuti akapachikidwe.
16 Alors les soldats l'emmenèrent dans la cour, qui est le Prétoire, et toute la cohorte s'étant là assemblée,
Asilikali anamutenga Yesu ndi kupita naye mʼkati mwa nyumba yaufumu (dera lokhalako asilikali a mfumu) ndipo anasonkhanitsa gulu lonse la asilikali.
17 Ils le vêtirent d'une robe de pourpre, et ayant fait une couronne d'épines entrelacées l'une dans l'autre, ils la lui mirent sur la tête;
Anamuveka Iye mwinjiro wofiira, kenaka analuka chipewa cha minga ndi kuyika pa mutu pake.
18 Puis ils commencèrent à le saluer, [en lui disant]: nous te saluons, Roi des Juifs;
Ndipo anayamba kunena kwa lye kuti, “Ulemu kwa inu Mfumu ya Ayuda!”
19 Et ils lui frappaient la tête avec un roseau, et crachaient contre lui; et se mettant à genoux, ils se prosternaient devant lui.
Ndipo anamugogoda pa mutu mobwerezabwereza ndi ndodo ndi kumulavulira. Anamugwadira ndi kumulambira Iye.
20 Et après s'être [ainsi] moqués de lui, ils le dépouillèrent de la robe de pourpre, et le revêtirent de ses habits, et l'emmenèrent dehors pour le crucifier.
Ndipo anamuchita chipongwe, anamuvula mwinjiro wofiira uja ndi kumuveka zovala zake. Kenaka anamutenga kuti akamupachike.
21 Et ils contraignirent un certain [homme, nommé] Simon, Cyrénéen, père d'Alexandre et de Rufus, qui passait [par là], revenant des champs, de porter sa croix.
Munthu wina ochokera ku Kurene, Simoni, abambo a Alekisanda ndi Rufasi amadutsa kuchokera ku dziko la kwawo, ndipo anamuwumiriza kuti anyamule mtanda.
22 Et ils le menèrent au lieu [appelé] Golgotha, c'est-à-dire, le lieu du Crâne.
Anafika naye Yesu pa malo otchedwa Gologota (kutanthauza kuti, malo a bade)
23 Et ils lui donnèrent à boire du vin mixtionné avec de la myrrhe; mais il ne le prit point.
Kenaka anamupatsa Iye vinyo wosakaniza ndi mure, koma Iye sanamwe.
24 Et quand ils l'eurent crucifié, ils partagèrent ses vêtements, en les jetant au sort pour savoir ce que chacun en aurait.
Ndipo anamupachika Iye. Anachita maere ogawana zovala zake kuti aone chimene aliyense angatenge.
25 Or il était trois heures quand ils le crucifièrent.
Linali ora lachitatu mmawa pamene anamupachika Yesu.
26 Et l'écriteau contenant la cause de sa condamnation était: LE ROI DES JUIFS.
Chikwangwani cholembedwapo mlandu wake chinali choti: mfumu ya ayuda.
27 Ils crucifièrent aussi avec lui deux brigands, l'un à sa main droite, et l'autre à sa gauche.
Achifwamba awiri anapachikidwanso pamodzi ndi Iye, wina kumanja kwake ndi wina kumanzere kwake.
28 Et ainsi fut accomplie l'Ecriture, qui dit: Et il a été mis au rang des malfaiteurs.
(Ndipo malemba anakwaniritsidwa amene amati, “Iye anayikidwa mʼgulu la anthu oyipa).”
29 Et ceux qui passaient près de là lui disaient des outrages, branlant la tête, et disant: Hé! toi, qui détruis le Temple, et qui le rebâtis en trois jours,
Amene amadutsa pafupi anamunenera mawu amwano, akupukusa mitu yawo ndi kuti, “Haa! Iwe amene udzawononga Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanganso masiku atatu,
30 Sauve-toi toi-même, et descends de la croix.
tsika kuchoka pa mtandapo ndipo udzipulumutse wekha!”
31 Les principaux Sacrificateurs se moquant aussi avec les Scribes disaient entre eux: il a sauvé les autres, il ne peut se sauver lui-même.
Chimodzimodzinso akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo anamunyoza Iye pakati pawo. Iwo anati, “Anapulumutsa ena, koma sangathe kudzipulumutsa yekha!
32 Que le Christ, le Roi d’Israël descende maintenant de la croix, afin que nous le voyions et que nous croyions! Ceux aussi qui étaient crucifiés avec lui, lui disaient des outrages.
Musiyeni Khristu, Mfumu ya Aisraeli, atsike tsopano kuchoka pa mtanda, kuti ife tione ndi kukhulupirira.” Iwonso amene anapachikidwa naye pamodzi anamulalatira.
33 Mais quand il fut six heures, il y eut des ténèbres sur tout le pays jusqu'à neuf heures.
Pa ora lachisanu ndi chimodzi masana mdima unabwera pa dziko lonse mpaka pa ora lachisanu ndi chinayi masana.
34 Et à neuf heures Jésus cria à haute voix, disant: Eloï, Eloï, lamma sabachthani? c'est-à-dire: Mon Dieu! Mon Dieu! pourquoi m'as-tu abandonné?
Pa ora lachisanu ndi chinayi Yesu analira mofuwula kuti, “Eloi, Eloi, lama sabakitani?” Kutanthauza kuti, “Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji Ine?”
35 Ce que quelques-uns de ceux qui étaient là présents, ayant entendu, ils dirent: voilà, il appelle Elie.
Ena amene anali pafupi atamva izi anati, “Tamverani, akuyitana Eliya.”
36 Et quelqu'un accourut, qui remplit une éponge de vinaigre, et qui l'ayant mise au bout d'un roseau, lui en donna à boire, en disant: laissez, voyons si Elie viendra pour l'ôter de la croix.
Munthu wina anathamanga, natenga chinkhupule atachiviyika mu vinyo wosasa, anachizika ku mtengo, ndi kumupatsa Yesu kuti amwe. Munthuyo anati, “Musiyeni yekha tsopano. Tiyeni tione ngati Eliya angabwere kudzamutsitsa.”
37 Et Jésus ayant jeté un grand cri, rendit l'esprit.
Ndi mawu ofuwula, Yesu anapuma komaliza.
38 Et le voile du Temple se déchira en deux, depuis le haut jusqu'en bas.
Chinsalu chotchinga cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati kuyambira pamwamba mpaka pansi.
39 Et le Centenier qui était là vis-à-vis de lui, voyant qu'il avait rendu l'esprit en criant ainsi, dit: certainement cet homme était Fils de Dieu.
Ndipo Kenturiyo, amene anayima patsogolo pa Yesu, atamva kulira kwake ndi kuona mmene anafera anati, “Zoonadi, uyu anali Mwana wa Mulungu.”
40 Il y avait là aussi des femmes qui regardaient de loin, entre lesquelles étaient Marie-Magdeleine, et Marie [mère] de Jacques le mineur, et de Joses, et Salomé.
Amayi ena anali patali kuonerera. Pakati pawo panali Mariya Magadalena, Mariya amayi a Yakobo wamngʼono ndi Yose ndi Salome.
41 Qui lorsqu'il était en Galilée, l'avaient suivi, et l'avaient servi; [il y avait là] aussi plusieurs autres femmes qui étaient montées avec lui à Jérusalem.
Amayi awa ankamutsatira Iye mu Galileya ndi kumutumikira Iye pa zosowa zake. Amayi enanso ambiri amene anabwera naye ku Yerusalemu analinso pomwepo.
42 Et le soir étant déjà venu, parce que c'était la Préparation qui est avant le Sabbat;
Linali Tsiku Lokonzekera (kunena kuti, tsiku lomwe limatsatizana ndi Sabata). Choncho madzulo atayandikira,
43 Joseph d'Arimathée, Conseiller honorable, qui attendait aussi le Règne de Dieu, s'étant enhardi, vint à Pilate, et [lui] demanda le corps de Jésus.
Yosefe wa ku Arimateyu, mkulu wolamulira odziwika bwino, amene amadikirira ufumu wa Mulungu, anapita kwa Pilato molimba mtima ndi kukapempha mtembo wa Yesu.
44 Et Pilate s'étonna qu'il fût déjà mort; et ayant appelé le Centenier, il lui demanda s'il y avait longtemps qu'il était mort.
Pilato anadabwa pakumva kuti anali atamwalira kale. Anayitana Kenturiyo, namufunsa ngati Yesu anali atamwalira kale.
45 Ce qu'ayant appris du Centenier, il donna le corps à Joseph.
Atawuzidwa ndi Kenturiyo kuti zinali motero, anapereka mtembowo kwa Yosefe.
46 Et [Joseph] ayant acheté un linceul, le descendit de la croix, et l'enveloppa du linceul, et le mit dans un sépulcre qui était taillé dans le roc, puis il roula une pierre sur l'entrée du sépulcre.
Choncho Yosefe anagula nsalu yabafuta, natsitsa thupi, ndipo analikulunga mʼnsalu, naliyika mʼmanda amene anawagoba pa mwala. Kenaka anagubuduza mwala umene anatseka nawo mandawo.
47 Et Marie-Magdeleine, et Marie [mère] de Joses regardaient où on le mettait.
Mariya Magadalena ndi Mariya amayi a Yose anaona kumene anamuyika Yesu.

< Marc 15 >