< Genesis 25 >

1 Forsothe Abraham weddide another wijf, Ceture bi name,
Abrahamu anakwatira mkazi wina dzina lake Ketura.
2 which childide to him Samram, and Jexan, and Madan, and Madian, and Jesboth, and Sue.
Iyeyu anamubalira Zimurani, Yokisani, Medani, Midiyani, Isibaki ndi Suwa.
3 Also Jexan gendride Saba and Dadan. Forsothe the sones of Dadan weren Asurym, and Lathusym, and Laomym.
Yokisani anabereka Seba ndi Dedani ndipo zidzukulu za Dedani ndiwo Aasuri, Aletusi, ndi Aleumi.
4 And sotheli of Madian was borun Efa, and Ofer, and Enoth, and Abida, and Heldaa; alle these weren the sones of Cethure.
Ana aamuna a Midiyani anali, Efai, Eferi, Hanoki, Abida ndi Elida. Onsewa anali zidzukulu za Ketura.
5 And Abraham yaf alle thingis whiche he hadde in possessioun to Isaac;
Abrahamu anasiyira Isake chilichonse anali nacho.
6 sotheli he yaf yiftis to the sones of concubyns; and Abraham, while he lyuede yit, departide hem fro Ysaac, his sone, to the eest coost.
Koma pamene anali ndi moyo, Abrahamu anapereka mphatso kwa ana aakazi ake ena onse. Kenaka anawatumiza ku dziko la kummawa kuti akhale kutali ndi mwana wake Isake.
7 Forsothe the daies of lijf of Abraham weren an hundrid and `fyue and seuenti yeer;
Abrahamu anakhala ndi moyo zaka 175.
8 and he failide, and diede in good eelde, and of greet age, and ful of daies, and he was gaderid to his puple.
Abrahamu anamwalira atakalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
9 And Ysaac and Ismael, his sones, birieden him in the double denne, which is set in the feeld of Efron, sone of Seor Ethei,
Ana ake, Isake ndi Ismaeli anamuyika mʼphanga la Makipela pafupi ndi Mamre, mʼmunda umene kale unali wa Efroni mwana wa Zohari Mhiti,
10 euene ayens Mambre, which denne he bouyte of the sones of Heth; and he was biried there, and Sare his wijf.
uwu ndi munda umene Abrahamu anagula kwa Ahiti. Kumeneko Abrahamu anakayikidwa pamodzi ndi mkazi wake Sara.
11 And aftir the deeth of Abraham God blesside Isaac his sone, which dwellide bisidis the pit bi name of hym that lyueth and seeth.
Atamwalira Abrahamu, Mulungu anadalitsa mwana wake Isake, amene ankakhala pafupi ndi Beeri-lahai-roi (chitsime cha Wamoyo Wondipenya).
12 These ben the generaciouns of Ismael, sone of Abraham, whom Agar Egipcian, seruauntesse of Sare, childide to Abraham;
Nazi zidzukulu za Ismaeli, mwana wa Abrahamu amene wantchito wa Sara, Hagara Mwigupto uja, anaberekera Abrahamu.
13 and these ben the names of the sones of Ismael, in her names and generaciouns. The firste gendride of Ismael was Nabaioth, aftirward Cedar, and Abdeel, and Mabsan,
Awa ndi mayina a ana a Ismaeli monga mwa mndandanda wa mabadwidwe awo: Nebayoti ndiye anali mwana woyamba wa Ismaeli; kenaka Kedara, Adibeeli, Mibisamu,
14 and Masma, and Duma, and Massa,
Misima, Duma, Masa,
15 and Adad, and Thema, and Ithur, and Nafir, and Cedma.
Hadadi, Tema, Yeturi, Nafisi ndi Kedema;
16 These weren the sones of Ismael, and these weren names by castels and townes of hem, twelue princes of her lynagis.
Amenewa ndi ana a Ismaeli ndi mayina awo monga mwa midzi ndi misasa yawo. Anali olamulira mafuko khumi ndi awiri.
17 And the yeeris of lijf of Ismael weren maad an hundrid and seuene and thretti, and he failide, and diede, and was put to his puple.
Ismaeli anakhala ndi moyo zaka 137. Iye anamwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
18 Forsothe he enhabitide fro Euila til to Sur, that biholdith Egipt, as me entrith in to Assiriens; he diede bifore alle his britheren.
Zidzukulu za Ismaeli zinkakhala mʼdera la pakati pa Havila ndi Suri, kummwera kwa Igupto, mukamapita cha ku Asuri. Choncho anakhala kummawa kwa abale awo.
19 Also these ben the generaciouns of Ysaac sone of Abraham. Abraham gendride Isaac,
Iyi ndi mbiri ya Isake mwana wa Abrahamu. Abrahamu anabereka Isake
20 and whanne Isaac was of fourti yeer, he weddide a wijf, Rebecca, douyter of Batuel, of Sirie of Mesopotanye, the sistir of Laban.
ndipo Isake anali ndi zaka makumi anayi pamene anakwatira Rebeka mwana wa Betueli Mwaramu wa ku Padanaramu mlongo wa Labani Mwaramu.
21 And Isaac bisouyte the Lord for his wijf, for sche was bareyn; and the Lord herde him, and yaf conseiuyng to Rebecca.
Isake anapempherera mkazi wake kwa Yehova popeza iye anali wosabereka. Yehova anayankha pemphero lake ndipo mkazi wake Rebeka anatenga pathupi.
22 But the litle children weren hurtlid togidre in hir wombe; and sche seide, If it was so to comynge to me, what nede was it to conseyue? And sche yede and axide counsel of the Lord,
Koma pamene anawo amalimbana mʼmimba mwake, iye anati, “Bwanji zikundichitikira zoterezi?” Choncho anapita kukafunsa kwa Yehova.
23 which answerde, and seide, Twei folkis ben in thi wombe, and twei puplis schulen be departid fro thi wombe, and a puple schal ouercome a puple, and the more schal serue the lesse.
Yehova anati kwa iye, “Udzabala mafuko awiri a anthu olimbana, ndipo magulu awiri a anthu ochokera mwa iwe adzasiyana; fuko limodzi lidzakhala la mphamvu kuposa linzake, ndipo wamkulu adzatumikira wamngʼono.”
24 Thanne the tyme of childberyng cam, and lo! twei children weren foundun in hir wombe.
Pamene nthawi inakwana yakuti abeleke, Rebeka anaberekadi mapasa.
25 He that yede out first was reed, and al rouy in the manere of a skyn; and his name was clepid Esau.
Woyamba kubadwa anali wofiira, ndipo thupi lake lonse linali ngati chovala cha ubweya; choncho anamutcha Esau.
26 Anoon the tothir yede out, and helde with the hond the heele of the brother; and therfore he clepide him Jacob. Isaac was sixti yeer eeld, whanne the litle children weren borun.
Kenaka mʼbale wake anabadwa atagwira chidendene cha Esau; choncho anamutcha Yakobo. Isake anali ndi zaka 60 pamene Rebeka anabereka mapasawa.
27 And whanne thei weren woxun, Esau was maad a man kunnynge of huntyng, and a man erthe tilier; forsothe Jacob was a symple man, and dwellide in tabernaclis.
Anyamatawo anakula ndipo Esau anakhala katswiri wosaka, munthu wamʼthengo, pamene Yakobo anali munthu wofatsa, wokonda kukhala pa nyumba.
28 Isaac louyde Esau, for he eet of the huntyng of Esau; and Rebecca louyde Jacob.
Isake ankakonda Esau chifukwa cha nyama za kutchire zomwe ankakonda kudya, koma Rebeka ankakonda Yakobo.
29 Sotheli Jacob sethide potage; and whanne Esau cam weri fro the feld,
Tsiku lina pamene Yakobo ankaphika chakudya, Esau anabwera kuchokera kuthengo ali wolefuka ndi njala.
30 he seide to Jacob, Yyue thou to me of this reed sething, for Y am ful weri; for which cause his name was clepid Edom.
Iye anati kwa Yakobo, “Tandipatsako phala lofiiralo, ndimwe! Ndalefuka ndi njala.” (Nʼchifukwa chake amatchedwanso Edomu).
31 And Jacob seide to him, Sille to me the riyt of the first gendrid childe.
Yakobo anayankha, “Choyamba undigulitse ukulu wako.”
32 He answerde, Lo! Y die, what schulen the firste gendrid thingis profite to me?
Esau anati, “Chabwino, ine ndatsala pangʼono kufa, ukulu undithandiza chiyani?”
33 Jacob seide, therfor swere thou to me. Therfor Esau swoor, and selde the firste gendrid thingis.
Koma Yakobo anati, “Lumbira kwa ine choyamba.” Kotero Esau analumbiradi, ndipo anagulitsa ukulu wake kwa Yakobo.
34 And so whanne he hadde take breed and potage, Esau eet and drank, and yede forth, and chargide litil that he hadde seld the riyt of the firste gendrid child.
Choncho Yakobo anamupatsa Esau buledi ndi phala lofiira lija. Iye anadya ndi kumwa, nanyamuka kumapita. Motero Esau anapeputsa ukulu wake wachisamba uja.

< Genesis 25 >