< Genesis 24 >

1 Forsothe Abraham was eld, and of many daies, and the Lord hadde blessid hym in alle thingis.
Tsopano Abrahamu anali atakalamba kwambiri, ndipo Yehova anamudalitsa mu zonse anachita.
2 And he seide to the eldere seruaunt of his hows, that was souereyn on alle thingis that he hadde, Put thou thin hond vndur myn hipe,
Tsiku lina Abrahamu anawuza wantchito wake wamkulu amene ankayangʼanira zonse anali nazo, kuti “Ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga.
3 that Y coniure thee bi the Lord God of heuene and of erthe, that thou take not a wijf to my sone of the douytris of Chanaan, among whiche Y dwelle;
Ndikufuna kuti ulumbire pamaso pa Yehova, Mulungu wakumwamba ndi dziko lapansi, kuti sudzamupezera mwana wanga mkazi pakati pa atsikana Achikanaani a kuno kumene ndikukhala,
4 but that thou go to my lond and kynrede, and therof take a wijf to my sone Ysaac.
koma kuti udzapita ku dziko la kwathu ndi kukamupezera mkazi mwana wanga Isake pakati pa abale anga.”
5 The seruaunt aunswerde, If the womman nyle come with me in to this lond, whether Y owe lede ayen thi sone to the place, fro which thou yedist out?
Wantchito uja anafunsa kuti, “Nanga atakhala kuti mkaziyo sakufuna kubwera nane kuno? Kodi ine ndingadzatenge mwana wanu ndi kubwerera naye ku dziko kumene munachokera?”
6 Abraham seide, Be war, lest ony tyme thou lede ayen thidur my sone;
Abrahamu anati, “Uwonetsetse kuti usadzabwerere naye mwana wanga kumeneko.
7 the Lord of heuene that took me fro the hows of my fadir, and fro the lond of my birthe, which spak to me, and swoor, and seide, Y schal yyue this lond to thi seed, he schal sende his aungel bifore thee, and thou schalt take fro thennus a wijf to my sone; forsothe if the womman nyle sue thee,
Yehova Mulungu wakumwamba amene ananditenga kwa makolo anga nanditulutsa mʼdziko lobadwira, ameneyo anayankhula nane molumbira kuti, ‘Kwa zidzukulu zako ndidzapereka dziko ili.’ Iyeyu adzatumiza mngelo wake kuti akutsogolere kumeneko kukapezera mwana wanga mkazi.
8 thou schalt not be holdun bi the ooth; netheles lede not ayen my sone thidur.
Ngati mkaziyo adzakana kubwerera nawe ndiye kuti udzakhala womasuka ku lumbiro langa. Koma usadzamutenge mwana wanga ndi kubwerera naye kumeneko.”
9 Therfore the seruaunt puttide his hond vndur the hipe of Abraham, his lord, and swoor to him on this word.
Choncho wantchitoyo anayika dzanja lake pansi pa ntchafu ya mbuye wake Abrahamu nalumbira kwa iye kuti adzachitadi monga mwa mawu a Abrahamu.
10 And he took ten camels of the floc of his lord, and yede forth, and bar with him of alle the goodis of his lord; and he yede forth, and cam to Mesopotanye, to the citee of Nachor.
Tsono wantchito uja anatengapo ngamira khumi mwa ngamira za mbuye wake pamodzi ndi zinthu zabwino za mitundumitundu. Ndipo ananyamuka kupita ku mzinda wa Nahori, mʼdziko la Mesopotamiya.
11 And whanne he hadde maad the camels to reste with out the citee, bisidis the pit of watir, in the euentid, in that tyme in which wymmen ben wont to go out to drawe watir,
Atafika, anagwaditsa pansi ngamira zija pafupi ndi chitsime chimene chinali kunja kwa mzinda uja. Awa anali madzulo ndithu, nthawi imene amayi amapita kukatunga madzi.
12 he seide, Lord God of my lord Abraham, Y biseche, meete with me to dai, and do mersi with my lord Abraham.
Ndipo wantchito uja anapemphera nati, “Haa, Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, mulole kuti zinthu zindiyendere ine lero, ndipo muonetseni mbuye wanga Abrahamu kukoma mtima kwanu kosasinthika.
13 Lo! Y stonde nyy the welle of watir, and the douytris of enhabiters of this citee schulen go out to drawe watir;
Taonani ndayima pambali pa chitsimechi, ndipo atsikana a mu mzindawu akubwera kudzatunga madzi.
14 therfor the damysel to which Y schal seie, Bowe doun thi watir pot that Y drynke, and schal answere, Drynke thou, but also Y schal yyue drynke to thi camels, thilke it is which thou hast maad redi to thi seruaunt Ysaac; and bi this Y schal vndirstonde that thou hast do mersi with my lord Abraham.
Ine ndipempha mtsikana wina kuti, ‘Chonde tula mtsuko wako kuti ndimweko madzi.’ Tsono iye akayankha kuti ‘Imwani,’ ndipo ndidzapatsanso ngamira zanu madziwo, ameneyo akhale mkazi amene mwasankhira mtumiki wanu Isake.” Zimenezi zikachitika, ndidzadziwa kuti mwaonetsadi kukoma mtima kwanu kosasinthika kwa mbuye wanga.
15 And he hadde not yit fillid the wordis with ynne hym silf, and lo! Rebecca, the douytir of Batuel, sone of Melcha, wijf of Nachor, brothir of Abraham, yede out, hauynge a watir pot in hir schuldre;
Asanatsirize kupemphera, anangoona Rebeka watulukira atasenza mtsuko wake pa phewa. Iyeyu anali mwana wa Betueli mwana wa Milika, mkazi wa Nahori mʼbale wake wa Abrahamu.
16 a damysel ful comeli, and faireste virgyn, and vnknowun of man. Sotheli sche cam doun to the welle, and fillide the watir pot, and turnide ayen.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri, namwali amene sanadziwe mwamuna. Iye anatsikira ku chitsime nadzaza mtsuko nakweranso ku mtunda.
17 And the seruaunt mette hir, and seide, Yyue thou to me a litil of the watir of thi pot to drynke.
Wantchito uja anathamanga kukakumana naye nati, “Chonde patseko madzi pangʼono a mu mtsuko wakowo kuti ndimwe.”
18 Which answerde, Drynke thou, my lord. And anoon sche dide doun the watir pot on hir schuldre, and yaf drynk to hym.
Mtsikanayo anati, “Imwani mbuye wanga.” Ndipo mofulumira anatsitsa mtsuko uja nawuyika mʼmanja ndi kumupatsa kuti amwe.
19 And whanne he hadde drunke, sche addide, But also Y schal drawe watir to thi camelis, til alle drynken.
Atatha kupereka madzi akumwa kwa mlendo uja, mtsikanayo anati, “Ndikatungiranso ngamira madzi kuti zimwe mpaka zitakwana.”
20 And sche helde out the watir pot in trouyis, and ran ayen to the pit, to drawe watir, and sche yaf watir drawun to alle the camels.
Choncho anafulumira kukhuthula madzi a mu mtsuko aja momwera ziweto, nathamanga kubwerera ku chitsime kukatunga madzi ena, ndipo anatunga okwanira ngamira zake zonse.
21 Sotheli he bihelde hir priueli, and wolde wite whether the Lord hadde sped his wei, ethir nay.
Modekha, munthu uja anayangʼanitsitsa kwambiri mtsikana uja kuti adziwedi ngati Yehova anamutsogolera pa ulendo wake uja kapena ayi.
22 Therfor after that the camels drunken, the man brouyte forth goldun eere ryngis, weiynge twei siclis, and as many bies of the arm, in the weiyte of ten siclis.
Ngamira zija zitatha kumwa, mlendo uja anatulutsa chipini chagolide cholemera theka la sekeli ndi zibangiri zagolide ziwiri zolemera masekeli 100.
23 And he seide to hir, Whos douyter art thou? schewe thou to me, is ony place in the hows of thi fadir to dwelle?
Kenaka anafunsa namwaliyo kuti, “Chonde tandiwuza, kodi ndiwe mwana wa yani? Ndipo kodi malo alipo kwanu woti ife nʼkugona?”
24 Which answerde, Y am the douyter of Batuel, sone of Nachor, whom Melcha childide to him.
Anamuyankha kuti, “Ine ndine mwana wa Betueli, mwana amene Milika anaberekera Nahori.”
25 And sche addide, seiynge, Also ful myche of prouendre and of hey is at vs, and a large place to dwelle.
Ndipo anapitiriza kunena kuti, “Chakudya chodyetsa nyamazi chilipo kwathu ndipo malo woti mugone aliponso.”
26 The man bowide hym silf,
Kenaka munthuyo anawerama pansi napembedza Yehova,
27 and worschipide the Lord, and seide, Blessid be the Lord God of my lord Abraham, which God took not aweie his mersy and treuthe fro my lord, and ledde me bi riyt weie in to the hous of the brother of my lord.
nati, “Alemekezeke Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene waonetsa kukoma mtima kwake kosasintha ndi kukhulupirika kwake kwa mbuye wanga. Yehova wanditsogolera pa ulendo wanga mpaka ndafika ku nyumba kwa abale ake a mbuye wanga.”
28 And so the damesel ran, and telde in the hous of hir modir alle thingis whiche sche hadde herd.
Mtsikana uja anathamanga nakafotokozera zimenezi anthu a kwa amayi ake.
29 Sotheli Rebecca hadde a brothir, Laban bi name, whiche yede out hastili to the man, where he was with out forth.
Tsono Rebeka anali ndi mlongo wake dzina lake Labani.
30 And whanne he hadde seyn the eere ryngis and byes of the arm in the hondis of his sister, and hadde herd alle the wordis of hir tellynge, the man spak to me these thingis, he cam to the man that stood bisidis the camels, and nyy the welle of watir,
Iyeyu atangoona chipini pa mphuno ndi zibangiri pa mikono ya mlongo wake komanso kumva zimene mlendo uja ananena kwa Rebekayo, anathamangira kwa mlendo uja, ndipo anamupeza atangoyima ndi ngamira zake pafupi ndi chitsime.
31 and seide to him, Entre thou, the blessid of the Lord; whi stondist thou with outforth? I haue maad redi the hows, and a place to thi camels.
Iye anati, “Tiyeni kwathu, ndinu munthu amene Yehova wamudalitsa. Bwanji mwangoyimirira panja pano? Ine ndakukonzerani malo ogona inu ndi ngamira zanu.”
32 And he brouyte hym in to the ynne, and unsadlide the camels, and yaf prouendre, and hey, and watir to waische the feet of camels, and of men that camen with hym.
Choncho munthu uja analowa mʼnyumba. Labani anatsitsa katundu anali pa ngamira uja. Kenaka anazipatsa ngamira zija chakudya, ndiponso anapereka madzi wosamba mapazi kwa mlendo uja ndi anthu ena onse.
33 And breed was set forth in his siyt, which seide, Y schal not ete til Y speke my wordis. He answerde to the man, Speke thou.
Chakudya chitabwera mlendo uja anati, “Sindidya mpaka nditakuwuzani zimene ndadzera kuno.” Labani anati, “Yankhulani.”
34 And the man seide, Y am the seruaunt of Abraham,
Motero iye anati, “Ine ndine wantchito wa Abrahamu.
35 and the Lord hath blessid my lord greetli, and he is maad greet; and God yaf to hym scheep, and oxun, siluer, and gold, seruauntis, and handmaides, camels, and assis.
Yehova wadalitsa mbuye wanga kwambiri, ndiponso walemera. Wamupatsa nkhosa ndi ngʼombe, siliva ndi golide, antchito aamuna ndi antchito aakazi, komanso ngamira ndi abulu.
36 And Sare, `the wijf of my lord, childide a sone to my lord in his eelde, and he yaf alle thingis that he hadde to that sone.
Sara, mkazi wa mbuye wanga anamubalira iye mwana wamwamuna ngakhale kuti Sarayo anali wokalamba. Tsono mbuye wanga wamupatsa mwanayo chuma chonse.
37 And my lord chargide me greetli, and seide, Thou schalt not take to my sone a wijf of the douytris of Canaan, in whos lond Y dwelle,
Tsono mbuye wanga anandilumbiritsa kuti ndisunge mawu ake akuti, ‘Usadzamupezere mwana wanga mkazi kuchokera mwa atsikana a dziko lino la Kanaani,
38 but thou schalt go to the hous of my fadir, and of myn kynrede thou schalt take a wijf to my sone.
koma upite ku banja la abambo anga ndi kwa abale anga kuti ukamupezere mkazi mwana wanga.’”
39 Forsothe Y answerde to my lord, What if the womman nyle come with me?
“Ndipo ine ndinati kwa mbuye wanga, ‘Nanga mkaziyo akakapanda kubwera nane pamodzi?’
40 He seide, The Lord in whose siyt Y go, schal sende his aungel with thee, and he schal dresse thi weie; and thou schalt take a wijf to my sone of my kynrede, and of my fadris hows.
“Iye anayankha, ‘Yehova amene ndakhala ndikumumvera nthawi zonse, adzatumiza mngelo wake kuti akuperekeze ndipo adzakuthandiza mpaka ukamupezere mwana wanga mkazi kuchokera ku mtundu wanga, wa fuko langa.
41 Thou schalt be innocent fro my curs, whanne thou comest to my kynesmen, and thei yyuen not `the womman to thee.
Ukadzachita zimenezi udzakhala mfulu wosamangidwa ndi lumbiro langali. Koma tsono ukadzafika kwa fuko langa, ndipo ngati sadzalola kukupatsa mbeta ya mwana wanga, aponso udzamasuka ku lumbiro langali.’”
42 Therfor Y cam to day to the welle of watir, and Y seide, Lord God of my lord Abraham, if thou hast dressid my weie in which Y go now, lo!
“Tsono lero lino pamene ndafika pa chitsime, ndinapempha kuti, ‘Yehova, Mulungu wa mbuye wanga, Abrahamu, ngati Inu mwandidalitsadi pa ulendowu,
43 Y stonde bisidis the welle of watir, and the maide that schal go out to drawe watir herith me, yyue thou to me a litil of water to drynke of thi pot,
taonani ndayima pambali pa chitsime ichi; ndipo ndidzati kwa namwali amene atabwere kudzatunga kuti, chonde nditamwako madzi a mu mtsuko wakowu,’
44 and seith to me, And thou drynke, and Y schal drawe watir to thi camels, thilke is the womman which the Lord hath maad redi to the sone of my lord.
ndipo ngati adzandiyankha kuti, ‘Imwani ndipo ndizimwetsanso madzi ngamira zanuzi,’ ameneyo akhale yemwe Yehova wamusankhira mwana wa mbuye wanga.”
45 While Y turnede in thouyte these thingis with me, Rebecca apperide, comynge with a pot which sche bare in the schuldre; and sche yede doun to the welle, and drowe watir. And Y seide to hir, Yyue thou a litil to me to drynke; and sche hastide,
“Ndisanatsirize kupemphera, ndinangoona Rebeka akutulukira mtsuko wake uli pa phewa. Anatsetserekera ku chitsime kukatunga madzi ndipo ndinati kwa iye, ‘Chonde patseko madzi akumwa.’
46 and dide doun the pot of the schuldre, and seide to me, And thou drynke, and Y schal yyue drynke to thi camels; Y drank, and watride the camels.
“Mofulumira, anatsitsa mtsuko wake pa phewa pake nati, ‘Imwani ndiponso ndizimwetsa madzi ngamira zanuzi.’ Kotero ine ndinamwa ndipo anamwetsanso ngamirazo.
47 And Y axide hir, and seide, Whos douytir art thou? Which answerde, Y am the douytir of Batuel, sone of Nachor, whom Melcha childide to him. And so Y hangide eere ryngis to ourne hir face, and Y puttide bies of the arm in hir hondis,
“Ndinamufunsa kuti, ‘Ndiwe mwana wa yani?’ “Iye anati, ‘Ndine mwana wa Betueli mwana wa Nahori, amene Milika anamuberekera.’ “Tsono ndinayika chipini pa mphuno yake ndi kumveka zibangiri mʼmikono yake,
48 and lowliche Y worschipide the Lord, and Y blessid the Lord God of my lord Abraham, which God ledde me bi riyt weie, that Y schulde take the douytir of the brothir of my lord to his sone.
kenaka ndinawerama pansi ndi kupembedza Yehova. Ndipo ndinatamanda Yehova, Mulungu wa mbuye wanga Abrahamu, amene anandilondolera mokhulupirika njira yanga. Iye wandifikitsa kwa mʼbale wake kumene ndapezera mbeta mwana wa mbuye wanga.
49 Wherfor if ye don mercy and treuthe with `my lord, schewe ye to me; ellis if othir thing plesith, also seie ye this, that Y go to the riyt side ethir to the left side.
Tsono ngati mukufuna kuonetsa kukoma mtima kwanu kwa mbuye wanga, ndikuonetsa kukhulupirika kwanu, ndiwuzeni; ndipo ngati si choncho ndiwuzeninso kuti ndidziwe chochita.”
50 Laban and Batuel answeriden, The word is gon out of the Lord; we moun not speke ony other thing with thee without his plesaunce.
Labani ndi Betueli anayankha nati, “Izi ndi zochokera kwa Yehova, ndipo ife sitinganenepo kanthu.
51 Lo! Rebecca is bifore thee; take thou hir, and go forth, and be sche wijf of the sone of thi lord, as the Lord spak.
Nayu Rebeka, mutengeni muzipita naye kuti akakhale mkazi wa mwana wa mbuye wanu, monga Yehova wanenera.”
52 And whanne the child of Abraham hadde herd this, he felde doun, and worschipide the Lord in erthe.
Wantchito wa Abrahamu uja atamva zimene anawerama pansi pamaso pa Yehova.
53 And whanne vessels of siluer, and of gold, and clothis weren brouyt forth, he yaf tho to Rebecca for yifte, and he yaf yiftis to hir britheren, and modir.
Kenaka wantchitoyo anatulutsa ziwiya zagolide ndi zasiliva ndi zovala nazipereka kwa Rebeka. Anaperekanso mphatso zina za mtengowapatali kwa mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka.
54 And whanne a feeste was maad, thei eeten and drunken to gider, and dwelliden there. Forsothe the child roos eerli, and spak, Delyuere ye me, that Y go to my lord.
Tsono wantchito uja ndi anthu amene anali naye anadya, kumwa nagona komweko. Kutacha mmawa wake, wantchito uja anati, “Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
55 Hir britheren and modir answerden, The damesele dwelle nameli ten daies at vs, and aftirward sche schal go forth.
Koma mlongo wake ndi amayi ake a Rebeka anayankha kuti, “Muloleni mtsikanayu abakhala nafe masiku khumi kapena kupyolerapo, kenaka mukhoza kupita.”
56 The child seide, Nyle ye holde me, for the Lord hath dressid my weie; delyuere ye me, that I go to my lord.
Koma iye anawawuza kuti, “Chonde musandichedwetse. Yehova wandithandiza kale pa ulendo wanga. Mundilole ndibwerere kwa mbuye wanga.”
57 And thei seiden, Clepe we the damysele, and axe we hir wille.
Koma iwo anati, “Bwanji timuyitane mtsikanayo ndipo timufunse ngati afuna kupita nanu panopa.”
58 And whanne sche was clepid, and cam, thei axiden, Wolt thou go with this man?
Choncho iwo anamuyitana Rebeka uja namufunsa kuti, “Kodi ukufuna kupita ndi munthuyu panopa?” Iye anayankha kuti, “Ndipita.”
59 And sche seide, Y schal go. Therfor they delyueriden hir, and hir nurse, and the seruaunt of Abraham, and hise felowis, and wischiden prosperitees to her sister,
Kotero anamulola Rebeka pamodzi ndi mlezi wake kuti apite ndi wantchito wa Abrahamu pamodzi ndi anthu amene anali naye.
60 and seiden, Thou art oure sister, encreesse thou in to a thousand thousandis, and thi seed gete the yatis of hise enemyes.
Ndipo iwo anadalitsa Rebeka ndi kumuwuza kuti, “Iwe ndiwe mlongo wathu, Mulungu akudalitse iwe, ukhale mayi wa anthu miyandamiyanda; ndi kuti zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo.”
61 Therfor Rebecca and hir damesels stieden on the camels, and sueden the man, which turnede ayen hasteli to his lord.
Kenaka Rebeka ndi antchito ake ananyamuka kukakwera ngamira zawo ndipo anapita naye pamodzi munthu uja. Choncho wantchito uja anatenga Rebeka nʼkumapita.
62 In that tyme Ysaac walkide bi the weie that ledith to the pit, whos name is of hym that lyueth and seeth; for he dwellide in the south lond.
Pa nthawiyi nʼkuti Isake atafika kuchokera ku chitsime cha Wamoyo Wondipenya (Beeri-lahai-roi), popeza tsopano ankakhala ku Negevi.
63 And he yede out to thenke in the feeld, for the dai was `bowid thanne; and whanne he hadde reisid the iyen, he seiy camels comynge afer.
Tsiku lina chakumadzulo, Isake anatuluka kukayendayenda ku munda, ndipo atakweza maso anaona ngamira zikubwera.
64 And whanne Ysaac was seyn, Rebecca liyte doun of the camel,
Rebeka nayenso anatukula maso naona Isake. Ndipo anatsika pa ngamira yake
65 and seide to the child, Who is that man that cometh bi the feeld in to the metyng of vs? And the child seide to hir, He is my lord. And sche took soone a mentil, and hilide hir.
nafunsa wantchito uja kuti, “Kodi munthu uyo ndi ndani akuyenda mʼmundamo kubwera kudzakumana nafe?” Wantchitoyo anayankha, “Ndiye mbuye wanga.” Choncho Rebeka anatenga nsalu ndi kufunda kumaso.
66 Forsothe the seruaunt tolde to his lord Ysaac alle thingis whiche he hadde do;
Tsono wantchito uja anawuza Isake zonse zimene anazichita.
67 which Ysaac ledde hir in to the tabernacle of Sare, his modir, and took hir to wijf; and so myche he louede hir, that he temperide the sorewe which bifelde of the deeth of the modir.
Isake analowa naye Rebeka mu tenti ya amayi ake Sara, ndipo anakhala mkazi wake. Isake anamukonda kwambiri Rebeka mkazi wake motero kuti zimenezi zinamutonthoza imfa ya amayi ake.

< Genesis 24 >