< Genesis 23 >

1 Forsothe Sare lyuede an hundrid and seuene and twenti yeer,
Sara anakhala ndi moyo zaka 127.
2 and diede in the citee of Arbee, which is Ebron, in the lond of Chanaan; and Abraham cam to biweyle and biwepe hir.
Anamwalirira ku Kiriyati-Araba, kumeneku ndi ku Hebroni, mʼdziko la Kanaani, ndipo Abrahamu anapita kukakhuza maliro a Sara, namulirira.
3 And whanne he hadde rise fro the office of the deed bodi, he spak to the sones of Heth, and seide,
Kenaka Abrahamu ananyamuka pamene panali mtembo wa mkazi wakepo kupita kukayankhula ndi anthu a ku Hiti. Ndipo anati,
4 Y am a comelyng and a pilgrym anentis you; yyue ye to me riyt of sepulcre with you, that Y birie my deed body.
“Ine ndine mlendo wongoyendayenda kwanu kuno. Bwanji mundigulitse malo woti akhale manda kuti ndiyikepo thupi la mkazi wanga.”
5 And the sones of Heth answeriden, and seiden, Lord, here thou vs;
Anthu a ku Hiti aja anamuyankha Abrahamu kuti,
6 thou art the prince of God anentis vs; birie thou thi deed bodi in oure chosun sepulcris, and no man schal mow forbede thee, that ne thou birie thi deed bodi in the sepulcre of him.
“Tatimverani mbuye wathu, inu ndinu mwana wa mfumu wamkulu pakati pathu. Chonde ikani thupi la mkazi wanu mʼmanda aliwonse amene mungafune. Palibe mmodzi wa ife amene adzakukanizani manda ake kuti musayike mkazi wanu.”
7 And Abraham roos, and worschipide the puple of the lond, that is, the sones of Heth.
Tsono Abrahamu anayimirira naweramira anthu a dziko la Hiti aja
8 And he seide to hem, If it plesith youre soule that Y birie my deed bodi, here ye me, and preie ye for me to Efron, the sone of Seor,
nati, “Ngati mwaloladi kuti ndiyike mkazi wanga kuno, ndiye ndimvereni. Mundipemphere kwa Efroni mwana wa Zohari
9 that he yyue to me the double caue, whiche he hath in the vttirmoste part of his feeld; for sufficiaunt money yyue he it to me bifore you into possessioun of sepulcre.
kuti andigulitse phanga la Makipela, limene lili kumapeto kwa munda wake. Mumupemphe kuti andigulitse pamtengo wake ndithu inu mukuona kuti akhale manda.”
10 Forsothe Efron dwellide in the myddis of the sones of Heth. And Efron answerde to Abraham, while alle men herden that entriden bi the yate of that citee,
Pamenepo nʼkuti Efroni Mhiti ali pomwepo pakati pa anthuwo amene anabwera ku chipata cha mzindawo. Ndipo onse akumva anamuyankha Abrahamu
11 and seide, My lord, it schal not be doon so, but more herkne thou that that Y seie; Y yyue to thee the feeld, and the denne which is therine, while the sones of my puple ben present; birie thou thi deed bodi.
nati, “Ayi mbuye wanga tandimverani, ine ndikukupatsani mundawo ndiponso phanga limene lili mʼmenemo. Ndikukupatsani malowa pamaso pa anthu a mtundu wanga. Chonde ikani mtembo wamkazi wanu.”
12 Abraham worschipide bifor the Lord, and bifor the puple of the lond,
Apo Abrahamu anaweramanso mwaulemu pamaso pa anthu a mʼdzikolo
13 and he spak to Efron, while his puple stood aboute, Y biseche, that thou here me; Y schal yyue money for the feeld, resseyue thou it, and so Y schal birie my deed bodi in the feeld.
ndipo anthu onse akumva Abrahamu anati kwa Efroni, “Ngati kungatheke, chonde ndimvereni. Ine ndichita kugula mundawu. Landirani ndalama za mundawu kuti ine ndiyike mkazi wanga mʼmenemo.”
14 And Efron answerde, My lord,
Koma Efroni anamuyankha Abrahamu nati,
15 here thou me, the lond which thou axist is worth foure hundrid siclis of siluer, that is the prijs bitwixe me and thee, but hou myche is this? birie thou thi deed bodi.
“Mundimvere mbuye wanga; mundawo mtengo wake ndi masekeli asiliva okwana 400. Koma zimenezo nʼchiyani pakati pa ine ndi inu? Ikani mtembo wa mkazi wanu.”
16 And whanne Abraham hadde herd this, he noumbride the monei which Efron axide, while the sones of Heth herden, foure hundrid siclis of siluer, and of preuyd comyn monei.
Abrahamu anavomera mtengo umene ananena Efroni Ahiti onse akumva ndipo anamuwerengera masekeli asiliva okwana 400 monga mwa mtengo wa ndalama umene amalonda a nthawi imeneyo ankagwiritsa ntchito.
17 And the feeld that was sumtyme of Efron, in which feeld was a double denne, biholdinge to Mambre, as wel thilke feeld as the denne and alle the trees therof, in alle termes therof bi cumpas, was confermed to Abraham in to possessioun,
Choncho munda wa Efroni wa ku Makipela umene unali kufupi ndi Mamre, kuphatikiza munda, phanga linali mʼmenemo pamodzi ndi mitengo yonse ya mʼmundamo, zinaperekedwa
18 while the sones of Heth seiyen and alle men that entriden bi the yate of that citee.
kwa Abrahamu ngati chuma chake pamaso pa anthu onse a ku Hiti amene anabwera ku chipata cha mzindawo.
19 And so Abraham biriede Sare, his wijf, in the double denne of the feeld, that bihelde to Mambre; this is Ebron in the lond of Chanaan.
Zitatha izi, Abrahamu anayika mkazi wake Sara mʼphanga la mʼmunda wa ku Makipela, kufupi ndi ku Mamre (kumene ndi ku Hebroni) mʼdziko la Kanaani.
20 And the feeld, and the denne that was therynne, was confermyd of the sones of Heth to Abraham, in to possessioun of sepulcre.
Choncho Ahiti anapereka munda pamodzi ndi phanga la mʼmenemo kwa Abrahamu kuti akhale manda.

< Genesis 23 >