< Genesis 26 >

1 Forsothe for hungur roos on the lond, aftir thilke bareynesse that bifelde in the daies of Abraham, Isaac yede forth to Abymelech, kyng of Palestyns, in Gerara.
Tsono kunagwa njala ina mʼdzikomo kuwonjezera pa ija ya poyamba ya nthawi ya Abrahamu ndipo Isake anapita kwa Abimeleki mfumu ya Afilisti ku Gerari.
2 And the Lord apperide to hym, and seide, Go not doun in to Egipt, but reste thou in the lond which Y schal seie to thee,
Yehova anadza kwa Isake nati, “Usapite ku Igupto; koma ukhale mʼdziko limene ndidzakuwuza kuti ukakhalemo.
3 and be thou a pilgrym ther ynne; and Y schal be with thee, and Y schal blesse thee; for Y schal yyue alle these cuntrees to thee and to thi seed, and Y schal fille the ooth which Y bihiyte to Abraham, thi fadir.
Khala mʼdziko lino ndipo ndidzakhala nawe ndi kukudalitsa. Pakuti kwa iwe ndi zidzukulu zako ndidzapereka mayiko onsewa. Choncho ndidzakwaniritsa pangano limene ndinalumbira kwa Abrahamu, abambo ako.
4 And Y schal multiplie thi seed as the sterris of heuene, and Y schal yyue alle these thingis to thin eyris, and alle folkis of erthe schulen be blessid in thi seed, for Abraham obeide to my vois,
Zidzukulu zako ndidzazichulukitsa ngati nyenyezi za mu mlengalenga ndi kuzipatsa mayiko onsewa. Ndiponso anthu onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa zidzukulu zako,
5 and kepte `my preceptis and comaundementis, and kepte cerymonyes and lawis.
chifukwa Abrahamu anandimvera, nasunga malamulo anga onse.”
6 And so Ysaac dwellide in Geraris.
Choncho Isake anakhala ku Gerari.
7 And whanne he was axid of men of that place of his wijf, he answarde, Sche is my sistir; for he dredde to knowleche that sche was felouschipid to hym in matrymonye, and gesside lest peraduenture thei wolden sle him for the fairnesse of hir.
Anthu akumaloko atafunsa Isake za mkazi wake, iye anati, “Ndi mlongo wanga ameneyu.” Iye anaopa kunena kuti, “Ndi mkazi wanga ameneyu,” popeza ankaganiza kuti anthu akumeneku akhoza kumupha ndi kukwatira mkazi wake popeza Rebeka anali wokongola.
8 And whanne ful many daies weren passid, and he dwellide there, Abymelech, kyng of Palestyns, bihelde bi a wyndow, and seiy hym pleiynge with Rebecca, his wijf.
Isake atakhalako kumeneko nthawi yayitali, Abimeleki mfumu ya Afilisti, anasuzumira pa zenera kuyangʼana kunja, ndipo anaona Isake akugwiragwira Rebeka, mkazi wake.
9 And whanne Isaac was clepid, the kyng seide, It is opyn, that sche is thi wijf; whi liedist thou, that sche was thi sistir? Isaac answerde, Y dredde, lest Y schulde die for hir.
Choncho Abimeleki anamuyitanitsa Isake nati, “Uyu ndi mkazi wako ndithu! Nanga bwanji umati, ‘Ndi mlongo wanga’?” Ndipo Isake anamuyankha kuti, “Ine ndimaganiza kuti ndingataye moyo wanga chifukwa cha iyeyu.”
10 And Abymelech seide, Whi hast thou disseyued vs? Sum man of the puple myyte do letcherie with thi wijf, and thou haddist brouyt in greuous synne on vs. And the kyng comaundide to al the puple,
Tsono Abimeleki anati, “Nʼchiyani chimene watichitira? Mmodzi mwa anthuwa anatsala pangʼono kugona ndi mkazi wako ndipo ukanatisandutsa ife kukhala olakwa.”
11 and seide, He that touchith the wijf of this man schal die bi deeth.
Choncho Abimeleki analamula anthu ake onse nati, “Aliyense amene avutitse munthu uyu pamodzi ndi mkazi wake adzaphedwa ndithu.”
12 Forsothe Isaac sowide in that lond, and he foond an hundrid fold in that yeer; and the Lord blesside hym.
Isake anadzala mbewu mʼmunda, ndipo chaka chomwecho anakolola zinthu zambiri chifukwa Yehova anamudalitsa.
13 And the man was maad riche, and he yede profitynge and encreessynge til he was maad ful greet.
Isake analemera. Chuma chake chinkachulukirachulukira mpaka anasanduka munthu wolemera kwambiri.
14 Also he hadde possessioun of scheep and grete beestis, and ful myche of meyne. For this thing Palestyns hadden enuye to hym,
Anali ndi nkhosa, ngʼombe ndi antchito ambiri mwakuti Afilisti anamuchitira nsanje.
15 and thei stoppiden in that tyme and filliden with erthe alle the pittis whiche the seruauntis of Abraham his fadir hadden diggid,
Nthawi iyi nʼkuti Afilisti atakwirira ndi dothi zitsime zonse zimene antchito abambo ake Abrahamu anakumba mu nthawi ya abambo akewo.
16 in so myche that Abymelech him silf seide to Ysaac, Go thou awei fro vs, for thou art maad greetly myytier than we.
Ndipo Abimeleki anati kwa Isake, “Muchoke pakati pathu chifukwa mwasanduka wamphamvu kuposa ife.”
17 And he yede awei, that he schulde come to the stronde of Gerare, and dwelle there.
Choncho Isake anachokako kumeneko nakakhala ku chigwa cha Gerari kumene anakhazikikako.
18 And he diggide eft other pittis, whiche the seruauntis of Abraham his fadir hadden diggid, and whiche the Filisteis hadden stoppid sumtyme, whanne Abraham was deed; and he clepide tho pittis bi the same names, bi whiche his fadir hadde clepid bifore.
Isake anafukulanso zitsime zija zimene zinakumbidwa mu nthawi ya abambo ake Abrahamu. Atamwalira Abrahamu, Afilisti anakwirira zitsimezi. Tsono anazitcha mayina omwewo amene abambo ake anazitcha.
19 Thei diggiden in the stronde, and thei founden wellynge watir.
Antchito a Isake anakumba mʼchigwamo ndipo anapezamo kasupe wa madzi.
20 But also strijf of scheepherdis of Gerare was there ayens the scheepherdis of Isaac, and thei seiden, The watir is oure; wherfor of that that bifelde he clepide the name of the pit fals chaleng.
Koma abusa a ku Gerari anakangana ndi abusa a Isake nati, “Madziwa ndi athu.” Motero iye anachitcha chitsimecho Mkangano chifukwa anakangana naye.
21 And thei diggiden anothir, and thei stryueden also for that, and Ysaac clepide that pit enemytes.
Kenaka iwo anakumba chitsime china, koma anakangananso chifukwa cha chitsimecho. Choncho anachitcha dzina lakuti Chidani.
22 And he yede forth fro thennus, and diggide another pit, for which thei stryueden not, therfor he clepid the name of that pit largenesse; and seide, Now God hath alargid vs, and hath maad to encreesse on erthe.
Anachokapo pamenepo nakakumba china. Koma apa sanakanganiranenso ndi munthu. Iye anachitcha Kutakasuka, nati, “Tsopano Yehova watipatsa ife malo otakasukirako ndipo tilemera muno.”
23 Forsothe he stiede fro that place in to Bersabee,
Kenaka Isake anachoka ku malo kuja kupita ku Beeriseba.
24 where the Lord God apperide to him in that nyyt; and seide, Y am God of Abraham, thi fadir; nyle thou drede, for Y am with thee, and Y schal blesse thee, and Y schal multiplie thi seed for my seruaunt Abraham.
Usiku umenewo Yehova anadza kwa Isake nati, “Ine ndine Mulungu wa abambo ako Abrahamu. Usachite mantha popeza Ine ndili ndi iwe. Ndidzakudalitsa ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri chifukwa cha mtumiki wanga Abrahamu.”
25 And so Ysaac bildide ther an auter to the Lord; and whanne the name of the Lord was inwardli clepid, he stretchide forth a tabernacle; and he comaundide hise seruauntis that thei schulden digge pittis.
Isake anamanga guwa lansembe pamenepo ndipo anapembedza Yehova. Pomwepo anamanga tenti yake, ndipo antchito ake anakumba chitsime.
26 And whanne Abymelech, and Ochosat, hise frendis, and Ficol, duk of knyytis, hadden come fro Geraris to that place,
Abimeleki pamodzi ndi Ahuzati mlangizi wake ndi Fikolo mkulu wa ankhondo ake anabwera kwa Isake kuchokera ku Gerari.
27 Isaac spak to hem, What camen ye to me, a man whom ye hatiden, and puttiden awei fro you?
Tsopano Isake anawafunsa kuti, “Bwanji mwabwera kwa ine, popeza munandichitira nkhanza ndi kundithamangitsa?”
28 Whiche answeriden, We seiyen that God is with thee, and therfor we seiden now, An ooth be bitwixe vs, and make we a couenaunt of pees,
Iwo anayankha, “Tsopano tadziwa kuti Yehova anali ndi iwe; ndiye taganiza kuti inu ndi ife tichite lumbiro. Ife tichite pangano ndi inu
29 that thou do not ony yuel to vs, as we touchiden `not ony thing of thine, nethir diden that that hirtide thee, but with pees we leften thee encressid bi the blessyng of the Lord.
kuti inu simudzatichitira zoyipa monga ifenso sitinakuchitireni nkhondo. Ife tinakuchitirani zabwino zokhazokha, ndipo tinakulolani kuti musamuke kuchoka kwathu mu mtendere. Tsopano Yehova wakudalitsani.”
30 Therfor Isaac made a feeste to hem; and after mete and drynk thei risen eerli,
Tsono Isake anawakonzera phwando, ndipo anadya ndi kumwa.
31 and sworen ech to other; and Isaac lefte hem peisibli in to her place.
Mmawa wake aliyense analumbira pangano kwa mnzake. Tsono Isake anawalola kuti anyamuke ndipo anamusiya mu mtendere.
32 Lo! forsothe in that dai the seruauntis of Ysaac camen, tellynge to him of the pit which thei hadden diggid, and seiden, We han foundun watir.
Tsiku limenelo, antchito a Isake anabwera namuwuza za chitsime chimene anakumba. Iwo anati, “Tawapeza madzi!”
33 Wherfor Ysaac clepide that pit abundaunce; and the name of the citee was set Bersabee til in to present dai.
Iye chitsimecho anachitcha Pangano. Nʼchifukwa chake mzindawu umatchedwa Beeriseba mpaka lero.
34 Esau forsothe fourti yeer eld weddide twei wyues, Judith, the douytir of Beeri Ethei, and Bethsamath, the douyter of Elon, of the same place;
Pamene Esau anali ndi zaka 40, anakwatira Yuditi mwana wamkazi wa Beeri Mhiti. Anakwatiranso Basemati mwana wa mkazi wa Eloni Mhiti.
35 whiche bothe offendiden the soule of Isaac and of Rebecca.
Akazi awiriwa anasandutsa Isake ndi Rebeka kukhala ndi moyo wa madandawulo nthawi zonse.

< Genesis 26 >