< Exodus 38 >

1 He made also the auter of brent sacrifice of the trees of Sechym, of fyue cubitis bi square, and of thre cubitis in heiythe;
Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229.
2 whose hornes camen forth of the corneris, and he hilide it with platis of bras.
Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa.
3 And in to vsis therof he made redi of bras dyuerse vessels, caudruns, tongis, fleischhokis, hokis, and `resseittis of firis.
Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
4 He made also the brasun gridile therof, `bi the maner of a net, and a `panne for colis vndur it, in the myddis of the auter.
Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo.
5 And he yetide foure ryngis, by so many endis of the gridile, to putte in the barris to bere;
Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira.
6 and he made tho same barris of the trees of Sechym, and hilide with platis of bras.
Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa.
7 And ledde in to the serclis that stonden forth in the sidis of the auter. Forsothe thilke auter was not sad, but holowe of the bildyngis of tablis, and voide with ynne.
Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.
8 He made also a `greet waischyng vessel of bras, with his foundement, of the myrours of wymmen that wakiden in the `greet street of the tabernacle.
Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
9 And he made the greet street, in whose south coost weren tentis of bijs foldid ayen, of an hundrid cubitis, twenti brasun pilers with her foundementis,
Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
10 the heedis of pilers, and al the grauyng of the werk, weren of siluer;
Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
11 euenli at the north coost the tentis, pilers, and foundementis and heedis of pilers, weren of the same mesure, and werk, and metal.
Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
12 Forsothe in that coost that biholdith the west weren tentis of fyfty cubitis, ten brasun pilers with her foundementis, and the `heedis of pilers, and al the grauyng of werk, weren of siluer.
Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
13 Sotheli ayens the eest he made redi tentis of fifti cubitis,
Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23.
14 of whiche tentis o side helde fiftene cubitis of thre pilers with her foundementis; and in the tother side,
Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu,
15 for he made the entryng of the tabernacle bitwixe euer either, weren tentis euenli of fiftene cubitis, thre pilers, and so many foundementis.
polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
16 Bijs foldid ayen hilide alle the tentis of the greet street.
Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino.
17 The foundementis of pilers weren of bras; forsothe the heedis of tho pilers, with alle her grauyngis, weren of siluer; but also he clothide with siluer tho pilers of the greet street.
Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.
18 And in the entryng therof he made a tente, bi `werk of broiderie, of iacynt, purpur, vermyloun, and of bijs foldid ayen, which tente hadde twenti cubitis in lengthe, and the heiythe was of fyue cubitis, bi the mesure which alle the tentis of the greet street hadden.
Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229,
19 Forsothe the pylers in the entryng weren foure, with brasun foundementis, and the heedis of tho pilers and grauyngis weren of siluer;
pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva.
20 and he made brasun stakis of the tabernacle, and of the greet street, bi cumpas.
Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.
21 These ben the instrumentis of the tabernacle of witnessyng, that ben noumbrid, bi the comaundement of Moises, in the cerymonyes of Leuytis, bi the hond of Ithamar, sone of Aaron, preest.
Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi:
22 Whiche instrumentis Beseleel, sone of Huri, sone of Hur, of the lynage of Juda, fillide; for the Lord comaundide bi Moises,
Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose,
23 while Ooliab, sone of Achysameth, of the lynage of Dan, was ioyned felowe to hym, and he hym silf was a noble crafti man of trees, and a tapesere and a broderere of iacynt, purpur, vermyloun and bijs.
pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala.
24 Al the gold that was spendid in the werk of seyntuarie, and that was offrid in yiftis, was of `nyne and twenti talentis, and of seuene hundrid and thretti siclis, at the mesure of seyntuarie.
Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.
25 Forsothe it was offrid of hem that passiden to noumbre fro twenti yeer and aboue, of sixe hundrid and thre thousand, and fyue hundrid and fifty of armed men.
Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika.
26 Ferthermore, an hundrid talentis of siluer weren, of whiche the foundementis of the seyntuarie weren yotun togidere, and of the entryng, where the veil hangith;
Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550.
27 an hundrid foundementis weren maad of an hundrid talentis, and for ech foundement was ordeyned o talent.
Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi.
28 Forsothe of a thousynde seuene hundrid and `thre scoor and fiftene siclis he made the heedis of pilers, and he `clothide tho same pilers with siluer.
Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.
29 Also of bras weren offrid `thre scoor and twelue thousynde talentis, and foure hundrid siclis ouer.
Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425.
30 Of whiche the foundementis in the entryng of the tabernacle of witnessyng weren yotun, and the brasun auter, with his gridele, and al the vessels that perteynen to the vss therof,
Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse,
31 and the foundementis of the greet street, as wel in the cumpas, as in the entryng therof, and the stakis of the tabernacle, and of the greet street bi cumpas.
matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.

< Exodus 38 >