< Exodus 39 >

1 Forsothe of iacynt, and purpur, vermyloun, and bijs, he made clothis, in whiche Aaron was clothid, whanne he mynystride in hooli thingis, as the Lord comaundide to Moises.
Anapanga zovala za ansembe, zovala potumikira ku malo wopatulika pogwiritsa ntchito nsalu ya mtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira. Anapanganso zovala zopatulika za Aaroni monga momwe Yehova analamulira Mose.
2 Therfor he made the `cloth on the schuldris of gold, iacynt, and purpur, and of reed selk twies died,
Popanga efodi, iwo anagwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yosalala yofewa.
3 and of bijs foldid ayen, bi werk of broiderie; also he kittide thinne goldun platis, and made thinne in to threedis, that tho moun be foldid ayen, with the warp of the formere colouris;
Anasula golide wopyapyala ndi kumulezaleza kuti alumikize kumodzi ndi nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yosalala yofewa yolukidwa mwaluso.
4 and he made tweyne hemmes couplid to hem silf to gidere, in euer either side of the endis; and `he made a girdil of the same colouris,
Iwo anapanga efodi imene inali ndi timalamba tiwiri ta pa mapewa, tosokerera ku msonga zake ziwiri kuti azitha kumanga.
5 as the Lord comaundide to Moises.
Lamba womangira efodi anali wolukidwa mwaluso ngati efodiyo. Anali nsalu imodzi ndi efodiyo, wopangidwa ndi golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
6 And he made redi twei `stonys of onychyn, boundun and closid in gold, and grauun bi the craft of worchere in iemmys, with the names of the sones of Israel; sixe names in o stoon, and sixe in the tother stoon, bi the ordre of her birthe.
Iwo anakonza miyala ya onikisi ndi kuyiika mu zoyikamo zake zagolide ndipo anazokota mayina a ana a Israeli monga amachitira pa chidindo.
7 And he settide tho stoonus in the sidis of the `clooth on the schuldris, in to a memorial of the sones of Israel, as the Lord comaundide to Moises.
Kenaka anayimangirira pa tinsalu ta mʼmapewa ta efodi tija ngati miyala ya chikumbutso cha ana a Israeli monga momwe Yehova analamulira Mose.
8 He made also the racional, `by werk of broiderie, bi the werk of the `cloth on the schuldris, of gold, iacynt, purpur, and reed selk twies died, and of biis foldid ayen; he made the racional foure cornerid,
Iwo anapanga chovala chapachifuwa mwaluso kwambiri. Anachipanga ngati efodi pogwiritsa ntchito golide, nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo, yofiira, yofewa yosalala ndi yolukidwa bwino.
9 double, of the mesure of foure fyngris.
Kutalika kwake kunali kofanana mbali zonse, mulitali masentimita 23, mulifupi masentimita 23, chinali chopinda pawiri.
10 And settide thereynne foure ordris of iemmes; in the firste ordre was sardius, topazius, smaragdus; in the secounde was carbuncle,
Kenaka anayikapo mizere inayi ya miyala yokongola kwambiri. Mzere woyamba anayika miyala ya rubi, topazi ndi berili;
11 safir, iaspis;
mzere wachiwiri anayikapo miyala ya emeradi, safiro ndi dayimondi;
12 in the thridde ordre was ligurie, achates, ametiste;
mzere wachitatu anayikapo miyala ya opera, agate ndi ametisiti;
13 in the fourthe ordre was crisolite, onochyn, and berille, cumpassid and enclosid with gold, bi her ordris.
mzere wachinayi anayikapo miyala ya topazi, onikisi ndi yasipa. Miyalayi anayiyika mu zoyikamo zagolide.
14 And tho twelue stonys weren grauyn with twelue names, of the lynage of Israel, alle stonys bi hem silf, bi the names of alle lynagis bi hem silf.
Miyalayo inalipo khumi ndi iwiri, uliwonse kuyimira dzina limodzi la ana a Israeli. Mwala uliwonse unazokotedwa ngati chidindo dzina limodzi la mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
15 Thei maden also in the racional litle chaynes, cleuynge to hem silf togidre,
Anapanga timaunyolo tagolide wabwino kwambiri ta pa chovala chapachifuwa, topota ngati chingwe.
16 of pureste gold, and tweyne hokys, and so many ryngis of gold. Forsothe thei settiden the ryngis on euer either side of the racional,
Anapanganso zoyikamo zake zagolide ndi mphete ziwiri zagolide, ndipo anamangirira mphetezo pa ngodya ziwiri za chovala chapachifuwa.
17 of whiche ryngis twei goldun chaynes hangiden, whiche thei settiden in the hokis, that stonden forth in the corneris of the `cloth on the schuldris.
Anamangirira timaunyolo tiwiri tagolide tija pa mphete za pa ngodya pa chovala chapachifuwacho.
18 These acordiden so to hem silf, bothe bifore and bihynde, that the `cloth on the schuldris, and the racional,
Ndipo mbali ina ya timaunyoloto anamangirira pa zoyikapo zake ziwiri zija, ndi kulumikiza pa tinsalu takutsogolo kwa mapewa a efodi.
19 weren knyt togidere, fastned to the girdil, and couplid ful strongli with ryngis, whiche ryngis a lace of iacynt ioynede togidere, lest tho weren loose, and `fletiden doun, and weren moued ech from other, as the Lord comaundide to Moises.
Anapanganso mphete ziwiri zagolide ndipo analumikiza ku ngodya ziwiri zamʼmunsi mwa chovala chapachifuwa, champhepete mwake, mʼkati pafupi ndi efodi ija.
20 Thei maden also `a coote on the schuldris, al of iacynt;
Kenaka anapanga mphete zina ziwiri zagolide ndi kuzilumikiza kumunsi kwa tinsalu takutsogolo kwa efodi, pafupi ndi msoko, pamwamba pangʼono pa lamba wamʼchiwuno wa efodi.
21 and the hood in the hiyere part, aboute the myddis, and a wouun hemme, bi the cumpas of the hood;
Anamangirira mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi ija monga Yehova analamulira Mose.
22 forsothe bynethe at the feet piyn applis of iacynt, and purpur, and vermyloun, and biys foldid ayen;
Anayipangira efodiyo mkanjo wamtundu wa mtambo, wolukidwa ndi mmisiri waluso.
23 and litle bellis of pureste gold, whiche thei settiden bitwixe pum garnadis, in the `lowest part of the coote, bi cumpas;
Mkanjowo unali ndi malo opisapo mutu pakati pakepo. Pa chibowopo panali chibandi chosokedwa mochita ngati kuluka monga muja akhalira malaya kuti chibowocho chilimbe, chisangʼambike.
24 a goldun litle belle, and a piyn apple; with whiche the bischop yede ourned, whanne he `was set in seruyce, as the Lord comaundide to Moises.
Pa mpendero wamʼmunsi wa mkanjowo, analumikiza mphonje zokhala ngati makangadza za nsalu yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira yofewa yosalala ndi yopetedwa bwino yomwe inazungulira mkanjo.
25 Thei maden also cootis of bijs, bi wouun werk, to Aaron and to hise sones,
Ndipo anapanga maberu agolide wabwino kwambiri ndipo analumikiza mozungulira mpendero pakati pa makangadzawo.
26 and mytres with smale corouns of biys,
Kotero panali mphonje imodzi ndi belu limodzi kuzungulira mpendero wa mkanjo wovala potumikira monga momwe Yehova analamulira Mose.
27 and lynnun clothis of bijs;
Kwa Aaroni ndi ana ake anawapangira minjiro ya nsalu yofewa yosalala, yolukidwa bwino ndi munthu waluso,
28 forsothe a girdil of bijs foldid ayen, of iacynt, purpur, and vermyloun, departid bi craft of broyderie, as the Lord comaundide to Moises.
nduwira ya nsalu yofewa yosalala, lamba wa nsalu yofewa yosalala, womanga mʼmutu, ndi makabudula amʼkati a nsalu yofewa yosalala olukidwa bwino.
29 Thei maden also a plate of hooli worschipyng, of pureste gold, and thei writeden therynne bi werk of a worchere in iemmes, The hooli of the Lord.
Anapanga lamba wolukidwa bwino wa nsalu yofewa ndi yosalala ya mtundu wa mtambo yapepo ndi yofiira. Ili linaliluso la munthu wopanga zokometsera monga Yehova analamulira Mose.
30 And thei bounden it with the mytre bi a lace of iacynt, as the Lord comaundide to Moises.
Iwo anapanga duwa lagolide wabwino kwambiri ngati chidindo ndipo anazokotapo mawu akuti, Wopatulikira Yehova.
31 Therfor al the werk of the tabernacle, and the hilyng of the witnessyng, was parformed; and the sones of Israel diden alle thingis whiche the Lord comaundide to Moises.
Kenaka analimangira ndi chingwe cha nsalu yamtundu wa mtambo pa nduwira, monga momwe Yehova analamulira Mose.
32 And thei offeriden the tabernacle, and the roof, and al the purtenaunce, ryngis, tablis, barris, pileris, and foundementis;
Tsopano ntchito yonse ya tenti ya msonkhano inatha. Aisraeli anachita zonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
33 the hilyng of `skynnes of rammes, maad reed, and another hilyng of skynnys of iacynt;
Kenaka anabweretsa chihema kwa Mose. Tenti ndi zipangizo zake, ngowe zake, maferemu ake, mitanda yake, mizati yake ndi matsinde ake;
34 the veil, the arke, barris, propiciatorie;
chophimba cha chikopa cha nkhosa yayimuna chonyikidwa mu utoto ofiira, chophimba cha chikopa cha akatumbu ndi nsalu zophimba;
35 the boord with vessels, and with the looues of settyng forth;
bokosi la umboni pamodzi ndi mitengo yake yonyamulira ndiponso chovundikira chake;
36 the candilstike, lanternes, and the purtenauncis of tho, with oile;
tebulo pamodzi ndi zipangizo zake ndiponso buledi wokhala pamaso pa Yehova;
37 the goldun auter, and oynement, and encense of swete smellynge spiceries;
choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri pamodzi ndi nyale zake ndi zipangizo zake zonse, ndiponso mafuta anyalezo;
38 and the tente in the entryng of the tabernacle;
guwa lagolide, mafuta odzozera, lubani onunkhira ndi nsalu yotchinga pa khomo lolowera mu tenti;
39 the brasun auter, gridile, barris, and alle vessels therof; the `greet waischyng vessel, with his foundement; the tentis of the greet street, and the pilers with her foundementis;
guwa lamkuwa ndi sefa yamkuwa, mitengo yake yonyamulira ndi zipangizo zake zonse; beseni ndi miyendo yake;
40 the tente in the entring of the greet street, and the coordis, and stakis therof. No thing of the vessels failide, that weren comaundid to be maad in to the seruyce of the tabernacle, and in to the roof of the boond of pees.
nsalu yotchingira bwalo pamodzi ndi mizati yake ndi matsinde ake ndiponso nsalu yotchingira pa khomo lolowera ku bwalo; zingwe zake ndi zikhomo za tenti; zipangizo zonse za chihema, tenti ya msonkhano;
41 Also the sones of Israel offriden the clothis whiche the prestis, that is, Aaron and hise sones, vsen in the seyntuarie,
ndiponso zovala zolukidwa zovala potumikira kumalo opatulika, zovala zopatulika za wansembe, Aaroni pamodzi ndi za ana ake aamuna pamene akutumikira monga ansembe.
42 as the Lord comaundide.
Aisraeli anagwira ntchito yonse monga momwe Yehova analamulira Mose.
43 And aftir that Moises siy alle tho thingis fillid, he blesside hem.
Mose anayendera ntchitoyo ndipo anaona kuti anayichita monga momwe Yehova analamulira. Kotero Mose anawadalitsa.

< Exodus 39 >