< Exodus 37 >

1 Forsothe Beseleel made also an arke of the trees of Sechym, hauynge twey cubitis and an half in lengthe, and a cubit and an half in breede; forsothe the hiynesse was of o cubit and an half; and he clothide the arke with purest gold, with ynne and without forth.
Bezaleli anapanga Bokosi la Chipangano lamatabwa amtengo wa mkesha. Kutalika kwake kunali masentimita 114, mulifupi mwake munali masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69.
2 And he made to it a goldun coroun `bi cumpas,
Iye analikuta bokosilo ndi golide wabwino kwambiri mʼkati mwake ndi kunja komwe. Anapanganso mkombero wagolide kuzungulira bokosilo.
3 and yetide foure goldun ryngis, bi foure corneris therof, twey ryngis in o side, and twei ryngis in the tother side.
Iye anapanga mphete zinayi zagolide ndi kuzimangirira ku miyendo yake inayi ija, mbali ina ziwiri ndi mbali inanso ziwiri.
4 And he made barris of the trees of Sechym, whiche barris he clothide with gold,
Kenaka anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide.
5 and whiche barris he putte into the ryngis that weren in the sidis of the arke, to bere it.
Ndipo analowetsa nsichizo mʼmphete zija za mbali zonse ziwiri za bokosilo kuti azinyamulira.
6 He made also a propiciatorie, that is, Goddis answeryng place, of pureste gold, of twei cubitis and an half in lengthe, and of o cubit and an half in breede.
Iye anapanga chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69.
7 Also he made twei cherubyns of gold, betun out with hamer, whiche he settide on euer eithir side of the propiciatorie,
Ndipo anapanga Akerubi awiri agolide osula ndi nyundo ndi kuwayika mbali ziwiri za chivundikirocho.
8 o cherub in the hiynesse of o part, and the tother cherub in the hiynesse of the tothir part; twei cherubyns, oon in ech hiynesse of the propiciatorie, stretchynge out the wengis,
Iye anapanga kerubi mmodzi mbali ina ndi wina mbali inayo. Akerubiwa anawapangira limodzi ndi chivundikirocho mʼmapeto mwa mbali ziwirizo.
9 and hilynge the propiciatorie, and biholdynge hem silf togidere and that.
Mapiko a Akerubiwo anatambasukira pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo kuti achiphimbe. Akerubiwo anakhala choyangʼanana, aliyense kuyangʼana chivundikirocho.
10 He made also a boord of `the trees of Sechym, in the lengthe of twey cubitis, and in the breede of o cubit, whiche boord hadde `a cubit and an half in heiythe.
Iwo anapanga tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69.
11 And he cumpaside the boord with clenneste gold, and made to it a goldun brynke bi cumpas;
Kenaka analikuta ndi golide wabwino kwambiri, ndipo anapanga mkombero wagolide mʼmbali mwake.
12 and he made to that brynke a goldun coroun, rasid bitwixe of foure fyngris; and on the same coroun he made anothir goldun coroun.
Iwo anapanga feremu yozungulira tebulo, mulifupi mwake ngati chikhatho cha dzanja, ndipo anayika mkombero wagolide kuzungulira feremuyo.
13 Also he yetide foure goldun serclis whiche he settide in foure corneris,
Iwo anapanga mphete zinayi zagolide ndipo anazilumikiza ku ngodya zake zinayi, kumene kunali miyendo yake inayi.
14 bi alle the feet of the boord ayens the coroun, and he puttide barris in to the serclis, that the `boord may be borun.
Mphetezo anaziyika kufupi ndi feremu kuti azikolowekamo nsichi zonyamulira tebuloyo.
15 And he made tho barris of the trees of Sechym, and cumpasside tho with gold.
Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide kuti azinyamulira tebulolo.
16 And he made vesselis to dyuerse vsis of the boord, vessels of vynegre, violis, and litle cuppis, and censeris of pure gold, in whiche the fletynge sacrifices schulen be offrid.
Ndipo anapanga ziwiya za pa tebulolo zagolide wabwino, mbale ndi zipande, mitsuko ndi mabeseni zogwiritsa ntchito popereka nsembe za chakumwa.
17 And he made a candilstike, betun out with hamer, of clenneste gold, of whos barre yerdis, cuppis, and litle rundelis and lilies camen forth;
Iwo anapanga choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri. Tsinde lake ndi mphanda zake zinasulidwa ndi nyundo. Zikho zake zokhala ndi mphukira ndi maluwa ake zinapangidwa kumodzi.
18 sixe in euer eithir side, thre yerdis on o side, and thre on the tother side; thre cuppis in the maner of a note bi ech yerde, and litle rundels to gidere, and lilies;
Mʼmbali mwake munali mphanda zisanu ndi imodzi, zitatu mbali iliyonse.
19 and thre cuppis at the licnesse of a note in the tother yerde, and litle rundels to gidere, and lilies; forsothe the werk of sixe schaftis, that camen forth of the `stok of the candilstike, was euene.
Zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa zinali pa mphanda yoyamba. Pa mphanda yachiwiri panalinso zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa. Ndipo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zinali chimodzimodzi ndipo zinatuluka mʼchoyikapo nyalecho.
20 Sotheli in that barre weren foure cuppis, in the maner of a note, and litle rundels and lilies weren bi alle cuppis;
Pa choyikapo nyalecho panali zikho zinayi zokhala ngati maluwa amtowo, mphukira ndi maluwa ake.
21 and litle rundels vndur twei schaftis, bi thre placis, whiche to gidre be maad sixe schaftis comynge forth of o barre;
Mphukira yoyamba inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zoyamba za pa choyikapo nyale. Mphukira yachiwiri inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zinazo. Mphukira yachitatu inali mʼmunsi mwa nthambi zina ziwirinso. Zonse pamodzi zinali nthambi zisanu ndi imodzi
22 therfor and the litle rundels, and schaftis therof, weren alle betun out with hamer, of pureste gold.
Mphukira ndi nthambi zonse zinasulidwa kumodzi ndi choyikapo nyalecho ndi golide wabwino kwambiri.
23 He made also seuene lanternes, with her `snytyng tongis, and the vessels where `tho thingis, that ben snytid out, ben quenchid, of clennest gold.
Iwo anapanga nyale zisanu ndi ziwiri, mbaniro ndi zowolera phulusa, zonse zinali zagolide wabwino kwambiri.
24 The candilstike with alle his vessels weiyede a talent of gold.
Iwo anapanga choyikapo nyale ndi zipangizo zake zonse zagolide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34.
25 He made also the auter of encense, of trees of Sechym, hauynge a cubit bi square, and twei cubitis in heiythe, of whos corneris camen forth hornes.
Iwo anapanga guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani. Linali lofanana mbali zonse, mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91, ndipo nyanga zake zinapangidwa kumodzi ndi guwalo.
26 And he clothide it with clenneste gold, and the gridele, and wallis, and hornes;
Iwo anakuta guwa lonse ndi golide wabwino kwambiri, pamwamba pake, mbali zonse ndi nyanga zake, ndipo anapanga mkombero wagolide kuzungulira guwalo.
27 and he made to it a litil goldun coroun bi cumpas, and twei goldun ryngis vndur the coroun, bi ech syde, that barris be put in to tho, and the auter mow be borun.
Anapanga mphete ziwiri pansi pa mkomberowo ndi kulumikiza ku mbali zonse ziwiri kuti apisemo nsichi zonyamulira.
28 Forsothe he made tho barris of the trees of Sechym, and hilide with goldun platis.
Anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndipo anayikuta ndi golide.
29 He made also oile to the oynement of halewyng, and encense of swete smellynge spiceries, moost clene, bi the werk of `a makere of oynement.
Iwo anapanganso mafuta opatulika odzozera ndi zofukiza za fungo lokoma kwambiri. Iyi inali ntchito ya mʼmisiri waluso lopanga zonunkhiritsa.

< Exodus 37 >