< Masalimo 71 >

1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
U tebe se, Gospode, uzdam, nemoj me ostaviti pod sramotom vjeènom.
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
Pravdom svojom izbavi me, i oprosti me, prigni k meni uho svoje i pomozi mi.
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Budi mi grad gdje bih svagda dolazio da živim, uredi spasenje moje; jer si ti grad moj i krjepost moja.
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
Bože moj! uzmi me iz ruke bezbožnikove, iz ruke bezakonikove i nasilnikove.
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
Jer si ti nadanje moje, Gospod je Gospod pouzdanje moje od mladosti moje.
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
Tebe se držim od roðenja, od utrobe matere moje ti si braniè moj; tobom se hvalim svagda.
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
Èudo sam mnogima, a ti si utoèište moje jako.
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
Usta su moja puna hvale tvoje, slave tvoje svaki dan.
9 Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
Nemoj me odbaciti pod starost, kad me izdaje snaga moja, nemoj me ostaviti.
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
Jer neprijatelji moji misle o meni, i koji vrebaju dušu moju dogovaraju se,
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
Govoreæi: Bog ga je ostavio, potjerajte i uhvatite ga, jer ga nema ko izbaviti.
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
Bože! Ne budi daleko od mene; Bože moj! pohitaj mi u pomoæ.
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
Nek se postide i poginu protivnici duše moje; neka popadne stid i sramota na one koji mi traže zla!
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
A ja æu se svagda uzdati, i ponavljaæu hvale tebi.
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
Usta æe moja kazivati pravdu tvoju, svaki dan dobroèinstva tvoja, jer im ne znam broja.
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
Uæi æu u sili Gospoda Gospoda, i slaviæu samo tvoju pravdu.
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
Bože! ti si me uèio od mladosti, i do danas kazujem èudesa tvoja.
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
Ni u starosti i kad osijedjeh nemoj me ostaviti, Bože, eda bih kazivao mišicu tvoju natražju, svoj omladini silu tvoju.
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
Pravda je tvoja, Bože, do najviše visine; u velikim djelima, koja si uèinio, Bože, ko je kao ti?
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
Koliko si me puta bacao u velike i ljute nevolje, pak si me opet ostavio meðu živima i iz bezdana me zemaljskih opet izvadio.
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
Mnogo si me puta podizao i ponavljao utjehe.
22 Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
I ja te hvalim uz psaltir, tvoju vjernost, Bože moj; udaram ti u gusle, sveèe Izrailjev!
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
Raduju se usta moja kad pjevam tebi, i duša moja, koju si izbavio.
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.
I jezik moj svaki dan kazuje pravdu tvoju; jer su postiðeni i posramljeni koji mi traže zla.

< Masalimo 71 >