< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
Prièe Solomuna sina Davidova, cara Izrailjeva,
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
Da se poznaje mudrost i nastava, da se razumiju rijeèi razumne,
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
Da se prima nastava u razumu, u pravdi, u sudu i u svemu što je pravo,
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
Da se daje ludima razboritost, mladiæima znanje i pomnjivost.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
Mudar æe slušati i više æe znati, i razuman æe steæi mudrost,
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
Da razumije prièe i znaèenje, rijeèi mudrijeh ljudi i zagonetke njihove.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Poèetak je mudrosti strah Gospodnji; ludi preziru mudrost i nastavu.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
Slušaj, sine, nastavu oca svojega, i ne ostavljaj nauke matere svoje.
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
Jer æe biti vijenac od milina oko glave tvoje, i grivna na grlu tvom.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Sine moj, ako bi te mamili grješnici, ne pristaj;
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
Ako bi rekli: hodi s nama da vrebamo krv, da zasjedamo pravome ni za što;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
Proždrijeæemo ih kao grob žive, i svekolike kao one koji slaze u jamu; (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
Svakojakoga blaga dobiæemo, napuniæemo kuæe svoje plijena;
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
Bacaæeš ždrijeb svoj s nama; jedan æe nam tobolac biti svjema;
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
Sine moj, ne idi na put s njima, èuvaj nogu svoju od staze njihove.
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
Jer nogama svojim trèe na zlo i hite da proljevaju krv.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
Jer se uzalud razapinje mreža na oèi svakoj ptici;
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
A oni vrebaju svoju krv i zasjedaju svojoj duši.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
Taki su putovi svijeh lakomijeh na dobitak, koji uzima dušu svojim gospodarima.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Premudrost vièe na polju, na ulicama pušta glas svoj;
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
U najveæoj vrevi vièe, na vratima, u gradu govori svoje besjede:
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
Ludi, dokle æete ljubiti ludost? i potsmjevaèima dokle æe biti mio potsmijeh? i bezumni dokle æe mrziti na znanje?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Obratite se na karanje moje; evo, izasuæu vam duh svoj, kazaæu vam rijeèi svoje.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
Što zvah, ali ne htjeste, pružah ruku svoju, ali niko ne mari,
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
Nego odbaciste svaki savjet moj, i karanja mojega ne htjeste primiti;
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
Zato æu se i ja smijati vašoj nevolji, rugaæu se kad doðe èega se bojite;
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
Kad kao pustoš doðe èega se bojite, i pogibao vaša kao oluja kad doðe, kad navali na vas nevolja i muka.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Tada æe me zvati, ali se neæu odazvati; rano æe tražiti, ali me neæe naæi.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
Jer mrziše na znanje, i straha Gospodnjega ne izabraše;
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
Ne pristaše na moj svjet, i preziraše sva karanja moja.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Zato æe jesti plod od putova svojih, i nasitiæe se savjeta svojih.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
Jer æe lude ubiti mir njihov, i bezumne æe pogubiti sreæa njihova.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
Ali ko me sluša, boraviæe bezbrižno, i biæe na miru ne bojeæi se zla.

< Miyambo 1 >