< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Sine moj, ako primiš rijeèi moje, i zapovijesti moje sahraniš kod sebe,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
Da pazi uho tvoje na mudrost, i prigneš srce svoje k razumu,
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
Ako prizoveš mudrost, i k razumu podigneš glas svoj,
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
Ako ga ustražiš kao srebro, i kao sakriveno blago ako dobro ustražiš;
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
Tada æeš razumjeti strah Gospodnji, i poznanje Božije naæi æeš.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
Jer Gospod daje mudrost, iz njegovijeh usta dolazi znanje i razum.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
Èuva pravima što doista jest, štit je onima koji hode u bezazlenosti,
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
Da bi se držali staza pravijeh, a on èuva put svetaca svojih.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Tada æeš razumjeti pravdu i sud i što je pravo, i svaki dobri put.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
Kad doðe mudrost u srce tvoje, i znanje omili duši tvojoj,
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
Pomnjivost æe paziti na te, razum æe te èuvati,
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
Izbavljajuæi te od zla puta, od ljudi koji govore opake stvari,
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
Koji ostavljaju prave pute da idu putovima mraènijem,
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
Koji se raduju zlo èineæi, i igraju u zlijem opaèinama;
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
Kojih su putovi krivi, i sami su opaki na stazama svojim;
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
Izbavljajuæi te od žene tuðe, od tuðinke, koja laska svojim rijeèima,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
Koja ostavlja voða mladosti svoje, i zaboravlja zavjet Boga svojega.
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
Jer k smrti vodi dom njezin, i k mrtvima staze njezine.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
Ko god uðe k njoj ne vraæa se, niti izlazi na put životni.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
Zato hodi putem dobrijeh, i drži se staza pravednièkih.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Jer æe pravednici nastavati na zemlji, i bezazleni æe ostati na njoj.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
A bezbožni æe se istrijebiti sa zemlje, i bezakonici æe se išèupati iz nje.

< Miyambo 2 >