< Masalimo 53 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Mahalati. Ndakatulo ya Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Iwo ndi oyipa ndipo njira zawo ndi zonyansa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino.
To the ouercomer bi the quere, the lernyng of Dauid. The vnwise man seide in his herte; God is not. Thei ben `corrupt, and maad abhomynable in her wickidnessis; noon is that doith good.
2 Mulungu kumwamba amayangʼana pansi pano pa ana a anthu kuti aone ngati alipo wina wanzeru, wofunafuna Mulungu.
God bihelde fro heuene on the sones of men; that he se, if `ony is vndurstondynge, ether sekynge God.
3 Aliyense wabwerera, iwo onse pamodzi akhala oyipa; palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita chabwino, ngakhale mmodzi.
Alle boweden awei, thei ben maad vnprofitable togidre; noon is that doith good, ther is not til to oon.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa adzaphunziradi; anthu amene amadya anthu anga monga mmene anthu amadyera buledi, ndipo sapemphera kwa Mulungu?
Whether alle men, that worchen wickidnesse, schulen not wite; whiche deuouren my puple as the mete of breed?
5 Iwo anali pamenepo atathedwa nzeru ndi mantha aakulu pamene panalibe kanthu kochititsa mantha. Mulungu anamwazamwaza mafupa a anthu amene anakuthirani nkhondo; inuyo munawachititsa manyazi, pakuti Mulungu anawanyoza.
Thei clepiden not God; there thei trembliden for drede, where no drede was. For God hath scaterid the boones of hem, that plesen men; thei ben schent, for God hath forsake hem.
6 Ndithu, chipulumutso cha Israeli nʼchochokera ku Ziyoni! Pamene Mulungu adzabwezeretsanso ulemerero wa anthu ake, lolani Yakobo akondwere ndi Israeli asangalale!
Who schal yyue fro Syon helthe to Israel? whanne the Lord hath turned the caitifte of his puple, Jacob schal `ful out make ioie, and Israel schal be glad.

< Masalimo 53 >