< Masalimo 16 >

1 Mikitamu ya Davide. Ndisungeni Inu Mulungu, pakuti ine ndimathawira kwa Inu.
`Of the meke and symple, the salm of Dauid. Lord, kepe thou me, for Y haue hopid in thee;
2 Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga; popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”
Y seide to the Lord, Thou art my God, for thou hast no nede of my goodis.
3 Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko, amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.
To the seyntis that ben in the lond of hym; he made wondurful alle my willis in hem.
4 Anthu amene amathamangira kwa milungu ina mavuto awo adzachulukadi. Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.
The sikenessis of hem ben multiplied; aftirward thei hastiden. I schal not gadire togidere the conuenticulis, `ethir litle couentis, of hem of bloodis; and Y schal not be myndeful of her names bi my lippis.
5 Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa; mwateteza kolimba gawo langa.
The Lord is part of myn eritage, and of my passion; thou art, that schalt restore myn eritage to me.
6 Malire a malo anga akhala pabwino; ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.
Coordis felden to me in ful clere thingis; for myn eritage is ful cleer to me.
7 Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu; ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.
I schal blesse the Lord, that yaf vndurstondyng to me; ferthermore and my reynes blameden me `til to nyyt.
8 Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
I purueide euere the Lord in my siyt; for he is on the riythalf to me, that Y be not moued.
9 Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera; thupi langanso lidzakhala pabwino,
For this thing myn herte was glad, and my tunge ioyede fulli; ferthermore and my fleisch schal reste in hope.
10 chifukwa Inu simudzandisiya ku manda, simudzalola kuti woyera wanu avunde. (Sheol h7585)
For thou schalt not forsake my soule in helle; nether thou schalt yyue thin hooli to se corrupcioun. (Sheol h7585)
11 Inu mwandidziwitsa njira ya moyo; mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu, ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.
Thou hast maad knowun to me the weies of lijf; thou schalt fille me of gladnesse with thi cheer; delityngis ben in thi riythalf `til in to the ende.

< Masalimo 16 >