< Masalimo 15 >

1 Salimo la Davide. Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika? Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?
Lord, who schal dwelle in thi tabernacle; ether who schal reste in thin hooli hil?
2 Munthu wa makhalidwe abwino, amene amachita zolungama, woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,
He that entrith with out wem; and worchith riytfulnesse.
3 ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira, amene sachitira choyipa mnansi wake kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,
Which spekith treuthe in his herte; which dide not gile in his tunge. Nethir dide yuel to his neiybore; and took not schenschip ayens hise neiyboris.
4 amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa. Koma amalemekeza amene amaopa Yehova, amene amakwaniritsa zomwe walonjeza ngakhale pamene zikumupweteka,
A wickid man is brouyt to nouyt in his siyt; but he glorifieth hem that dreden the Lord. Which swerith to his neiybore, and disseyueth not;
5 amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa. Iye amene amachita zinthu zimenezi sadzagwedezeka konse.
which yaf not his money to vsure; and took not yiftis on the innocent. He, that doith these thingis, schal not be moued with outen ende.

< Masalimo 15 >