< Masalimo 17 >

1 Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
The preier of Dauid. Lord, here thou my riytfulnesse; biholde thou my preier. Perseuye thou with eeris my preier; not maad in gileful lippis.
2 Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
Mi doom come `forth of thi cheer; thin iyen se equite.
3 Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
Thou hast preued myn herte, and hast visitid in niyt; thou hast examynyd me bi fier, and wickidnesse is not foundun in me.
4 Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
That my mouth speke not the werkis of men; for the wordis of thi lippis Y haue kept harde weies.
5 Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
Make thou perfit my goyngis in thi pathis; that my steppis be not moued.
6 Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
I criede, for thou, God, herdist me; bowe doun thin eere to me, and here thou my wordis.
7 Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
Make wondurful thi mercies; that makist saaf `men hopynge in thee.
8 Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
Kepe thou me as the appil of the iye; fro `men ayenstondynge thi riyt hond. Keuere thou me vndur the schadewe of thi wyngis;
9 kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
fro the face of vnpitouse men, that han turmentid me. Myn enemyes han cumpassid my soule;
10 Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
thei han closide togidere her fatnesse; the mouth of hem spak pride.
11 Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
Thei castiden me forth, and han cumpassid me now; thei ordeyneden to bowe doun her iyen in to erthe.
12 Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
Thei, as a lioun maad redi to prey, han take me; and as the whelp of a lioun dwellynge in hid places.
13 Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
Lord, rise thou vp, bifor come thou hym, and disseyue thou hym; delyuere thou my lijf fro the `vnpitouse,
14 Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
delyuere thou thi swerd fro the enemyes of thin hond. Lord, departe thou hem fro a fewe men of `the lond in the lijf of hem; her wombe is fillid of thin hid thingis. Thei ben fillid with sones; and thei leften her relifis to her litle children.
15 Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.
But Y in riytfulnesse schal appere to thi siyt; Y schal be fillid, whanne thi glorie schal appere.

< Masalimo 17 >