< Masalimo 110 >

1 Salimo la Davide. Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti, “Khala ku dzanja langa lamanja mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.”
`The salm of Dauith. The Lord seide to my Lord; Sitte thou on my riyt side. Til Y putte thin enemyes; a stool of thi feet.
2 Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni; udzalamulira pakati pa adani ako.
The Lord schal sende out fro Syon the yerde of thi vertu; be thou lord in the myddis of thin enemyes.
3 Ankhondo ako adzakhala odzipereka pa tsiku lako la nkhondo. Atavala chiyero chaulemerero, kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha, udzalandira mame a unyamata wako.
The bigynnyng is with thee in the dai of thi vertu, in the briytnessis of seyntis; Y gendride thee of the wombe before the dai sterre.
4 Yehova walumbira ndipo sadzasintha maganizo ake: “Ndiwe wansembe mpaka muyaya monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”
The Lord swoor, and it schal not repente him; Thou art a preest with outen ende, bi the ordre of Melchisedech.
5 Ambuye ali kudzanja lako lamanja; Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.
The Lord on thi riyt side; hath broke kyngis in the dai of his veniaunce.
6 Adzaweruza anthu a mitundu ina, adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi.
He schal deme among naciouns, he schal fille fallyngis; he schal schake heedis in the lond of many men.
7 Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira; choncho adzaweramutsa mutu wake.
He dranke of the stronde in the weie; therfor he enhaunside the heed.

< Masalimo 110 >