< Masalimo 109 >

1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
To victorye, the salm of Dauid.
2 pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
God, holde thou not stille my preisyng; for the mouth of the synner, and the mouth of the gileful man is openyd on me.
3 Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
Thei spaken ayens me with a gileful tunge, and thei cumpassiden me with wordis of hatrede; and fouyten ayens me with out cause.
4 Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
For that thing that thei schulden loue me, thei bacbitiden me; but Y preiede.
5 Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
And thei settiden ayens me yuelis for goodis; and hatrede for my loue.
6 Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
Ordeyne thou a synner on him; and the deuel stonde on his riyt half.
7 Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
Whanne he is demed, go he out condempned; and his preier `be maad in to synne.
8 Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
Hise daies be maad fewe; and another take his bischopriche.
9 Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
Hise sones be maad faderles; and his wijf a widewe.
10 Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
Hise sones tremblinge be born ouer, and begge; and be cast out of her habitaciouns.
11 Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
An vsurere seke al his catel; and aliens rauysche hise trauelis.
12 Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
Noon helpere be to him; nether ony be that haue mercy on hise modirles children.
13 Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
Hise sones be maad in to perisching; the name of him be don awei in oon generacioun.
14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
The wickidnesse of hise fadris come ayen in to mynde in the siyt of the Lord; and the synne of his modir be not don awei.
15 Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
Be thei maad euere ayens the Lord; and the mynde of hem perische fro erthe.
16 Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
For that thing that he thouyte not to do merci,
17 Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
and he pursuede a pore man and beggere; and to slee a man compunct in herte.
18 Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
And he louede cursing, and it schal come to hym; and he nolde blessing, and it schal be maad fer fro him. And he clothide cursing as a cloth, and it entride as water in to hise ynnere thingis; and as oile in hise boonus.
19 Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
Be it maad to him as a cloth, with which he is hilyd; and as a girdil, with which he is euere gird.
20 Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
This is the werk of hem that bacbiten me anentis the Lord; and that speke yuels ayens my lijf.
21 Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
And thou, Lord, Lord, do with me for thi name; for thi merci is swete.
22 Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
Delyuere thou me, for Y am nedi and pore; and myn herte is disturblid with ynne me.
23 Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
I am takun awei as a schadowe, whanne it bowith awei; and Y am schakun awei as locustis.
24 Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
Mi knees ben maad feble of fasting; and my fleische was chaungid for oile.
25 Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
And Y am maad schenschipe to hem; thei sien me, and moueden her heedis.
26 Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
Mi Lord God, helpe thou me; make thou me saaf bi thi merci.
27 Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
And thei schulen wite, that this is thin hond; and thou, Lord, hast do it.
28 Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
Thei schulen curse, and thou schalt blesse, thei that risen ayens me, be schent; but thi seruaunt schal be glad.
29 Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
Thei that bacbiten me, be clothid with schame; and be thei hilid with her schenschipe as with a double cloth.
30 Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
I schal knouleche to the Lord greetli with my mouth; and Y schal herie hym in the myddil of many men.
31 Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.
Which stood nyy on the riyt half of a pore man; to make saaf my soule fro pursueris.

< Masalimo 109 >