< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
The song of `the salm of Dauid. Min herte is redi, God, myn herte is redi; Y schal singe, and Y schal seie salm in my glorie.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
My glorie, ryse thou vp, sautrie and harp, rise thou vp; Y schal rise vp eerli.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Lord, Y schal knouleche to thee among puplis; and Y schal seie salm to thee among naciouns.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
For whi, God, thi merci is greet on heuenes; and thi treuthe is til to the cloudis.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
God, be thou enhaunsid aboue heuenes; and thi glorie ouer al erthe.
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
That thi derlingis be delyuerid, make thou saaf with thi riythond, and here me; God spak in his hooli.
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
I schal make ful out ioye, and Y schal departe Siccimam; and Y schal mete the grete valei of tabernaclis.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Galaad is myn, and Manasses is myn; and Effraym is the vptaking of myn heed. Juda is my king; Moab is the caudron of myn hope.
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
In to Ydume Y schal stretche forth my scho; aliens ben maad frendis to me.
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Who schal lede me forth in to a stronge citee; who schal lede me forth til in to Idume?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Whether not thou, God, that hast put vs awei; and, God, schalt thou not go out in oure vertues?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Yyue thou help to vs of tribulacioun; for the heelthe of man is veyn.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
We schulen make vertu in God; and he schal bringe oure enemyes to nouyt.

< Masalimo 108 >