< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Alleluya. Lord, Y schal knouleche to thee in al myn herte; in the counsel and congregacioun of iust men.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
The werkis of the Lord ben greete; souyt out in to alle hise willis.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
His werk is knoulechyng and grete doyng; and his riytfulnesse dwellith in to the world of world.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
The Lord merciful in wille, and a merciful doere, hath maad a mynde of hise merueilis;
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
he hath youe meete to men dredynge hym. He schal be myndeful of his testament in to the world;
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
he schal telle to his puple the vertu of hise werkis.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
That he yyue to hem the eritage of folkis; the werkis of hise hondis ben treuthe and doom.
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
Alle hise comaundementis ben feithful, confermed in to the world of world; maad in treuthe and equite.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
The Lord sente redempcioun to hys puple; he comaundide his testament with outen ende. His name is hooli and dreedful;
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
the bigynnyng of wisdom is the drede of the Lord. Good vndirstondyng is to alle that doen it; his preising dwellith in to the world of world.

< Masalimo 111 >