< Miyambo 1 >

1 Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
The parablis of Salomon, the sone of Dauid, king of Israel;
2 Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
to kunne wisdom and kunnyng;
3 kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
to vndurstonde the wordis of prudence; and to take the lernyng of teching; to take riytfulnesse, and dom, and equyte;
4 Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
that felnesse be youun to litle children, and kunnyng, and vndurstonding to a yong wexynge man.
5 Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
A wise man heringe schal be wisere; and a man vndurstondinge schal holde gouernails.
6 kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
He schal perseyue a parable, and expownyng; the wordis of wise men, and the derk figuratif spechis of hem.
7 Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
The drede of the Lord is the bigynning of wisdom; foolis dispisen wisdom and teching.
8 Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
My sone, here thou the teching of thi fadir, and forsake thou not the lawe of thi modir;
9 Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
that grace be addid, ethir encreessid, to thin heed, and a bie to thi necke.
10 Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
Mi sone, if synneris flateren thee, assente thou not to hem.
11 Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
If thei seien, Come thou with vs, sette we aspies to blood, hide we snaris of disseitis ayens an innocent without cause;
12 tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
swolowe we him, as helle swolowith a man lyuynge; and al hool, as goynge doun in to a lake; we schulen fynde al preciouse catel, (Sheol h7585)
13 Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
we schulen fille oure housis with spuylis; sende thou lot with vs,
14 Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
o purs be of vs alle;
15 Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
my sone, go thou not with hem; forbede thi foot fro the pathis of hem.
16 Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
For the feet of hem rennen to yuel; and thei hasten to schede out blood.
17 Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
But a net is leid in veyn bifore the iyen of briddis, that han wengis.
18 Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
Also `thilke wickid disseyueris setten aspies ayens her owne blood; and maken redi fraudis ayens her soulis.
19 Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
So the pathis of ech auerouse man rauyschen the soulis of hem that welden.
20 Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
Wisdom prechith with outforth; in stretis it yyueth his vois.
21 ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
It crieth ofte in the heed of cumpenyes; in the leeues of yatis of the citee it bringith forth hise wordis,
22 “Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
and seith, Hou long, ye litle men in wit, louen yong childhod, and foolis schulen coueyte tho thingis, that ben harmful to hem silf, and vnprudent men schulen hate kunnyng?
23 Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
Be ye conuertid at my repreuyng; lo, Y schal profre forth to you my spirit, and Y schal schewe my wordis.
24 Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
For Y clepide, and ye forsoken; Y helde forth myn hond, and noon was that bihelde.
25 Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
Ye dispisiden al my councel; and chargiden not my blamyngis.
26 Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
And Y schal leiye in youre perisching; and Y schal scorne you, whanne that, that ye dreden, cometh to you.
27 Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
Whanne sodeyne wretchidnesse fallith in, and perisching bifallith as tempest; whanne tribulacioun and angwisch cometh on you.
28 “Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
Thanne thei schulen clepe me, and Y schal not here; thei schulen rise eerli, and thei schulen not fynde me.
29 Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
For thei hatiden teching, and thei token not the drede of the Lord,
30 popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
nether assentiden to my councel, and depraueden al myn amendyng.
31 Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
Therfor thei schulen ete the fruytis of her weie; and thei schulen be fillid with her counseils.
32 Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
The turnyng awei of litle men in wit schal sle hem; and the prosperite of foolis schal leese hem.
33 Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”
But he that herith me, schal reste with outen drede; and he schal vse abundaunce, whanne the drede of yuels is takun awei.

< Miyambo 1 >