< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Mi sone, if thou resseyuest my wordis, `and hidist myn heestis anentis thee;
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
that thin eere here wisdom, bowe thin herte to knowe prudence.
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
For if thou inwardli clepist wisdom, and bowist thin herte to prudence;
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
if thou sekist it as money, and diggist it out as tresours;
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
thanne thou schalt vndirstonde the drede of the Lord, and schalt fynde the kunnyng of God.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
For the Lord yyueth wisdom; and prudence and kunnyng is of his mouth.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
He schal kepe the heelthe of riytful men, and he schal defende hem that goen sympli.
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
And he schal kepe the pathis of riytfulnesse, and he schal kepe the weies of hooli men.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Thanne thou schalt vndirstonde riytfulnesse, and dom, and equytee, and ech good path.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
If wysdom entrith in to thin herte, and kunnyng plesith thi soule,
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
good councel schal kepe thee, and prudence schal kepe thee; that thou be delyuered fro an yuel weie,
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
and fro a man that spekith weiward thingis.
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
Whiche forsaken a riytful weie, and goen bi derk weies;
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
whiche ben glad, whanne thei han do yuel, and maken ful out ioye in worste thingis;
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
whose weies ben weywerd, and her goyingis ben of yuel fame.
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
That thou be delyuered fro an alien womman, and fro a straunge womman, that makith soft hir wordis;
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
and forsakith the duyk of hir tyme of mariage,
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
and hath foryete the couenaunt of hir God. For the hous of hir is bowid to deeth, and hir pathis to helle.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
Alle that entren to hir, schulen not turne ayen, nether schulen catche the pathis of lijf.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
That thou go in a good weie, and kepe the pathis of iust men.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Forsothe thei that ben riytful, schulen dwelle in the lond; and symple men schulen perfitli dwelle ther ynne.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
But vnfeithful men schulen be lost fro the loond; and thei that doen wickidli, schulen be takun awey fro it.

< Miyambo 2 >