< Masalimo 150 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika; mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.
Alleluya. Herie ye the Lord in hise seyntis; herie ye hym in the firmament of his vertu.
2 Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu; mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.
Herie ye hym in hise vertues; herie ye hym bi the multitude of his greetnesse.
3 Mutamandeni poyimba malipenga, mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.
Herie ye hym in the soun of trumpe; herie ye hym in a sautre and harpe.
4 Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina, mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.
Herie ye hym in a tympane and queer; herie ye hym in strengis and orgun.
5 Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga, mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.
Herie ye hym in cymbalis sownynge wel, herye ye hym in cymbalis of iubilacioun;
6 Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova. Tamandani Yehova.
ech spirit, herye the Lord.

< Masalimo 150 >