< Numeri 5 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises, and seide, Comaunde thou to the sones of Israel,
2 “Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
that thei caste out of the castels ech leprouse man, and that fletith out seed, and is defoulid on a deed bodi; caste ye out of the castels,
3 Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
as wel a male as a female, lest thei defoulen tho, whanne thei dwellen with you.
4 Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
And the sones of Israel diden so; and thei castiden hem out of the castels, as the Lord spak to Moises.
5 Yehova anati kwa Mose,
And the Lord spak to Moises,
6 “Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
and seide, Speke thou to the sones of Israel, Whanne a man ethir a womman han do of alle synnes that ben wont to falle to men, and han broke bi necgligence the `comaundement of the Lord,
7 ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
and han trespassid, thei schulen knowleche her synne, and thei schulen yelde thilke heed, and the fyuethe part aboue, to hym ayens whom thei synneden.
8 Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
But if noon is that schal resseyue thei schulen yyue to the Lord, and it schal be the preestis part, outakun the ram which is offrid for clensyng, that it be a quemeful sacrifice.
9 Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
Also alle the firste fruytis, whiche the sones of Israel offren, perteynen to the preest;
10 Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
and what euer thing is offrid of ech man in the seyntuarie, and is youun to the `hondis of the preest, it schal be the preestis part.
11 Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises,
12 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
and seide, Speke thou to the sones of Israel, and thou schalt seie to hem, If `the wijf of a man hath errid, and hath dispisid the hosebonde,
13 nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
and hath slept with another man, and the hosebonde may not take ether preue this, but the auowtrye is hid, and may not be preuyd bi witnessis, for sche is not foundun in leccherie;
14 mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
if the spirit of gelousie stirith the housebonde ayens his wijf, which is ether defoulid, ethir is apechid bi fals suspecioun,
15 apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
the man schal brynge hir to the preest, and he schal offre an offryng for hir `the tenthe part of a mesure clepid satum of barli meele; he schal not schede oyle ther onne, nethir he schal putte encense, for it is the sacrifice of gelousie, and an offryng enquerynge auowtrye.
16 “‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
Therfor the preest schal offre hir, and schal sette bifore the Lord;
17 Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
and he schal take holi watir in `a vessel of erthe, and he schal putte in to it a litil of the erthe of the pawment of the tabernacle.
18 Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
And whanne the womman stondith in the siyt of the Lord, he schal diskyuere hir heed, and he schal putte `on the hondis of hir the sacrifice of remembryng, and the offryng of gelousie. Sotheli he schal holde moost bittir watris, in whiche he gaderide togidere cursis with cursyng.
19 Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
And he schal conioure hir, and schal seie, If an alien man slepte not with thee, and if thou art not defoulid in the forsakyng the bed of the hosebonde, these bittereste watris schulen not anoye thee, in to whiche Y haue gaderid togidere cursis;
20 Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
ellis if thou bowidst awei fro thin hosebonde, and art defoulid, and hast leyn with another man,
21 pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
thou schalt be suget to these cursyngys; the Lord yyue thee in to cursyng, and in to ensaumple of alle men in his puple; `the Lord make thin hipe to wexe rotun, and thi wombe swelle, and be brokun;
22 Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
cursid watris entre in to thi wombe, and while the wombe swellith, thin hipe wexe rotun. And the womman schal answere, Amen! amen!
23 “‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
And the preest schal write thes cursis in a litil book, and he schal do awey tho cursis with bittereste watris, in to whiche he gaderide cursis,
24 Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
and he schal yyue to hir to drynke. And whanne sche hath drunke tho watris,
25 Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
the preest schal take of hir hond the sacrifice of gelousie, and he schal reise it bifor the Lord, and he schal putte on the auter;
26 Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
so oneli that he take bifore an handful of sacrifice `of that that is offrid, and brenne on the auter, and so yyue drynke to the womman the moost bittere watris.
27 Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
And whanne sche hath drunke tho watris, if sche is defoulid, and is gilti of auowtrie, for the hosebonde is dispisid, the watris of cursyng schulen passe thorouy hir, and while the wombe is bolnyd, the hipe schal wexe rotun, and the womman schal be in to cursyng and in to ensaumple to al the puple.
28 Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
That if sche is not pollutid, sche schal be harmeles, and schal brynge forth fre children.
29 “‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
This is the lawe of gelousie, if a womman bowith awei fro hir hosebonde, and is defoulid,
30 kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
and the hosebonde is stirid with the spirit of gelousye, and bryngith hir in to the `siyt of the Lord, and the preest doith to hir bi alle thingis that ben writun, the hosebonde schal be with out synne,
31 Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”
and sche schal resseyue hir wickidnesse.

< Numeri 5 >