< Numeri 4 >

1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
And the Lord spak to Moises and to Aaron,
2 “Werengani Akohati omwe ndi gawo limodzi la Alevi monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
and seide, Take thou the summe of the sones of Caath, fro the myddis of Leuytis,
3 Werengani amuna onse amene ali ndi zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu amene amabwera kudzagwira ntchito mu tenti ya msonkhano.
bi her housis and meynees, fro the threttithe yeer and aboue `til to the fiftithe yeer, of alle that entren, that thei stonde and mynystre in the tabernacle of boond of pees.
4 “Ntchito ya Akohati mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kusamalira zinthu zopatulika kwambiri.
This is the religioun of the sones of Caath; Aaron and his sones schulen entren in to the tabernacle of boond of pees, and in to the hooli of hooli thingis,
5 Pamene anthu akusamuka pa msasa, Aaroni ndi ana ake aamuna azilowa mu tenti ndi kuchotsa chinsalu chotchingira ndi kuphimba nacho bokosi la umboni.
whanne the tentis schulen be moued; and thei schulen do doun the veil that hangith bifore the yatis, and thei schulen wlappe in it the arke of witnessyng;
6 Ndipo azikuta bokosilo ndi zikopa za akatumbu ndi kuyala pamwamba pake nsalu ya mtundu wa thambo ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
and thei schulen hile eft with a veil of `skynnys of iacynt, and thei schulen stretche forth aboue a mentil al of iacynt, and thei schulen putte in barris `on the schuldris of the bereris.
7 “Pa tebulo pamene pamakhala buledi wa ansembe aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo, ndipo aziyikapo mbale, mabeseni, zipande ndi mitsuko yoperekera nsembe yachakumwa. Aziyikaponso buledi wokhala pamenepo nthawi zonse.
Also thei schulen wlappe the boord of proposicioun in a mentil of iacynt, and thei schulen putte therwith cenceris, and morteris of gold, litil cuppis, and grete cuppis to fletyng sacrifices `to be sched; looues schulen euere be in the boord.
8 Tsono pamwamba pa izi aziyalapo nsalu yofiira, ndi kuzikuta mʼzikopa za akatumbu ndi kuyika mitengo yonyamulira mʼmalo mwake.
And thei schulen strecche forth aboue a reed mentil, which thei schulen hile eft with an hilyng of `skynnes of iacynt, and thei schulen putte yn barris.
9 “Azitenga nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira choyikapo nyale, pamodzi ndi nyale zake, zopanira zake, zotengera zake ndi mitsuko yonse yosungiramo mafuta.
Thei schulen take also a mentil of iacynt with which thei schulen hile the candilstike, with hise lanternes, and tongis, and snytels, and alle the `vessels of oile that ben nedeful to the lanternes to be ordeyned;
10 Kenaka achikulunge pamodzi ndi zipangizo zake zonse mʼzikopa za akatumbu ndi kuchiyika pa chonyamulira chake.
and on alle thingis thei schulen putte an hilyng of `skynnys of iacynt, and thei schulen putte in barris.
11 “Pamwamba pa guwa la golide aziyalapo nsalu ya mtundu wa thambo ndi kukutira ndi zikopa za akatumbu ndi kuyika mʼmalo mwake mitengo yonyamulira.
Also and thei schulen wlappe the goldun auter in a clooth of iacynt; and thei schulen stretche forth aboue an hilyng of `skynnys of iacynt, and thei schulen putte in barris.
12 “Azitenga zipangizo zonse zogwiritsira ntchito ku malo wopatulika, azizikulunga mʼnsalu ya mtundu wa thambo, azizikuta ndi zikopa za akatumbu ndi kuziyika pa zonyamulira zake.
Thei schulen wlappe in a mentil of iacynt alle the vessels in whiche it is mynystrid in the seyntuarie, and thei schulen strecche forth aboue an hilyng of `skynnys of iacynt, and thei schulen putte yn barris.
13 “Azichotsa phulusa la pa guwa lansembe lamkuwa ndi kuyalapo nsalu yapepo pamwamba pake.
But also thei schulen clense the auter fro aische, and thei schulen wlappe it in a clooth of purpur.
14 Kenaka aziyikapo zipangizo zonse zogwiritsira ntchito potumikira pa guwa, kuphatikizapo miphika yowotchera nyama, mafoloko otengera nyama, zowolera phulusa ndi mbale zowazira magazi pa guwa lansembe ndipo pamwamba pake aziyalapo zikopa za akatumbu ndi kuziyika mʼzonyamulira zake.
And thei schulen putte with it alle vessels whiche thei vsen in the seruyce therof, that is, ressettis of firis, tongis, and fleischokis, hokis, and censeris, ether pannys of coolis; thei schulen hile alle the vessels of the auter togidere in a veil of `skynnes of iacynt, and thei schulen putte in barris.
15 “Aaroni ndi ana ake aamuna akamaliza kukutira ziwiya za ku malo wopatulika ndi zipangizo zopatulika zonse, ndipo akakonzeka kusamuka pamalopo, Akohati abwere kudzazinyamula koma asagwire zinthu zopatulikazo. Akatero adzafa. Izi ndizo zinthu zimene Akohati ayenera kunyamula mu tenti ya msonkhano.
And whanne Aaron and hise sones han wlappid the seyntuarie, and alle vessels therof, in the mouyng of tentis, thanne the sones of Caath schulen entre, that thei bere the thingis wlappid, and touche not the vessels of the seyntuarie, lest thei dien.
16 “Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe, aziyangʼanira mafuta a nyale, ndi lubani wa nsembe zofukiza, nsembe yaufa yoperekedwa nthawi zonse ndi mafuta odzozera. Aziyangʼaniranso chihema ndi zonse zili mʼmenemo, kuphatikizapo zida ndi ziwiya zonse zopatulika.”
Thes ben the birthuns of the sones of Caath, in the tabernacle of boond of pees, on whiche Eleazar, the sone of Aaron, preest, schal be; to whois cure `the oile perteyneth to ordeyne lanternes, and the encense which is maad bi craft, and the sacrifice which is offrid euere, and the oile of anoyntyng, and what euere thing perteyneth to the ournyng of the tabernacle, and of alle vessels that ben in the seyntuarie.
17 Yehova anawuzanso Mose ndi Aaroni kuti,
And the Lord spak to Moises and to Aaron, and seide,
18 “Onetsetsani kuti mabanja a fuko la Kohati asachotsedwe kwa Alevi.
Nyle ye leese the puple of Caath fro the myddis of Leuytis;
19 Koma muziwachitira izi kuti asafe, akhalebe ndi moyo pamene ayandikira zinthu za ku malo wopatulika kwambiri: Aaroni ndi ana ake aamuna azipita ku malo wopatulika ndi kumamupatsa munthu aliyense ntchito yake ndi zimene ayenera kunyamula.
but do ye this thing to hem, that thei lyue, and die not, if thei touchen the hooli of hooli thingis. Aaron and hise sones schulen entre, and thei schulen dispose the werkis of alle men, and thei schulen departe `what who owith to bere.
20 Koma Akohati asalowe kukaona zinthu zopatulika, ngakhale kanthawi pangʼono, chifukwa akatero adzafa.”
Othere men se not bi ony curiouste tho thingis that ben in the seyntuarie, bifore that tho ben wlappid; ellis thei schulen die.
21 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises,
22 “Werenganso Ageresoni monga mwa mabanja ndi mafuko awo.
and seide, Take thou the summe also of the sones of Gerson, bi her housis, and meynees, and kynredis; noumbre thou
23 Uwerenge amuna onse a zaka makumi atatu mpaka a zaka makumi asanu zakubadwa amene amabwera kudzatumikira ku tenti ya msonkhano.
fro thretti yeer and aboue `til to fifti yeer alle that entren and mynystren in the tabernacle of boond of pees.
24 “Ntchito ya mafuko a Ageresoni pamene akugwira ntchito ndi kunyamula katundu ndi iyi:
This is the office of the sones of Gersonytis, that thei bere the curteyns of the tabernacle, and the roof of the boond of pees, an other hilyng,
25 Azinyamula makatani a ku chihema, tenti ya msonkhano, zokutira zake ndi zokutira kunja za zikopa za akatumbu, makatani a pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
and a veil of iacynt aboue alle thingis, and the tente which hangith in the entryng of the tabernacle of the boond of pees;
26 makatani wotchingira bwalo lozungulira chihema ndi guwa, katani ya pa khomo, zingwe ndi zida zonse zimene zimagwiritsidwa ntchito mʼchihema. Ageresoni azichita zonse zofunika kuchitika ndi zinthu zimenezi.
and the curteyns of the greet street, and the veil in the entryng, `which veil is bifor the tabernacle.
27 Ntchito yawo yonse, kaya kunyamula kapena kugwira ntchito zina, achite Ageresoni motsogozedwa ndi Aaroni ndi ana ake aamuna. Uwagawire ntchito zonse zimene akuyenera kugwira.
Whanne Aaron comaundith and hise sones, the sones of Gerson schulen bere alle thingis that perteynen to the auter, the coordis, and vessels of seruyce; and alle schulen wite, to what charge thei owen to be boundun.
28 Iyi ndiye ntchito ya fuko la Ageresoni ku tenti ya msonkhano. Ntchito zawo zichitike motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.
This is the office of the meynee of Gersonytis, in the tabernacle of boond of pees; and thei schulen be vndur the hond of Ythamar, the sone of Aaron, preest.
29 “Werenga Amerari monga mwa mafuko awo ndi mabanja awo.
Also thou schalt noumbre the sones of Merary, bi the meynees and housis of her fadris,
30 Werenga amuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu zakubadwa amene akatumikire mu tenti ya msonkhano.
fro thretti yeer and aboue `til to fifti yeer, alle that entren to the office of her seruice, and to the ournyng of the boond of pees of witnessyng.
31 Ntchito yawo pamene azikatumikira mu tenti ya msonkhano ndi iyi: kunyamula matabwa a chihema, mitanda, mizati ndi matsinde,
These ben `the chargis of hem; thei schulen bere the tablis of the tabernacle, and the barris therof, the pilers and her foundementis; also the pilers of the greet street bi cumpas,
32 ndiponso mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema, zingwe ndi zipangizo zake zonse ndiponso zonse zokhudzana ndi ntchito yake. Uwuze munthu aliyense chomwe ayenera kuchita.
with her foundementis, and her stakis, and coordis; thei schulen take alle instrumentis and purtenaunce at noumbre, and so thei schulen bere.
33 Iyi ndiyo ntchito ya mafuko a Amerari pamene akugwira ntchito ku tenti ya msonkhano motsogozedwa ndi Itamara mwana wa wansembe Aaroni.”
This is the office of `the meynee of Meraritis, and the seruyce in the tabernacle of boond of pees; and thei schulen be vndur the hond of Ythamar, the sone of Aaron, preest.
34 Mose, Aaroni ndi atsogoleri a magulu a anthu anawerenga Akohati monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Therfor Moises and Aaron and the princes of the synagoge noumbriden the sones of Caath, bi the kynredis and housis of her fadris,
35 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
fro thretti yeer and aboue `til to the fiftithe yeer, alle that entren to the seruyce of the tabernacle of boond of pees;
36 atawawerenga mwa mafuko awo, anali 2,750.
and thei weren foundun two thousynde seuene hundrid and fifti.
37 Ichi chinali chiwerengero cha mafuko a Akohati onse omwe ankatumikira mu tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
This is the noumbre of the puple of Caath, which entrith in to the tabernacle of boond of pees; Moises and Aaron noumbriden these, bi the word of the Lord, bi the hond of Moises.
38 Ageresoni anawerengedwanso monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
And the sones of Gerson weren noumbrid, bi the kyneredis and housis of her fadris,
39 Amuna onse a zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzagwira ntchito ku tenti ya msonkhano,
fro thretti yeer and aboue `til to `the fiftithe yeer, alle that entren that thei mynystre in the tabernacle of boond of pees;
40 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 2,630.
and thei weren foundun two thousynde sixe hundrid and thretti.
41 Ichi chinali chiwerengero cha Ageresoni mwa mabanja awo amene ankatumikira ku tenti ya msonkhano. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga mwa lamulo la Yehova.
This is the puple of Gersonytis, which Moises and Aaron noumbriden, bi the `word of the Lord.
42 Amerari anawawerenga monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
And the sones of Merary weren noumbrid, bi the kynredis and housis of her fadris,
43 Amuna onse kuyambira zaka makumi atatu mpaka makumi asanu amene anabwera kudzatumikira ntchito mu tenti ya msonkhano,
fro threttithe yeer and aboue `til to `the fiftithe yere, alle that entren to fille the customs, ether seruices, of the tabernacle of boond of pees;
44 atawawerenga mwa mafuko ndi mabanja awo, anali 3,200.
`and thei weren foundun thre thousynde and two hundrid.
45 Ichi ndicho chinali chiwerengero cha mabanja a Amerari. Mose ndi Aaroni anawawerenga monga momwe Yehova anawalamulira kudzera mwa Mose.
This is the noumbre of the sones of Merari, whiche Moyses and Aaron noumbriden, bi `the comaundement of the Lord, bi the hoond of Moises.
46 Kotero Mose, Aaroni ndi atsogoleri a Israeli anawerenga Alevi onse monga mwa mafuko ndi mabanja awo.
Alle that weren noumbrid of Leuytis, and whiche Moyses and Aaron and the princes of Israel maden to be noumbrid, bi the kynredis and housis of her fadris,
47 Aamuna onse a zaka makumi atatu mpaka zaka makumi asanu omwe anabwera kudzagwira ntchito yonyamula zinthu ku tenti ya msonkhano
fro thretti yeer and aboue `til to `the fiftithe yeer, and entriden to the seruyce of the tabernacle, and to bere chargis,
48 analipo 8,580.
weren togidere eiyte thousynde fyue hundrid and foure scoor.
49 Aliyense anamupatsa ntchito ndi kumuwuza choti anyamule monga mwa lamulo la Yehova kudzera mwa Mose. Anawawerenga chomwechi potsata zimene Yehova analamula Mose.
By the `word of the Lord Moises noumbride hem, ech man bi his office and hise chargis, as the Lord comaundide to hym.

< Numeri 4 >