< Luka 4 >

1 Yesu, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anachoka ku mtsinje wa Yorodani ndipo anatsogozedwa ndi Mzimu Woyerayo kupita ku chipululu,
A IEJUJ, me dir en Nen jaraui, puredo jan Iordan, o Nen kotin kalualan i nan jap tan.
2 kumene anayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anayi. Sanadye kena kalikonse pa masiku amenewo, ndipo pa mapeto pake anamva njala.
O wia jonejon pan tewil ran panaul. A jota kotin konot ni ran oko. Ran akan lao imwi jokela ap men konot.
3 Mdierekezi anati kwa Iye, “Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza mwala uwu kuti usanduke buledi.”
Tewil ap indai on i: Ma komui japwilim en Kot, en majani on takai wet, a en wiala prot.
4 Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha.’”
A Iejuj kotin japen i majani: A intinidier: Kaidin prot eta, me aramaj en memaureki, pwe majan en Kot akan.
5 Mdierekezi anamutengera Iye pamalo aatali ndipo mʼkamphindi namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi.
Tewil ap kaluadalan i pon nana ileile eu o kajala on i wein jappa karoj ni marep taieu.
6 Ndipo anati kwa Iye, “Ndidzakupatsani ulamuliro ndi ulemerero wawo; pakuti anandipatsa ine, ndipo ndingathe kupereka kwa aliyense amene ndikufuna.
Tewil indan i: I pan ki on komui manaman pukat karoj o a linan, pwe a muei on ia er, a i pan ki on, me i mauki.
7 Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”
Ari, ma komui pan poni ia, karoj ap pan japwilim omui la.
8 Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’”
Iejuj kotin japen i majani: A intinidier: Koe en poni on Kaun om Kot; i eta, koe en papa.
9 Mdierekezi anapita naye ku Yerusalemu namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu dziponyeni nokha pansi kuchokera pano.
I ap kalualan i Ierujalem o kauada i pon konkon en im en kaudok o indai on i: Ma komui japwilim en Kot, kajedi pein komui,
10 Pakuti kwalembedwa, “Adzalamulira angelo ake za iwe kuti akutchinjirize mosamala;
Pwe a intinidier: A pan kajilaki japwilim a tounlan kai komui, pwen apapwali komui.
11 ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.”
O wa komui nan lim ar akan, pwe aluwilu omui der dipikelekel ni takai eu.
12 Yesu anayankha kuti, “Mawu akuti, ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’”
Iejuj kotin japen majani on i: A lolokido, koe ender kajone jon Kaun om Kot!
13 Mdierekezi atamaliza mayesero awa onse, anamusiya Iye kufikira atapeza mpata wina.
Tewil lao kanikiela jonejon karoj, ap muei jan i anjau kij.
14 Yesu anabwerera ku Galileya mu mphamvu ya Mzimu Woyera, ndipo mbiri yake inafalikira ku madera onse a ku midzi.
Iejuj ap kotin pure don Kalilaa ni rojon en Nen, ap indand jili nan jap karoj me mi imp a.
15 Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.
A kotin kaukawewe nan ar jinakoke kan, o karoj kapina i.
16 Iye anapita ku Nazareti, kumene anakulira, ndipo pa tsiku la Sabata anakalowa mʼsunagoge, monga mwa chikhalidwe chake. Ndipo anayimirira kuti awerenge malemba.
A kotin lel Najaret, waja a kotin kakairida ia, ap kotilon jon nan jinakoke duen a kin wiada ni ran en japat o kotida, pwen wadok.
17 Anamupatsa buku la mneneri Yesaya. Atalitsekula, anapeza pamalo pamene panalembedwa kuti,
Puk en jaukop Iejaia an wijike don i a lao lim pajan puk o ap diarada waja o me intinidier:
18 “Mzimu wa Ambuye ali pa Ine; chifukwa wandidzoza kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kwa osauka. Wandituma kuti ndilalikire kwa a mʼndende kuti amasulidwe ndi kwa osaona kuti apenyenso, kumasulidwa kwa osautsidwa,
Nen en Kaun kotikot re i, I me a keie kin ia da, pwen padaki on me jamama kan ronamau. A kadar ia do, pwen kaloki on me jalidi kan, me ren jaladokela, o me majkun akan pan kilan waja, o me patau kan pan maioda,
19 ndi kulalikira za nthawi imene Ambuye adzakomere mtima anthu awo.”
O kaloki jaunpar mau en Kaun o.
20 Kenaka Iye anatseka bukulo, nalibwezera kwa wotumikira ndipo anakakhala pansi. Maso a aliyense mʼsunagogemo anali pa Iye,
A kotin lim pena puk o ap kupure on me papa men o kotidi. Maj en karoj nan jinakoke kankakil i.
21 ndipo anawawuza kuti, “Lero malemba awa akwaniritsidwa mmene mwamveramu.”
I ari tapiada majani on irail: Kijin likau wet pwaidar mo’mail ran wet.
22 Onse anayankhula zabwino za Iye ndipo anadabwa ndi mawu ogwira moyo amene anatuluka mʼkamwa mwake. Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu si mwana wa Yosefe?”
Ir karoj ap kadede o puriamuiki majan kompok kan, me pwili jan jilan i, ap indada: Kaidin i nain Iojep?
23 Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, mudzandiwuza mwambi uwu: Singʼanga, dzichiritse wekha! Chitanso mʼmudzi wa kwanu kuno zimene ife tamva kuti Iwe unazichita ku Kaperenawo.”
A ap kotin majani on irail: Nan melel, komail pan indan ia karajeraj wet: Jaunwini, jauaja pein uk! Pwe re ronadar duen ion kapuriamui, me wiauier nan Kapernaum; ari kom pil wiada iliieta waja et nan jap omui.
24 Iye anapitiriza kuti, “Zoonadi, ndikukuwuzani kuti palibe mneneri amene amavomerezedwa ku mudzi kwawo.
A kotin majani: Melel I indai on komail, jota jaukop amen me konekon nan japwe.
25 Ine ndikukutsimikizirani kunali amayi ambiri amasiye mu Israeli mʼnthawi ya Eliya, kumwamba kutatsekedwa kwa zaka zitatu ndi theka ndipo kunali njala yayikulu mʼdziko lonselo.
A melel I indai on komail, li odi toto mi nan Ijrael ni muein Kliaj, ni anjau nanlan matata par jilu o jaunipon wonu, ni lek In pal ap kipadi jap karoj;
26 Komabe Eliya sanatumidwe kwa mmodzi mwa iwo, koma kwa mkazi wamasiye wa ku Zerefati ku chigawo cha Sidoni.
A jota amen, me Eliaj pakadar won, pwe ren li odi men nan Jarepta nan jap Jidon.
27 Ndipo kunali akhate ambiri ku Israeli mʼnthawi ya mneneri Elisa, koma panalibe mmodzi mwa iwo anachiritsidwa kupatula Naamani wa ku Siriya.”
O me tuketuk kan me toto nan Ijrael ni muein jaukop Kliaj, a jota amen re’rail, me kelailadar, pwe Naeman eta men Jirien.
28 Anthu onse mʼsunagogemo anapsa mtima atamva izi.
Karoj, me mi nan jinakoke ni ar ronadar mepukat, ap makar kida kaualap,
29 Anayimirira namutulutsira kunja kwa mzindawo, ndipo anamutengera pamwamba pa phiri pamene mzindawo unamangidwapo, ndi cholinga chakuti amuponyere ku phompho.
Re udar jikonlar i jan kanimo, o kalualan i pon kailan dol o, waja ar kanim kakaudar ia, pwen kajedi jan ia,
30 Koma Iye anangoyenda pakati pa gulu la anthulo nachokapo.
A i kotin weid nan pun ar, kotila jan irail.
31 Kenaka Iye anapita ku Kaperenawo, mudzi wa ku Galileya, ndipo pa Sabata anayamba kuphunzitsa anthu.
I ari kotilan Kapernaum kanim en Kalilaa, o kotin kawewe on irail ni ran en japat akan.
32 Iwo anadabwa ndi chiphunzitso chake chifukwa uthenga wake unali ndi ulamuliro.
Irail ari puriamuiki a padak, pwe a majan me manaman.
33 Mʼsunagogemo munali munthu wogwidwa ndi mzimu woyipa. Iye analira ndi mawu akulu, akuti
A aramaj amen mi nan jinakoke, me nen en tewil jaut amen ti po a, me weriwer laud,
34 “Aa! Kodi mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
Inda: Ko jan kit, menda re omui kit Iejuj en Najaret! Kom kotido, en kawe kit ala. I aja, me komui nain Kot jaraui.
35 Yesu anachidzudzula kwambiri nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye.” Chiwandacho chinamugwetsa munthuyo pansi pamaso pa onse ndipo chinatuluka wosamupweteka.
Iejuj ap kidaue i majani: Nenenla o ko jan re a. Tewil lao kajedi i nan pun arail, ap koiei jan re a, jota me jued kot a wiai on i.
36 Anthu onse anadabwa ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi chiphunzitso ichi ndi chotani? Ndi ulamuliro ndi mphamvu Iye akulamulira mizimu yoyipa ndipo ikutuluka!”
Irail karoj ap puriamui kila, kajokajoi nan pun arail indada: Dakot majan pot et? Pwe a majan manaman o rojon on nen jaut akan, irail ap kin ko wei jan.
37 Ndipo mbiri yake inafalikira madera onse ozungulira.
I ari indand jili nin jap karoj waja o.
38 Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize.
I ap kotida jan nan jinakoke, ap kotilon on nan im en Jimon. A jaulap en Jimon me jomau karakar. Irail ari poekipoeki i re a.
39 Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.
I ari koti don i majani on jomau o, ap madan ko jan, i ari madan paurida papa irail.
40 Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa.
Katipin lao kirilar, rap wa don i ar luet akan karoj. I ari kotikidan amen amen lim a kan, kakelail ir ada.
41 Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.
O tewil akan pil kowei jan ren me toto, me weriwer indada: Komui japwilim en Kot. I ari kotin kidau ir ada, o jota mueid on irail, en lokaia, pwe re aja, me i Krijtuj.
42 Kutacha, Yesu anapita ku malo a yekha. Anthu ankamufunafuna Iye ndipo pamene anafika kumene anali, anthuwo anayesetsa kumuletsa kuti asawachokere.
A lao waja ran a kotilan waja rir, a pokon o raparapaki i, re pokon don i o kolekol i pwen der koti wei jan irail.
43 Koma Iye anati, “Ine ndikuyenera kulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ku mizinda inanso chifukwa ichi ndi chimene ananditumira.”
A i kotin majani on ir: I pil pan padaki ronamau en wein Kot nan kanim tei ko, pwe i me I pakadar kidor.
44 Ndipo Iye anapitirirabe kulalikira mʼmasunagoge a ku Yudeya.
A i kotin padapadak nan jinakoke en Kalilaa kan.

< Luka 4 >