< Marko 1 >

1 Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu,
TAPIN ronamau en Iej uj Krijluj, Japwilim en Kot.
2 monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya: “Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu,”
Duen a intinidi ren jaukop Iejaia Kilan, i kadarala moui men kadar me pan kaonopada al omui!
3 “Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
Nil eu likelikwir jili nan jap tan: Komail kaonopada al en Kaun o kaineneda al a!
4 Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo.
Ioanej kotido wia paptaij nin jap tan o padapadak duen paptaij en kalula on lapwa dip akan.
5 Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani.
Toun jap en Juj akan o toun Ierujalem karoj pokon don re a; irail paptaijela re a nan pilap Iordan, weokada dip arail akan.
6 Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo.
Ioanej kin likauwi wun en kamel, o perapirki kil en man, o kin kankan manjiek o oni en nan wel.
7 Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake.
O padapadak majani: Meamen laud jan ia kotido mur i. Jal en a jut i jota war on idiokidi lapwada.
8 Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”
I paptaij kilar komail pil. A a pan paptaij kin komail Nen jaraui!
9 Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
Kadekadeo ni ran oko Iejuj ap kotido jan Najaret en Kalilaa ap paptaijela ren Ioanej nan Iordan.
10 Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda.
A madan kotida jan nan pil o, ap kotin majani nanlan kan ar ritida, o Nen mom en muroi piridi don poa.
11 Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”
Nil eu ap peidido jan nanlan kan: Nai kompok komui, me I perenki!
12 Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu,
A madan Nen kalua won jap tan.
13 ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.
A ap kotikoteki jap tan ran panaul wia jonejon pan Jatan, ieian man laualo; a tounlan kan me papa on i.
14 Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati,
Murin en Ioanej a panalar, Iejuj ap koti don Kalilaa, padapadak ronamau en wein Kot.
15 “Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”
Majani: Anjau o leler wein Kot mier! Komail kalula! Kamelele ronamau!
16 Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi.
Ni a kotikot jili liman jed en Kalilaa, a ap majani Jimon o ri a ol Andreaj ara lalaid jili, pwe ira jaujed.
17 Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
Iejuj ap kotin majani on ira: Koma idauen ia do! Pwe I pan wia kin koma la jaujed en aramaj!
18 Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.
Ira ari madan kajedi ara uk eko, ap idauenla i.
19 Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo.
Ari, ni a kotila jan waja o, a ap kotin majani Iakopuj, nain Jepedauj o ri a ol Ioanej mimi pon jop pot wonewone ara uk oko.
20 Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.
I ari kotin molipe ira madan, ira ari pededi jam ara Jepedauj nin jop o ren toun dodok ko o idauen la i.
21 Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa.
Irail ap koti don Kapernaum. A madan kotilon on nan jinakoke ni ran en japat o kawewe.
22 Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo.
Re ap puriamuiki a padak, pwe a kotin kawewe on irail ni manaman jota dueta jaunkawewe kan.
23 Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti,
Aramaj amen ian mi nan jinakoke o, me nen jaut mi lole, ap weriwer,
24 “Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
Indada: Ko jan kit! Menda re omui kit, Iejuj en Najaret? Komui kotido en kawe kit ala? I aja komui, Jaraui en Kot.
25 Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!”
Iejuj ari ononida, majani: Nenenla o kowei jan i!
26 Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.
Nen jaut lao kapururada ap weriwer laudeda, a ap koiei jan i.
27 Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.”
Irail karoj puriamui, pepeidok nan pun arail indada: Dakot met? Padak kap, dakot met? Pwe ni manaman a majani on nen jaut akan, irail ari peiki on i.
28 Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.
I ari madan indand jili nin jap karoj impan Kalilaa.
29 Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya.
Irail ari madan koti jan nan jinakoke, ap ian Iakopuj o Ioanej kotilon on nan im en Jimon o Andreaj,
30 Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye.
Jaulap en Jimon wononeki jomau karakar. Irail ap kaireki i madan duen i.
31 Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.
I ari koti won ale pa a, kauada. Jomau karakar ap madan ko jan; i ari papa irail.
32 Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda.
A lao jautik penaer, ni katipin kirila, re ap wa pena on I karoj me jomau o me tewil ti po arail.
33 Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo,
O toun kanim o pokon don ni im o.
34 Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.
A ap kotin kakelailada me toto me jomauki jon en jomau toto, kauja jan tewil toto, ap kulikedi tewil akan, ren der lokaia, pwe re aja i.
35 Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera.
A kotin kipada nin joran, kotilan jap tan, pwen laolao wuja o.
36 Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye,
Jimon o me ian ko ap idauen i.
37 ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”
Ni arail diar i, re ap potoan on i: Irail karoj raparapa kin komui.
38 Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.”
A ap kotin majani on irail: Kitail daulul won jap tei ko, pwe I en pil padak waja o, pwe i me I kokido.
39 Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.
A ap kotin padapadak jili nan arail jinakoke kan nan jap en Kalilaa karoj o kakauj tewil akan,
40 Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
Ol tuketuk amen ap poto don i kolepuki poeki potoan on i: Ma re kotin kupura, re kotin I kamwakeke ia da!
41 Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!”
Iejuj ari kupuro kila, kapawei lim a jair i majani on i: I pan, mwakekelada!
42 Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.
A ni a majani eta, ari a tuketuk ko jan madan, a ap makelekel lar.
43 Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti,
I ari kalikedi i, ap madan kadarala.
44 “Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.”
Majani on i: Kalaka! Koe depa indai on meamen; a kowei kajale on koe jamero o, o kida, pweki om makelekelada, me Mojej majani, pwen kadede on irail.
45 Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.
Ari, a kolata kaloki jili, juaiki jili o ari, kareda en Iejuj a jola janjal koti don kanim o, kotikot eta liki nan jap tan, irail ap pokon don re a jan pali karoj.

< Marko 1 >