< Luka 22 >

1 Phwando la buledi wopanda yisiti lotchedwa Paska litayandikira,
A KAMADIP en prot jomut korendor, me adaneki paja.
2 akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo amafunafuna mpata woti amuphere Yesu, pakuti ankachita mantha ndi anthu.
Jamero lapalap o jaunkawewe kan raparapaki, pwen kamatala i, pwe irail majak aramaj akan.
3 Kenaka Satana analowa mwa Yudasi, wotchedwa Isikarioti, mmodzi wa khumi ndi a iwiriwo.
A Jatan tilon on Iudaj me adaneki Ijkariot, me kijan ekriamen ko.
4 Ndipo Yudasi anapita kwa akulu a ansembe ndi akulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi kukambirana nawo za mmene iye angaperekere Yesu.
I ari koieila ren jamero lapalap o jaumaj akan, kalelapok duen a pan panalan ir i.
5 Iwo anakondwa ndipo anagwirizana zomupatsa ndalama.
Irail ari peren kida, wiaki eu en ki on i moni.
6 Iye anavomera, ndipo anayamba kufunafuna mpata wabwino wakuti amupereke Yesu kwa iwo pamene panalibe gulu la anthu pafupi.
I ari inauki on irail, o raparapaki, duen a pan panalan ir i jo moromoron.
7 Kenaka linafika tsiku la buledi wopanda yisiti pamene mwana wankhosa wa Paska amaperekedwa nsembe.
Ran en prot jomut ap leler, anjaun kamela paja.
8 Yesu anatuma Petro ndi Yohane nati, “Pitani kukatikonzera Paska kuti tikadye.”
I ari poronela Petruj o loanej majani: U kowei, kaonopadan kitail paja, pwe kitail en mana.
9 Iwo anafunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonzere kuti?”
Irail idok re a: la waja, re kotin kupura, jen kaonopada?
10 Iye anayankha kuti, “Taonani, mukamalowa mu mzinda, mudzakumana ndi mwamuna atanyamula mtsuko wamadzi. Mulondoleni ku nyumba imene akalowe,
A kotin majani on irail: Kilan, koma lao pedelon kanim o, aramaj amen pan tu on koma, me wa pakit en pil eu, idauen i nan im o, me a pedelon on lole!
11 ndipo mukamuwuze mwini nyumbayo kuti, ‘Aphunzitsi kufunsa kuti, chili kuti chipinda cha alendo, kumene Ine ndi ophunzira anga tikadyere Paska?’
Koma ap indan kaun pan im o: Jaunpadak o majanie don komui: Ia pera en kairu, waja I pan mana paja ia ianaki ai tounpadak kan?
12 Iyeyo adzakuonetsani chipinda chachikulu chapamwamba, chokhala ndi zonse. Kachiteni zokonzekera mʼmenemo.”
I ari pan kajale on koma weip poa eu, me audeki men momod, i waja koma pan kaonopada!
13 Iwo anapita nakapeza zinthu monga mmene Yesu anawawuzira. Tsono anakonza Paska.
Ira lao koieila, ap diarada, duen a kotin majani on ira; ira ap kaonopada paja.
14 Ora litakwana, Yesu ndi ophunzira ake anakhala pa tebulo.
Auer lao leler, i ap kaipokedi ni tepel o wanporon ekriamen ian i.
15 Ndipo Iye anawawuza kuti, “Ine ndakhala ndikuyembekezera kudya Paska uyu ndi inu ndisanamve zowawa.
I ap kotin majani on irail. I anane melel ian komail mana paja wet mon ai pan kalokolok.
16 Pakuti Ine ndikukuwuzani kuti sindidzadyanso Paska wina mpaka Paskayi itakwaniritsidwa mu ufumu wa Mulungu.”
Pwe I indai on komail, I jolar pan kan jan met kokolata, a lao kapunala nan wein Kot.
17 Atanyamula chikho, Iye anayamika ndipo anati, “Tengani ndipo patsiranani pakati panu.
I ari kotikida dal o laolaoki a majani: Ale met, nek nan pun omail!
18 Pakuti ndikukuwuzani kuti, Ine sindidzamwanso zochokera ku chipatso cha mphesa mpaka ufumu wa Mulungu utabwera.”
Pwe I indai on komail, I jolar pan nim jan kijan wan wain, wein Kot lao pwaidar.
19 Ndipo Iye anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema, nagawira iwo nati, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.”
A kotin limada prot, laolaoki o pilitiki pena, ap kotiki on irail majani: War ai metet, me panalan komail! Komail en wia me wet, men kataman kin ia.
20 Chimodzimodzinso, utatha mgonero, anatenga chikho nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga, amene akhetsedwa chifukwa cha inu.
O pil dal en nim murin kajipon majani: Dal wet kadede kap ni mom en nt’ ai, me kapwilepilidi on komail.
21 Koma dzanja la amene akundipereka Ine lili pamodzi ndi langa pa chakudya pano.
A kilan, pa en me pan pan ia la, me ian ia ni tepel o.
22 Mwana wa Munthu apita monga mmene zinalembedwera, koma tsoka kwa munthu amene amupereka Iye.”
Nan melel, Nain aramaj pan kokola duen a kileledier, a juedi on aramaj o, me a pan pankila!
23 Iwo anayamba kufunsana pakati pawo kuti ndi ndani wa iwo amene akanachita ichi.
Irail ari pikikidi idok nan pun arail, ij re irail, me pan wiada met?
24 Komanso mkangano unabuka pakati pawo kuti ndani mwa iwo amene amaganiziridwa kukhala wamkulu.
Irail pil akamaiki nan pun arail, duen ij me pan lapalap re irail.
25 Yesu anawawuza kuti, “Mafumu a anthu a mitundu ina amaonetsa mphamvu za ufumu wawo pa anthuwo; ndipo amene ali ndi ulamuliro, amapatsidwa dzina la kuti ‘Opindula.’
A kotin majani on irail: Nanmarki en wei pokon akan kin poe irail edi o me manaman akan kin adaneki monjap kalanan.
26 Koma inu simuyenera kukhala choncho. Mʼmalo mwake, wamkulu pakati panu akhale ngati wamngʼono pa onse, ndipo iye amene alamulira akhale ngati wotumikira.
A komail jota pan dueta, a me lapalap re omail, i en dueta me tikitik, o me kin kaunda, en dueta me kin papa.
27 Pakuti wamkulu ndani, iye amene ali pa tebulo kapena iye amene akutumikira? Kodi si iye amene ali pa tebulo? Koma ndili pakati panu ngati mmodzi wokutumikirani.
Pwe ij me lapalap ren me mondi ni tepel de me kin papa? Kaidin i, me mondi ni tepel? A nai dueta ladu pamail.
28 Inu ndinu amene mwayima nane mʼmayesero.
Nan komail me ian ia ni ai jonejon.
29 Ndipo Ine ndikupatsani inu ufumu, monga momwe Atate anga anandipatsiranso Ine,
Nai ari kileledi on komail wei eu, duen Jam ai kileledi on ia er;
30 kuti inu muthe kudya ndi kumwa pa tebulo langa mu ufumu wanga ndi kukhala pa mipando yaufumu kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israeli.”
Pwe komail en mana o nim ni ai tepel nan ai wei o mondi pon men mondi ko, kakaun kainok en Ijrael eijokriau.
31 “Simoni, Simoni, Satana wapempha kuti akupete ngati tirigu.
Kaun ap kotin majani: Jimon, Jimon, kilan, Jatan non kin komail, pwen koko komail dueta wan prot.
32 Koma Ine ndakupempherera Simoni, kuti chikhulupiriro chako chisafowoke ndipo pamene udzabwerera kwa Ine, udzalimbikitse abale ako.”
A nai me kapakapa kin uk, pwe om pojon de nikila. A koe lao japaledo kakelada ri om ol akan!
33 Koma iye anayankha kuti, “Ambuye, ndine wokonzeka kupita nanu ku ndende ndi kufa komwe.”
A a potoan on i: Main, i pan idauen ir lel nan imaten o matala.
34 Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuza Petro, tambala asanalire lero lino, udzandikana katatu kuti sukundidziwa Ine.”
A kotin majani: Petruj, I indai on uk, nan malek jota pan kakorot ran wet, koe lao kamamki pan jilepak, me koe aja ia.
35 Kenaka Yesu anawafunsa iwo kuti, “Ine nditakutumizani wopanda chikwama cha ndalama, thumba kapena nsapato, kodi inu munasowa kanthu?” Iwo anayankha kuti, “Palibe chimene tinasowa.”
A kotin majani on irail: Ni ai kadar komail wei jo ed en moni, o jo ed en jailok, o jo jut, meakot komail lekekilar? Re ap potoan on: Jota.
36 Iye anawawuza kuti, “Koma tsopano ngati muli ndi chikwama cha ndalama, chitengeni, ndiponso thumba. Ndipo ngati mulibe lupanga, gulitsani mkanjo wanu ndi kugula.
I ari kotin majani on irail: A met, me a ed en moni mia, en ale o pil ed en jailok, o me jo a, i en netekila a likau, ap id netiada kodlaj pot.
37 Zalembedwa kuti, ‘Ndipo Iye anawerengedwa pamodzi ndi anthu ochimwa,’ ndipo Ine ndikuwuzani kuti izi ziyenera kukwaniritsidwa mwa Ine. Inde, zimene zinalembedwa za Ine, zikukwaniritsidwa.”
Pwe I indai on komail, me intinidier, pil pan pwai on ia: A wadawad on me dipan akan, pwe me intinidier duen nai, pan kaimwijokala.
38 Ophunzira anati, “Taonani Ambuye, awa malupanga awiri.” Iye anayankha kuti, “Amenewa akwanira.”
Irail indada: Main, kotin majani, iet kodlaj riapot. A kotin majani on irail. Ari, i eta.
39 Yesu anapitanso monga mwa masiku onse ku Phiri la Olivi, ndipo ophunzira ake anamutsatira Iye.
I ari kotilan dol Oliwe, duen a kin wia; tounpadak kan idauenla i.
40 Atafika pamalopo, Iye anawawuza kuti, “Pempherani kuti musagwe mʼmayesero.”
I lao lei on waja o, ap kotin majani on irail: Komail kapakap pwe komail de ko on nan jonejon.
41 Iye anapita patsogolo pangʼono patali ngati kuponya mwala, anagwada napephera kuti,
I ari tororela jan irail doo weita kapir won takai eu, ap kelepuki laolao.
42 “Atate ngati mukufuna chotsereni chikho ichi. Komatu muchite zimene mukufuna osati zimene ndikufuna ine.”
Majani: Jam (ai), ma komui mauki, koti ki wei jan ia dal wet, ari jo, kaidin injen ai, pwe kupur omui ta en wiaui.
43 Mngelo wochokera kumwamba anafika namulimbikitsa.
Nan tounlan amen pwarado jan nanlan katinada i.
44 Ndipo mopsinjika mtima, anapemphera moona mtima, ndipo thukuta lake linali ngati madontho a magazi akugwera pansi.
A ni a kotin pador on mela, ap nianian a laolao, lao pudo a likamata nta, me dinedinedi on nan pwel.
45 Iye atamaliza kupemphera, ndi kubwerera kwa ophunzira ake, anawapeza atagona atafowoka ndi chisoni.
A kotida jan a laolao o kotin pur on tounpadak kan, ir mamair aki ar mamauk.
46 Iye anafunsa kuti, Nʼchifukwa chiyani mukugona? “Dzukani ndipo pempherani kuti inu musagwe mʼmayesero.”
Majani on irail: Da me komail mamairki? Paurida o kapakap, pwe komail de ko on nan jonejon!
47 Pamene Iye ankayankhulabe, gulu la anthu linabwera, ndipo munthu wotchedwa Yudasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo analitsogolera. Iye anamuyandikira Yesu kuti amupsompsone.
A ni a kotin majani mepukat, kilan, pokon o, o me adaneki ludaj, amen ir ekriamen, tion mo’rail, kaikai don Iejuj, pwen metik i.
48 Koma Yesu anamufunsa kuti, “Yudasi, kodi ukupereka Mwana wa Munthu ndi mpsopsono?”
A Iejuj kotin majani on i: ludaj, koe pan pan kila metik eu Nain arama?
49 Otsatira Yesu ataona zimene zimati zichitike, anati, “Ambuye, kodi timenyane ndi malupanga athu?”
Irail me ian i lao kilaner me pan wiaui, rap indai on i: Main, je jo pan wokieki ir kodlaj?
50 Ndipo mmodzi wa iwo anatema wantchito wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake lamanja.
Amen ir pala ladun jamero lapalap amen o jara jan jalon a pali maun.
51 Koma Yesu anayankha kuti, “Zisachitikenso zimenezi!” Ndipo Iye anakhudza khutu la munthuyo ndi kumuchiritsa.
Iejuj ap kotin japen majani: Arier! I ap kotin jair jalon a, kakelada i.
52 Kenaka Yesu anafunsa akulu a ansembe, akuluakulu oyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndi akuluakulu ena amene anabwerawo kuti, “Kodi Ine ndikutsogolera gulu lowukira kuti mubwere ndi malupanga ndi zibonga?
Iejuj ap kotin majani on jamero lapalap akan, o kaun pan im en kaudok, o jaumaj akan, me ko don i: Dueta lolap amen, me komail koko don, wa kodlaj o katiu kai?
53 Tsiku lililonse ndinali nanu mʼmabwalo a mʼNyumba ya Mulungu ndipo inu simunandigwire. Koma iyi ndi nthawi yanu pamene mdima ukulamulira.”
Ni ran karoj nai ian komail nan im en kaudok, a komail jota man jair ia, pwe anjau wet omail anjau o manaman en rotorot.
54 Pamenepo anamugwira Iye, napita naye ndipo anamutengera ku nyumba ya mkulu wa ansembe. Petro anamutsatira patali.
Re ap jaikidi i o kalualon on nan im en jamero lapalap o, a Petruj idauenla doowei jan.
55 Koma pamene anasonkha moto pakati pa bwalo la milandu, anakhala onse pansi ndipo Petro anakhalanso pansi.
Irail ap jaunda kijiniai eu nan waron en kel o mod pena, a Petruj mondi nan pun arail.
56 Mtsikana wantchito anamuona atakhala nawo pafupi ndi moto. Iye anamuyangʼanitsitsa ndipo anati, “Munthu uyu anali ndi Yesu.”
A lidu men kilan i a momod impan kijiniai o kankakil i indada:
57 Koma Petro anakana nati, “Mtsikana, ine sindimudziwa ameneyu.”
let et pil ian i. I ari kamam kin i indada: Li, i jaja i.
58 Patatha kanthawi pangʼono, wina wake anamuona ndipo anati, “Iwenso ndiwe mmodzi mwa iwo.” Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, ayi sindine.”
A mur kij amen kilan i indada: Koe pil amen irail. A Petruj indada: O kaidin nai!
59 Patatha pafupifupi ora limodzi, munthu winanso anati, “Zoonadi, munthu uyu anali ndi Iye, pakuti ndi mu Galileya.”
Kadekadeo murin auer eu amen katitiki indada: Melel i men et ian i, pwe i kijan men Kaliaa.
60 Petro anayankha kuti, “Munthu iwe, sindikudziwa zimene ukunena apa.” Pamene iye ankayankhula, tambala analira.
A Petruj indada: O i poneponeki om kajokajoi! A pitipit ni a lokelokaia malek ap kakoroteda.
61 Ambuye anachewuka namuyangʼanitsitsa Petro. Pamenepo Petro anakumbukira mawu amene Ambuye anayankhula kwa iye kuti, “Asanalire tambala lero lino, udzandikana Ine katatu.”
Kaun ap kotin jaupeido majani Petruj. Petruj ap tamanda majan en Kaun, duen a kotin majani on i: Mon malek kakorot, koe pan kamam kin ia pan jilepak.
62 Ndipo iye anapita panja nakalira kwambiri.
Petruj ari koieila janejan kaualap.
63 Anthu amene ankalonda Yesu anayamba kumuchita chipongwe ndi kumumenya.
A ol oko, me kolekol i, lalaue o woki i.
64 Anamumanga mʼmaso ndi kumufunsa kuti, “Tanenera! Wakumenya iwe ndi ndani?”
Irail lao perala jilan i, ap idedok re a indada: Kopada, ij i, me pikir uk ada?
65 Ndipo iwo anamunena zachipongwe zambiri.
O jon en lalaue toto, me re ki on i.
66 Kutacha, bungwe la akuluakulu, pamodzi ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anakumana pamodzi, ndipo anamuyika Yesu patsogolo pawo.
A lao ran pajan jaumaj akan o jamero lapalap o jaunkawewe kan ap pokon pena o kalua i don nan arail kapun.
67 Iwo anati, “Tiwuze, ngati ndiwe Khristu.” Yesu anayankha kuti, “Ine nditakuwuzani simungandikhulupirire.
Indada: Ma koe Krijtuj, ap katiti on kit! A kotin majani on irail: Ma I pan indai on komail, komail jota pan kamelele;
68 Ine nditakufunsani inu, simungandiyankhe.
A ma I pan idok, komail jota pan japen, o pil jota lapwa ia da.
69 Koma kuyambira tsopano, Mwana wa Munthu adzakhala ku dzanja lamanja la Mulungu wamphamvu.”
Ari, jan met Nain aramaj pan mondi ni pali maun en rojon en Kot.
70 Onse anafunsa kuti, “Ndiye kuti ndiwe Mwana wa Mulungu?” Iye anayankha kuti, “Mwanena ndinu kuti Ndine.”
Ir karoj ap idok: Ari, japwilim en Kot koe? A a kotin majani on irail: Komail me indada, pwe nai i.
71 Pamenepo iwo anati, “Nanga tikufuniranjinso umboni wina? Ife tamva kuchokera pa milomo yake.”
Irail indada: Ari, menda apot kadede? Pwe pein kitail rona jan nan au a.

< Luka 22 >