< Luka 17 >

1 Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo.
He said then to the disciples (of Him; *no) Impossible it is that the stumbling blocks not to come, (but *N+kO) woe [to him] through whom they come!
2 Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa.
It is better for him if (a stone of a mill *N+kO) is hung around the neck of him and he has been thrown into the sea than that he may cause to stumble little [ones] of these one.
3 Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha. “Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni.
do take heed to yourselves. If (now *k) shall sin (against *k) (you *K) the brother of you, do rebuke him; and if he shall repent, do forgive him.
4 Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”
And if seven times in the day (he shall sin *N+kO) against you and seven times (day *k) shall return (to *N+kO) you saying: I repent, you will forgive him.
5 Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”
And said the apostles to the Lord; do add to us faith!
6 Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.
Said then the Lord; If (you have *N+kO) faith like a grain of mustard, you have spoken then would to the mulberry tree this; do be uprooted and do be planted in the sea, and it have obeyed would you.
7 “Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’
Which now of you a servant having plowing or shepherding, the [one] having come in out of the field will say to him; Immediately having come (do recline? *N+kO)
8 Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’
But surely he will say to him; do prepare what I may eat, and having girded yourself about do serve me while I may eat and I may drink, and after these things you will eat and will drink you yourself?’
9 Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita?
Not is he thankful to the servant (that [one] *k) because he did the [things] having been commanded (to him not I think? *K)
10 Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’”
Thus also you yourselves, when you may have done all the [things] having been commanded you, do say that Servants unworthy are we; (for *k) that which (we were obliged *NK+o) to do we have done.
11 Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu.
And it came to pass in the going up (him *ko) to Jerusalem that He himself was passing through ([the] midst *N+kO) of Samaria and Galilee.
12 Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali
And when is entering He into a certain village met with Him ten leprous men, who (stood *NK+O) afar off.
13 ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”
And they themselves lifted up [their] voice saying; Jesus Master, do have compassion on us.
14 Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.
And having seen [them] He said to them; Having gone do show yourselves to the priests. And it came to pass in the going them, they were cleansed.
15 Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza.
one then of them having seen that he was healed, turned back with a voice loud glorifying God.
16 Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.
and he fell on [his] face at the feet of Him giving thanks to Him; and he himself was a Samaritan.
17 Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti?
Having answered then Jesus said; (surely *NK+o) the ten were cleansed? But the nine are where?
18 Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?”
None was there found having returned to give glory to God only except foreigner this?
19 Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”
And He said to him; Having risen up do go forth; the faith of you has cured you!
20 Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso,
Having been asked now by the Pharisees when is coming the kingdom of God, He answered to them and said; Not comes the kingdom of God with careful observation,
21 kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”
nor will they say; Behold here or (behold *ko) There. Behold for the kingdom of God in the midst of you is.
22 Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona.
He said then to the disciples; Will come days when you will desire one of the days of the Son of Man to see and not you will behold [it].
23 Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo.
And they will say to you; Behold there or Behold here. Not may go forth nor may follow.
24 Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake.
As for the lightning (which *ko) is flashing from the [one end] under (the *no) sky to the [other end] under [the] sky shines, thus will be (also *k) the Son of Man in the day of Him.
25 Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.
First however it behooves Him many things to suffer and to be rejected by generation this.
26 “Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu.
And even as it came to pass in the days of Noah, thus will it be also in the days of the Son of man:
27 Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.
They were eating, were drinking, were marrying, (were being given in marriage, *N+kO) until that day entered Noah into the ark, and came the flood and destroyed (all. *N+kO)
28 “Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga.
Likewise (even as *N+kO) it came to pass in the days of Lot; they were eating, they were drinking, they were buying, they were selling, they were planting, they were building.
29 Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.
in that then day went out Lot from Sodom, it rained fire and brimstone from heaven and destroyed (all; *N+kO)
30 “Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera.
According (to these *N+kO) will it be in that day the Son of Man is revealed.
31 Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse.
In that [very] day the [one who] will be on the housetop and the goods of him in the house, not he should come down to take away them; and the [one] in (the *k) field likewise not he should return to the [things] back.
32 Kumbukirani mkazi wa Loti!
do remember the wife of Lot!
33 Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga.
Who[ever] if shall seek the life of him (to gain *N+KO) will lose it, (and *k) who[ever] (but *no) (maybe *N+kO) (shall lose *NK+o) (it *k) will preserve it.
34 Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa.
I say to you; in that night there will be two upon bed one: The one will be taken, and the other will be left.
35 Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.
There will be two [women] grinding at the same [place]; (The *no) one will be taken, (and *k) (and *no) the other will be left.
36 Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”
(two in field; one will be taken and another it will be left *K)
37 Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?” Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”
And answering they say to Him; Where, Lord? And He said to them; Where the body [is], there (also *no) the vultures (will be gathered. *N+kO)

< Luka 17 >