< Luka 19 >

1 Yesu analowa mu Yeriko napitirira.
And having entered He was passing through Jericho.
2 Kunali munthu kumeneko dzina lake Zakeyu; iye anali mkulu wa wolandira msonkho ndipo anali wolemera.
And behold a man by name being called Zacchaeus and he himself was a chief tax collector and (he himself *N+kO) (was *k) rich;
3 Iye ankafuna kuona Yesu kuti ndani, koma pokhala wamfupi sanathe chifukwa cha gulu la anthu.
And he was seeking to see Jesus who He is and not he was able because of the crowd, because in stature small he was.
4 Choncho iye anathamangira patsogolo ndipo anakwera mu mtengo wamkuyu kuti amuone Iye, pakuti Yesu ankadutsa njira imeneyo.
And having run (to the *no) front he went up into a sycamore-fig tree so that he may see Him, for (through *k) that [way] He was soon to pass.
5 Yesu atafika pa malopo, anayangʼana mmwamba ndipo anati kwa iye, “Zakeyu, tsika msangamsanga. Ine ndiyenera kukhala mʼnyumba mwako lero.”
And as He came to the place, having looked up Jesus (he saw him and *K) said to him; Zacchaeus, having hurried do come down; today for in the house of you it behooves Me to stay.
6 Ndipo nthawi yomweyo anatsika ndipo anamulandira mosangalala.
And having hurried he came down and received Him rejoicing.
7 Anthu onse ataona zimenezi anayamba kungʼungʼudza, nati, “Iye akupita kuti akakhale mlendo wa wochimwa.”
And having seen [it] (all *N+kO) were grumbling saying that With a sinful man He has entered to stay.
8 Koma Zakeyu anayimirira ndipo anati kwa Ambuye, “Taonani Ambuye! Theka la chuma changa ndipereka kwa osauka ndipo ngati ndinamubera wina aliyense pa chilichonse, ndidzamubwezera mochulukitsa kanayi.”
Having stood then Zacchaeus said to the Lord; Behold the half my possessions Lord, to the poor I give; and if of anyone anything I have defrauded, I restore [it] fourfold.
9 Yesu anati kwa iye, “Lero chipulumutso chafika mʼnyumba ino, chifukwa munthu uyu nayenso ndi mwana wa Abrahamu.
Said then to him Jesus that Today salvation to the house this has come, because also he himself a son of Abraham is;
10 Pajatu Mwana wa Munthu anabwera kudzafunafuna ndi kupulumutsa chotayikacho.”
Came for the Son of Man to seek and to save that having been lost.
11 Pamene iwo ankamvera izi, Iye anapitiriza kuwawuza fanizo, chifukwa Iye anali kufupi ndi Yerusalemu ndipo anthu ankaganiza kuti ufumu wa Mulungu ukanaoneka nthawi yomweyo.
When are hearing now they these things having proceeded He spoke a parable because near being to Jerusalem He and thinking they that immediately is about the kingdom of God to appear.
12 Iye anati, “Munthu wa banja laufumu anapita ku dziko lakutali kukadzozedwa ufumu ndipo kenaka abwerenso kwawo.
He said therefore; A man certain of noble birth proceeded to a country distant to receive for himself a kingdom and to return.
13 Tsono iye anayitana antchito ake khumi ndi kuwapatsa ndalama khumi. Iye anati, ‘Gwiritsani ntchito ndalama izi mpaka nditabwerera.’
Having called then ten servants his own he gave to them ten minas and said to them; (Do trade *NK+o) (in that *NO) (until *k) I come back.
14 “Koma anthu ake anamuda ndipo anatuma nthumwi pambuyo pake kukanena kuti, ‘Sitikufuna munthuyu kuti akhale mfumu yathu.’
But the citizens of him were hating him and sent a delegation after him saying; Not we are willing [for] this [man] to reign over us.
15 “Iye analandira ufumuwo ngakhale zinali zotero, ndipo anabwerera kwawo. Kenaka iye anatumiza uthenga kwa antchito ake amene anawapatsa ndalama aja, ndi cholinga chakuti adziwe chimene anapindula nazo.
And it came to pass on the returning of him having received the kingdom that he directed to be called to him servants these to whom (he had given *N+kO) the money, in order that he may know (who *k) what (they had gained by trading. *N+kO)
16 “Woyamba anabwera ndipo anati, ‘Bwana ndalama zanu zapindula khumi zina.’
Came up then the first saying; lord, the mina of you ten (has produced *N+kO) more minas.
17 “Bwana wakeyo anayankha kuti, Wachita bwino wantchito wabwino. ‘Chifukwa wakhulupirika pa zinthu zazingʼono, lamulira mizinda khumi.’
And He said to him; (well done *N+kO) good servant! Because in very little faithful you were, do be having authority you are over ten cities.
18 “Wachiwiri anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama zanu zapindula zisanu zina.’
And came the second saying; The mina of you, lord, has made five minas.
19 “Bwana anayankha kuti, ‘Iwe lamulira mizinda isanu.’
He said then also to this one; And you yourself over do be five cities.
20 “Kenaka wantchito wina anabwera ndipo anati, ‘Bwana, ndalama yanu nayi; ine ndinayibisa ndi kuyisunga mʼkansalu.
And another came saying; lord, behold the mina of you which I was keeping lying in a piece of cloth;
21 Ine ndimakuopani, chifukwa ndinu munthu wowuma mtima. Inu mumatenga chimene simunachiyike ndi kukolola chimene simunadzale.’
I was afraid for of you, because a man harsh you are; You take up what not you did lay down and you reap what not you did sow.
22 “Bwana wake anayankha kuti, ‘Ine ndikukuweruza iwe ndi mawu ako omwewo. Ndiwe wantchito woyipa. Kani umadziwa kuti ndine munthu wowuma mtima ndi wotenga chimene sindinasungitse, ndi kukolola chimene sindinadzale?
He says (now *k) to him; Out of the mouth of you I will judge you, evil servant. You knew that I myself a man harsh am taking up what not I did lay down and reaping what not I did sow;
23 Nanga nʼchifukwa chiyani sunasungitse ndalama yanga, kuti ine pobwera, ndidzayitenge ndi chiwongoladzanja?’
Then because of why not did you give my money to (the *k) bank, and I myself and I myself having come with interest maybe it collected
24 “Ndipo iye anawuza amene anayimirira pafupi kuti, ‘Tengani ndalama yake ndi kumupatsa amene ali ndi ndalama khumiyo!’”
And to those having stood by he said; do take from him the mina and do give [it] to the [one] the ten minas having.
25 Iwo anati, “Bwana iyeyu ali nazo kale khumi!”
And they said to him; Master, he has ten minas.
26 Iye anayankha kuti, “Ndikukuwuzani kuti, aliyense amene ali nazo, adzapatsidwa zambiri, koma amene alibe, adzalandidwa ngakhale chimene ali nacho.
I say (for *ko) to you that to everyone who is having will be given, from however the [one] not having even that which he has will be taken away (from of him. *ko)
27 Tsono adani anga aja amene sankafuna kuti ndikhale mfumu yawo, abweretseni pano ndi kuwapha ine ndikuona.”
Furthermore the enemies of mine (these *N+kO) those not having been willing [for] me to reign over them do bring here and do slay them before me.
28 Yesu atatha kunena izi, anayendabe kupita ku Yerusalemu.
And having said these things He was going on ahead going up to Jerusalem.
29 Iye atayandikira ku Betifage ndi Betaniya pa phiri lotchedwa Olivi, Iye anatuma awiri a ophunzira nati kwa iwo,
And it came to pass as He drew near to Bethphage and Bethany toward the mount which is being called Olivet He sent two of the disciples (of him *ko)
30 “Pitani mʼmudzi uli patsogolo panu, mukakalowa mʼmudzimo, mukapeza mwana wabulu womangiriridwa amene wina aliyense sanakwerepo. Mukamumasule ndi kubwera naye kuno.
(speaking; *N+kO) do go into the ahead village, in which entering you will find a colt tied on which no [one] ever yet of men has sat; (and *no) having untied it do bring [it].
31 Ngati wina aliyense akakufunsani kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mukumumasula mwana buluyo?’ Mukamuwuze kuti, ‘Ambuye akumufuna.’”
And if anyone you shall ask; Because of why do you untie [it]? thus will you say (to him: *k) Because the Lord of it need has.’
32 Otumidwawo anapita nakamupeza mwana wabulu monga momwe Yesu anawawuzira.
Having departed then those sent found [it] even as He had said to them.
33 Pamene ankamasula mwana wabuluyo, eni ake anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukumasula mwana wabuluyo?”
When are untying then they the colt said the masters of it to them; Why untie you the colt?
34 Iwo anayankha kuti, “Ambuye akumufuna.”
And they said: (that *no) The Lord of it need has.
35 Iwo anabweretsa buluyo kwa Yesu, naponya zovala zawo pa bulupo ndi kumukwezapo Yesu.
And they led it to Jesus, and having cast (their *N+kO) garments on the colt they put on [it] Jesus.
36 Pamene ankapita, anthu anayala zovala zawo mu msewu.
When is going then He they were spreading the garments (of them *NK+o) on the road.
37 Iye atafika pafupi ndi pamene msewu umatsikira ku phiri la Olivi, gulu lonse la ophunzira linayamba kuyamika Mulungu mwachimwemwe ndi mawu ofuwula chifukwa cha zodabwitsa zonse anaziona.
When is drawing near then he already at the descent of the Mount of Olives began all the multitude of the disciples rejoicing to praise God in a voice loud for (all *NK+o) which they had seen [the] mighty works
38 “Yodala mfumu imene ikubwera mʼdzina la Ambuye!” “Mtendere kumwamba ndi ulemerero mmwambamwamba!”
saying: Blessed [is] the coming King in [the] name of [the] Lord; In heaven peace, and glory in [the] highest.
39 Ena mwa Afarisi mʼgulumo anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, adzudzuleni ophunzira anu!”
And some of the Pharisees from the crowd said to Him; Teacher, do rebuke the disciples of You.
40 Iye anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani kuti, ngati atakhala chete, miyala idzafuwula.”
And answering He said (to them: *ko) I say to you (that *ko) if these (will be silent, *N+kO) the stones (will cry out. *N+kO)
41 Iye atayandikira ku Yerusalemu ndi kuona mzindawo, anawulirira
And as He drew near, having seen the city He wept over (it *N+kO)
42 nati, “Iwe ukanadziwa lero lino zinthu zokubweretsera mtendere, koma tsopano zabisikira maso ako.
saying that If you had known (and indeed *k) in the day (of you *k) this even you yourself the [things] for peace (of you; *ko) Now however they are hidden from eyes of you.
43 Pakuti masiku adzabwera pamene adani ako adzamanga mitumbira yankhondo nakuzungulira, nadzakutsekereza mbali zonse.
For will come days upon you that (will cast around *N+kO) the enemies of you a barricade you and they will surround you and they will hem in you on every side
44 Iwo adzakugwetsera pansi, iwe, ana ako onse a mʼkati mwako. Iwo sadzasiya mwa iwe mwala wina pa unzake, chifukwa sunazindikire nthawi ya kubwera kwa Mulungu.”
and will level to the ground you and the children of you within you and not will leave a stone upon (a stone *N+kO) within you, because which not you knew the season of visitation of you.
45 Kenaka Iye analowa mʼdera la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kutulutsa kunja amene amachita malonda.
And having entered into the temple He began to cast out those selling (in to it *k) (and buying *K)
46 Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzakhala nyumba ya mapemphero, koma inu mwayisadutsa phanga la achifwamba.”
saying to them; It has been written: (And *no) (will be *N+kO) the house of Mine a house of prayer’; You yourselves however it made a den of robbers.’
47 Tsiku lililonse amaphunzitsa mʼNyumba ya Mulungu. Koma akulu a ansembe, aphunzitsi amalamulo ndi atsogoleri pakati pa anthu amayesetsa kuti amuphe.
And He was teaching every day in the temple; the however chief priests and the scribes were seeking Him to destroy and the foremost of the people,
48 Komabe iwo sanathe kupeza njira ina iliyonse kuti achite izi, chifukwa anthu onse anakhulupirira mawu ake.
And not they were finding what they may do; the people for all were hanging on His [words] listening.

< Luka 19 >