< Yohane 1 >

1 Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
In [the] beginning was the Word, and the Word was with God, and God was the Word.
2 Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
He was in [the] beginning with God.
3 Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa.
All things through Him came into being, and without Him came into being not even one [thing] that has come into being.
4 Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
In Him life was, and the life was the light of men,
5 Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
And the Light in the darkness shines, and the darkness it not grasped [it].
6 Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane.
There came a man sent from God, [the] name to Him [was] John.
7 Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire.
He came as a witness that he may testify concerning the Light, that all may believe through him.
8 Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika.
Not was He the Light, but that he may witness concerning the Light.
9 Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
Was the Light true who enlightens every man coming into the world.
10 Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye.
In the world He was, and the world through Him came into being, and the world Him not knew.
11 Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
To [His] own He came, and [His] own Him not received.
12 Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu;
As many as however received Him, He gave to them authority children of God to be, to those believing in the name of Him,
13 ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
who not [born] of blood nor [born] of will of flesh nor [born] of will of man but of God were born.
14 Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
And the Word flesh became and He dwelt among us, and we beheld the glory of Him, a glory as of an only begotten from [the] Father, full of grace and truth.
15 Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’”
John witnesses concerning Him and he has cried out saying; This was He (of whom I was saying; *NK+o) The [One] after me coming precedence over me has, because before me He was.’
16 Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso.
(For *N+KO) from the fullness of Him we ourselves all have received then grace for grace.
17 Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
For the law through Moses was given, grace and truth through Jesus Christ came.
18 Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
God no [one] has seen ever yet; (the *ko) only begotten (God *N+KO) who is being in the bosom of the Father, He has made [Him] known.
19 Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani.
And this is the testimony of John when sent (to him *no) the Jews from Jerusalem priests and Levites that they may ask him; You yourself who are?
20 Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
And he confessed and not denied but confessed that I myself not am the Christ.
21 Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?” Iye anati, “Sindine.” “Kodi ndiwe Mneneri?” Iye anayankha kuti, “Ayi.”
And they asked him; What then? You yourself Elijah are And he says; Not I am. The prophet are you yourself? And he answered; No.
22 Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
They said therefore to him; Who are you? That an answer we may give to those having sent us; what say you about yourself?
23 Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’”
He was saying; I myself [am] a voice crying in the wilderness; do make straight the way of [the] Lord; even as said Isaiah the prophet.
24 Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa
And (those *k) sent were out from the Pharisees
25 anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
And they asked him and they said to him; Why then baptize you if you yourself not are the Christ (nor *N+kO) Elijah (nor *N+kO) the prophet?
26 Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa.
Answered them John saying; I myself baptize with water; [in the] midst (now *k) of you (he has stood *NK+o) whom you yourselves not know,
27 Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
(he himself is *k) the [One] after me coming, (who before me has been; *K) of whom not am I myself worthy that I may untie of Him the strap of the sandal.
28 Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
These things in (Bethany *N+kO) took place across the Jordan where was John baptizing.
29 Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
On the next day he sees (John *k) Jesus coming to him and says; Behold the Lamb of God, who is taking away the sin of the world.
30 Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’
He it is (concerning *N+kO) whom I myself said; After me comes a man who precedence over me has because before me He was.
31 Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
And I myself And I myself not knew Him, but that He may be revealed to Israel, because of this came I myself with water baptizing.
32 Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye.
And bore witness John saying that I have beheld the Spirit descending (as *N+kO) a dove out of heaven, and it remained upon Him.
33 Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’
And I myself And I myself not knew Him, but the [One] having sent me to baptize with water, He to me said; Upon whom maybe you may see the Spirit descending and abiding on Him, He is the [One] baptizing with [the] Spirit Holy.
34 Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
And I myself And I myself have seen and have borne witness that this is the (Son *NK+O) of God.
35 Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake.
On the next day again had stood John and of the disciples of him two.
36 Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
And having looked at Jesus walking he says; Behold the Lamb of God!
37 Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu.
And heard the two disciples of Him [Him] speaking and they followed Jesus.
38 Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
Having turned then Jesus and having beheld them following He says to them; What seek you? And they said to Him; Rabbi which is to say (meaning *N+kO) Teacher — where are You staying?
39 Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.” Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
He says to them; do come and (you will behold. *N+kO) They went (therefore *NO) and saw where He abides, and with Him they stayed the day that; [The] hour (now *k) was about [the] tenth.
40 Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu.
Was Andrew the brother of Simon Peter one of the two which having heard from John and having followed Him.
41 Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
Finds he (first *N+kO) the brother [his] own Simon and he says to him; We have found the Messiah, which is being translated Christ.
42 Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
(and *k) He led him to Jesus. Having looked at (now *k) him Jesus said; You yourself are Simon the son (of John; *N+KO) You yourself will be called Cephas which means Peter.
43 Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
On the next day He desired to go forth into Galilee And He finds Philip And says to him Jesus; do follow Me.
44 Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida.
Was now Philip from Bethsaida, from the city of Andrew and Peter.
45 Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
Finds Philip Nathanael and says to him; [Him] whom wrote of Moses in the Law also the prophets, we have found, Jesus son of Joseph of Nazareth.
46 Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?” Filipo anati, “Bwera udzaone.”
And said to him Nathanael; Out of Nazareth is able any good thing to be? Says to him Philip; do come and do see.
47 Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
Saw Jesus Nathanael coming to Him and He says concerning him; Behold truly an Israelite in whom deceit not there is.
48 Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?” Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
Says to Him Nathanael; From where me know You? Answered Jesus and said to him; Before you Philip calling being under the fig tree I saw you.
49 Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
Answered to him Nathanael (and says: *k) Rabbi, You yourself are the Son of God, You yourself King are of Israel.
50 Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.”
Answered Jesus and said to him; Because I said to you (that *no) I saw you under the fig tree, believe you? Greater things than these You will see.
51 Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”
And He says to him; Amen Amen I say to all of you (from now *K) you will behold the heaven having opened and the angels of God ascending and descending on the Son of Man.

< Yohane 1 >