< Levitiko 18 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises, and seide, Speke thou to the sones of Israel,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
and thou schalt seie to hem, Y am youre Lord God;
3 Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
ye schulen not do by the custom of the lond of Egipt, in which ye dwelliden; ye schulen not do bi the custom of the cuntrei of Canaan, `to which Y schal brynge you yn, nethir ye schulen go in the lawful thingis of hem.
4 Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Ye schulen do my domes, and ye schulen kepe myn heestis, and ye schulen go in tho; Y am youre Lord God.
5 Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
Kepe ye my lawis and domes, whiche a man `schal do, and schal lyue in tho; Y am youre Lord God.
6 “‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
Ech man schal not neiy to the nyy womman of his blood, that he schewe `the filthe of hir; Y am the Lord.
7 “‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
Thou schalt not diskyuere the filthe of thi fadir and the filthe of thi modir; sche is thi modir, thou schalt not schewe hir filthe.
8 “‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
Thou schalt not vnhile the filthe of the wijf of thi fadir, for it is the filthe of thi fadir.
9 “‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
Thou schalt not schewe the filthe of thi sistir, of fadir `ether of modir, which sister is gendrid at hoome ether without forth.
10 “‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
Thou schalt not schewe the filthe of the douyter of thi sone, ether of neece of thi douyter, for it is thi filthe.
11 “‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
Thou schalt not schewe the filthe of the douyter of the wijf of thi fadir, which sche childide to thi fadir, and is thi sistir.
12 “‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
Thou schalt not opene the filthe of the `sister of thi fadir, for sche is the fleisch of thi fadir.
13 “‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
Thou schalt not schewe the filthe of the sistir of thi modir, for sche is the fleisch of thi modir.
14 “‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
Thou schalt not shewe the filthe of the brothir of thi fadir, nethir thou schalt neiye to his wijf, which is ioyned to thee bi affinyte.
15 “‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
Thou schalt not schewe the filthe of thi sones wijf, for sche is the wijf of thi sone, nether thou schalt diskiuere hir schenschip; and no man take his brotheris wijf.
16 “‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
Thou schalt not schewe the filthe of `the wijf of thi brother, for it is the filthe of thi brothir.
17 “‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
Thou schalt not schewe the filthe of thi wijf, and of hir douyter; thou schalt not take the douytir of hir sone, and the douytir of hir douyter, that thou schewe hir schenschip; thei ben the fleisch of hir, and siche letcherie is incest.
18 “‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
Thou schalt not take `the sister of thi wijf, in to concubynage of hir, nethir thou schalt schewe `the filthe of hir, while thi wijf lyueth yit.
19 “‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
Thou schalt not neiye to a womman that suffrith rennyng of blood of monethe, nethir thou schalt schewe hir filthe.
20 “‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
Thou schalt not do letcherie with `the wijf of thi neiybore, nether thou schalt be defoulid with medlyng of seed.
21 “‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
Thou schalt not yyue of thi seed, that it be offrid to the idol Moloch, nether thou schalt defoule the name of thi God; Y am the Lord.
22 “‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
Thou schalt not be medlid with a man bi letcherie of womman, for it is abhomynacioun.
23 “‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
Thou schalt not do letcherie with ony beeste, nethir thou schalt be defoulid with it. A womman schal not ligge vnder a beeste, nether schal be medlid therwith, for it is greet synne.
24 “‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
Be ye not defoulid in alle these thingis, in whiche alle `folkis, ether hethen men, ben defoulid, whiche folkis Y schal caste out bifor youre siyt,
25 Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
of whiche the lond is defoulid, of which lond Y schal vysyte the grete synnes, that it spewe out hise dwellers.
26 Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
Kepe ye my lawful thingis and domes, that ye do not of alle these abhomynaciouns, as wel a man borun in the lond as a comelyng which is a pilgrym at you.
27 pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
For the dwellers of the lond, that weren bifor you, diden alle these abhomynaciouns, and defouliden that lond.
28 Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
Therfor be ye war, lest it caste out viliche also you in lijk manere, whanne ye han do lijk synnes, as it castide out vileche the folk, that was bifor you.
29 “‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
Ech man that doith ony thing of these abhomynaciouns, schal perische fro the myddis of his puple.
30 Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Kepe ye myn heestis; nyle ye do tho thingis, whiche thei that weren bifor you diden, and be ye not defoulid in tho; Y am youre Lord God.

< Levitiko 18 >