< Levitiko 17 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises, and seide, Speke thou to Aaron,
2 “Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi:
and to hise sones, and to alle the sones of Israel, and seie thou to hem, This is the word which the Lord comaundide,
3 Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa,
and seide, Ech man of the hows of Israel schal be gilti of blood, if he sleeth an oxe, ether a scheep, ethir a geet in the castels, ethir out of the castels,
4 mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
and offrith not an offryng to the Lord at the dore of the tabernacle; as he schedde mannus blood, so he schal perische fro the myddis of his puple.
5 Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano.
Therfor the sones of Israel owen to offre her sacrifices to the preest, whiche thei sleen in the feeld, that tho be halewid to the Lord, bifor the dore of the tabernacle of witnessyng, and that thei offre tho pesible sacrifices to the Lord.
6 Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova.
And the preest schal schede the blood on the auter of the Lord, at the dore of the tabernacle of witnessyng; and he schal brenne the ynnere fatnesse in to odour of swetnesse to the Lord.
7 Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’”
And thei schulen no more offre her sacrifices to fendis, with whiche thei diden fornycacioun; it schal be a lawful thing euerlastynge to hem, and to the aftircomeris `of hem.
8 “Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse
And thou schalt seie to hem, A man of the hows of Israel, and of the comelyngis that ben pilgryms among you, that offrith a brent sacrifice, ethir a slayn sacrifice,
9 popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’”
and bryngith it not to the dore of the tabernacle of witnessyng, that it be offrid to the Lord, schal perische fro his puple.
10 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake.
If ony man of the sones of Israel, and of comelyngis that ben pilgryms among you, etith blood, Y schal sette faste my face ayens `the soule of hym, and Y schal leese hym fro his puple;
11 Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo.
for the lijf of fleisch is in blood, and Y yaf that blood to you, that ye clense on myn auter `for youre soulis, and that the blood be for the synne of soule.
12 Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’”
Therfor Y seide to the sones of Israel, Ech lyuynge man of you schal not ete blood, nethir of the comelyngis that ben pilgryms among you.
13 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi,
What euer man of the sones of Israel, and of the comelyngis that ben pilgryms anentis you, takith a wielde beeste, ethir a brid, whiche it is leueful to ete, whether bi huntyng, whether bi haukyng, schede the blood therof, and hile it with erthe;
14 chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
for the lijf of ech fleisch is in blood. Wherfor Y seide to the sones of Israel, Ye schulen not ete the blood of ony fleisch, for the lijf of fleisch is in blood, and who euer etith blood, schal perische.
15 “‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa.
A man that etith a thing deed bi it silf, ethir takun of a beeste, as wel of men borun in the lond, as of comelyngis, he schal waische hise clothis and hym silf in watir, and he schal be `defoulid til to euentid; and by this ordre he schal be maad cleene; that if he waischith not his clothis,
16 Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’”
ether his bodi, he schal bere his wickidnesse.

< Levitiko 17 >