< Yoswa 14 >

1 Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli.
A ovo je što dobiše našljedstvo sinovi Izrailjevi u zemlji Hananskoj, što razdijeliše u našljedstvo Eleazar sveštenik i Isus sin Navin i poglavari porodica otaèkih po plemenima sinova Izrailjevih,
2 Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose.
Ždrijebom dijeleæi im našljedstvo, kao što zapovijedi Gospod preko Mojsija, meðu devet plemena i polovinu plemena.
3 Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo.
Jer Mojsije dade našljedstvo dvjema plemenima i polovini plemena s ovu stranu Jordana, a Levitima ne dade našljedstva meðu njima.
4 Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo.
Jer sinova Josifovijeh bjehu dva plemena: Manasijino i Jefremovo, i Levitima ne dadoše dijela u zemlji, osim gradova u kojima æe živjeti i podgraða njihovijeh za stoku njihovu i za blago njihovo.
5 Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
Kako bješe zapovjedio Gospod Mojsiju, tako uèiniše sinovi Izrailjevi i podijeliše zemlju.
6 Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea.
A sinovi Judini doðoše k Isusu u Galgalu, i reèe mu Halev sin Jefonijin Kenezej: ti znaš šta je kazao Gospod Mojsiju sluzi Božijemu za me i za te u Kadis-Varniji.
7 Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera.
Bilo mi je èetrdeset godina kad me posla Mojsije sluga Gospodnji iz Kadis-Varnije da uhodim zemlju, i javih mu stvar, kako mi je bilo u srcu.
8 Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.
A braæa moja što idoše sa mnom uplašiše srce narodu; ali se ja jednako držah Gospoda Boga svojega.
9 Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’
I zakle se Mojsije onaj dan govoreæi: zaista zemlja po kojoj si hodio nogama svojima, dopašæe tebi u našljedstvo i sinovima tvojim dovijeka; jer si se sasvijem držao Gospoda Boga mojega.
10 “Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85.
A sada, eto, saèuva me Gospod u životu, kao što je rekao; ima veæ èetrdeset i pet godina kako to reèe Gospod Mojsiju, kad Izrailj iðaše po pustinji; i sad, eto, ima mi danas osamdeset i pet godina.
11 Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse.
I danas sam jošte krjepak, kao što sam bio kad me je Mojsije slao; krjepost mi je i sad onaka kaka je bila onda za boj i da odlazim i dolazim.
12 Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”
Zato daj mi sada ovu goru, za koju je govorio Gospod u onaj dan; jer si èuo u onaj dan da su ondje Enakimi i gradovi veliki i tvrdi; da ako bude Gospod sa mnom, te ih istjeram, kao što je Gospod kazao.
13 Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake.
I Isus ga blagoslovi, i dade Hevron Halevu sinu Jefonijinu u našljedstvo.
14 Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse.
Zato pripade Hevron Halevu sinu Jefonijinu Kenezeju u našljedstvo do današnjega dana, jer se jednako držao Gospoda Boga Izrailjeva.
15 (Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki). Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.
A ime Hevronu bijaše preðe Kirijat-Arva, a Arva bijaše velik èovjek meðu Enakimima. I zemlja poèinu od rata.

< Yoswa 14 >