< Oweruza 1 >

1 Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
A po smrti Isusovoj upitaše sinovi Izrailjevi Gospoda govoreæi: ko æe izmeðu nas iæi prvi na Hananeje da se bije s njima?
2 Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
I Gospod reèe: Juda neka ide; eto dao sam mu zemlju u ruke.
3 Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
A Juda reèe Simeunu bratu svojemu: hajde sa mnom na moj dio da se bijemo s Hananejima; pak æu i ja iæi s tobom na tvoj dio. I poðe Simeun s njim.
4 Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
I izide Juda; i dade im Gospod Hananeje i Ferezeje u ruke, i pobiše ih u Vezeku deset tisuæa ljudi.
5 Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
Jer naðoše Adoni-Vezeka u Vezeku, i udariše na nj, i pobiše Hananeje i Ferezeje.
6 Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
I pobježe Adoni-Vezek, a oni ga potjeraše i uhvativši ga otsjekoše mu palce u ruku i u nogu.
7 Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
Tada reèe Adoni-Vezek: sedamdeset careva otsjeèenijeh palaca u ruku i u nogu kupiše što bješe pod mojim stolom; kako sam èinio, tako mi plati Bog. I odvedoše ga u Jerusalim, i ondje umrije.
8 Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
Jer sinovi Judini udariše na Jerusalim i uzeše ga, i isjekoše graðane oštrijem maèem, a grad sažegoše ognjem.
9 Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
Potom izidoše sinovi Judini da vojuju na Hananeje, koji življahu u gori i na jugu i u ravni.
10 Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
I Juda izide na Hananeje koji življahu u Hevronu, a Hevronu bijaše preðe ime Kirijat-Arva; i pobiše Sesaja i Ahimana i Talmaja.
11 Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
A odatle otidoše na Davirane, a Daviru prije bješe ime Kirijat-Sefer.
12 Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
I reèe Halev: ko savlada Kirijat-Sefer i uzme ga, daæu mu Ahsu kæer svoju za ženu.
13 Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
I uze ga Gotonilo, sin Kenezov, mlaði brat Halevov; i dade mu Ahsu kæer svoju za ženu.
14 Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
I kad polažaše, nagovaraše ga da ište u oca njezina polje; pa skoèi s magarca. A Halev joj reèe: što ti je?
15 Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
A ona mu reèe: daj mi dar; kad si mi dao suhe zemlje, daj mi i izvora vodenijeh. I dade joj Halev izvore gornje i izvore donje.
16 Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
A i sinovi Keneja tasta Mojsijeva izidoše iz grada palmova sa sinovima Judinijem u pustinju Judinu, koja je na jugu od Arada. I došavši življahu s narodom.
17 Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
Potom izide Juda sa Simeunom bratom svojim, i pobiše Hananeje koji življahu u Sefatu, i raskopaše ga, i prozva se grad Orma.
18 Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
I Gazu uze Juda s meðama njezinijem, i Askalon s meðama njegovijem, i Akaron s meðama njegovijem.
19 Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
Jer Gospod bješe s Judom, te osvoji goru; ali ne izagna onijeh koji življahu u dolini, jer imahu gvozdena kola.
20 Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
I dadoše Halevu Hevron, kao što bješe zapovjedio Mojsije, a on izagna odande tri sina Enakova.
21 Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
A sinovi Venijaminovi ne izagnaše Jevuseja koji življahu u Jerusalimu; nego Jevuseji ostaše u Jerusalimu sa sinovima Venijaminovijem do ovoga dana.
22 A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
Izidoše i sinovi Josifovi na Vetilj, i Gospod bijaše s njima.
23 Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
I uhodiše Vetilj sinovi Josifovi, a ime gradu bješe prije Luz.
24 Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
I uhode vidješe èovjeka koji iðaše iz grada i rekoše mu: hajde pokaži nam kuda æemo uæi u grad, pa æemo ti uèiniti milost.
25 Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
A on im pokaza kuda æe uæi u grad; i isjekoše u gradu sve oštrijem maèem, a onoga èovjeka pustiše sa svom porodicom njegovom.
26 Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
I otide onaj èovjek u zemlju Hetejsku, i ondje sazida grad, i prozva ga Luz; to mu je ime do danas.
27 Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
A Manasija ne izagna stanovnika iz Vet-Sana i sela njegovijeh, ni iz Tanaha i sela njegovijeh, ni stanovnika iz Dora i sela njegovijeh, ni stanovnika iz Ivleama i sela njegovijeh, ni stanovnika iz Megida i sela njegovijeh; i Hananeji stadoše živjeti u toj zemlji.
28 Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
A kad ojaèa Izrailj, udari na Hananeje danak, ali ih ne izagna.
29 Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
Ni Jefrem ne izagna Hananeja koji življahu u Gezeru; nego ostaše Hananeji s njim u Gezeru.
30 Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Zavulon ne izagna stanovnika iz Kitrona, ni stanovnika iz Nalola; nego ostaše Hananeji s njim, i plaæahu danak.
31 A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
Asir ne izagna stanovnika iz Akona, ni stanovnika iz Sidona ni iz Alava, ni iz Ahaziva, ni iz Helve, ni iz Afika, ni iz Reova;
32 Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
Nego Asir življaše meðu Hananejima, stanovnicima one zemlje, jer ih ne izagna.
33 Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
Neftalim ne izagna stanovnika iz Vet-Semesa, ni stanovnika iz Vet-Anata; nego življaše meðu Hananejima stanovnicima one zemlje; i stanovnici u Vet-Semesu i u Vet-Anatu plaæahu im danak.
34 Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
A Amoreji pritješnjavahu sinove Danove u gori, i ne dadijahu im slaziti u dolinu.
35 Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
I Amoreji stadoše živjeti u gori Eresu, u Ajalonu i u Salvimu; a kad osili ruka doma Josifova, plaæaše danak.
36 Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.
A meða Amorejima bješe od gore Akravimske, od stijene pa na više.

< Oweruza 1 >