< Yoswa 24 >

1 Tsono Yoswa anasonkhanitsa mafuko onse a Israeli ku Sekemu. Iye anayitanitsa akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi akuluakulu a boma la Israeli, ndipo iwo anafika pamaso pa Mulungu.
Potom sabra Isus sva plemena Izrailjeva u Sihem, i sazva starješine Izrailjeve i poglavare njegove i sudije njegove i upravitelje njegove, i stadoše pred Bogom.
2 Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
I reèe Isus svemu narodu: ovako veli Gospod Bog Izrailjev: s onu stranu rijeke živješe negda oci vaši, Tara otac Avramov i otac Nahorov, i služiše drugim bogovima.
3 Koma ine ndinatenga kholo lanu Abrahamu kumuchotsa ku dziko la kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndipo ndinamutsogolera kupita ku dziko la Kanaani. Ndinamupatsa zidzukulu zambiri. Ndinamupatsa Isake,
Ali uzeh oca vašega Avrama ispreko rijeke i provedoh ga kroz svu zemlju Hanansku i umnožih sjeme njegovo davši mu Isaka.
4 ndipo Isake ndinamupatsa Yakobo ndi Esau. Ndinapereka dziko la mapiri la Seiri kwa Esau, koma Yakobo ndi ana ake anapita ku Igupto.
A Isaku dadoh Jakova i Isava, i dadoh Isavu goru Sir da je njegova; a Jakov i sinovi njegovi sidoše u Misir.
5 “‘Kenaka ndinatuma Mose ndi Aaroni, ndipo ine ndinazunza Aigupto. Pambuyo pake ndinakutulutsani.
I poslah Mojsija i Arona, i muèih Misir, kako uèinih usred njega, potom vas izvedoh.
6 Nditatulutsa makolo anu ku Igupto ndinafika nawo ku Nyanja Yofiira. Aigupto anawathamangira ndi magaleta ndi okwera pa akavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.
A kad izvedoh iz Misira oce vaše, doðoše na more, a Misirci gnaše oce vaše s kolima i s konjicima do Crvenoga Mora.
7 Tsono makolo anuwo anapemphera kwa Ine kuti ndiwathandize, ndipo ndinayika mtambo wakuda pakati pawo ndi Aiguptowo, ndipo Nyanja inamiza Aigupto aja. Inu munaona ndi maso anu zimene ndinachita kwa Aiguptowo ndipo inu munakhala mʼchipululu nthawi yayitali.
Tada zavapiše ka Gospodu, i postavih tamu izmeðu vas i Misiraca, i navedoh na njih more koje ih zatrpa, i oèi vaše vidješe šta uèinih od Misiraca; potom ostaste u pustinji dugo vremena.
8 “‘Pambuyo pake Ine ndinabwera nanu ku dziko la Aamori amene amakhala kummawa kwa Yorodani. Iwo anamenyana nanu koma ndinawapereka mʼdzanja lanu. Ndinawawononga pamaso panu, ndipo inu munalanda dziko lawo.
Iza toga dovedoh vas u zemlju Amoreja koji življahu s onu stranu Jordana; i oni se pobiše s vama, ali ih dadoh vama u ruke, te naslijediste zemlju njihovu, i istrijebih ih ispred vas.
9 Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, analimbana ndi Israeli. Iye anayitanitsa Balaamu mwana wa Beori kuti akutemberereni.
A Valak sin Seforov car Moavski podiže se da se bije s Izrailjem, i posla te dozva Valama sina Veorova da vas prokune.
10 Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.
Ali ne htjeh poslušati Valama, te vas on još blagoslovi, i izbavih vas iz ruke njegove.
11 “‘Ndipo inu munawoloka Yorodani ndi kufika ku Yeriko. Anthu a ku Yeriko analimbana nanu pamodzi ndi Aamori, Aperezi, Akanaani, Ahiti, Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi. Koma Ine ndinawapereka mʼdzanja lanu.
Potom prijeðoste preko Jordana, i doðoste pod Jerihon, i biše se s vama Jerihonjani, Amoreji i Ferezeji i Hananeji i Heteji i Gergeseji i Jeveji i Jevuseji; i dadoh ih vama u ruke.
12 Ine ndinatumiza mavu amene anapirikitsa mafumu awiri Aamori aja pamaso panu. Inu simunachite izi ndi lupanga ndi uta wanu.
I poslah pred vama stršljene, koji ih izagnaše ispred vas, dva cara Amorejska; ne maèem tvojim ni lukom tvojim.
13 Motero ndinakupatsani dziko limene simunalivutikire ndiponso mizinda imene simunamange. Inu mukukhala mʼmenemo ndi kumadya zipatso za mʼmunda wamphesa ndi kuthyola zipatso mʼmitengo ya olivi zimene simunadzale.’
I dadoh vam zemlju, koje ne radiste, i gradove, kojih ne gradiste, i u njima živite; iz vinograda i iz maslinika, kojih nijeste sadili, jedete.
14 “Ndipo tsopano wopani Yehova ndi kumutumikira Iye mokhulupirika ndi moona. Chotsani milungu imene makolo anu ankapembedza kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndi ku Igupto ndipo tumikirani Yehova.
Zato sada bojte se Gospoda i služite mu vjerno i istinito; i povrzite bogove, kojima su služili oci vaši s onu stranu rijeke i u Misiru, pa služite Gospodu.
15 Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova.”
Ako li vam nije drago služiti Gospodu, izberite sebi danas kome æete služiti: ili bogove kojima su služili oci vaši s onu stranu rijeke, ili bogove Amoreja u kojih zemlji živite; a ja i dom moj služiæemo Gospodu.
16 Ndipo anthu anayankha, “Sizingatheke kuti timusiye Yehova ndi kutumikira milungu ina!
A narod odgovori i reèe: ne daj Bože da ostavimo Gospoda da služimo drugim bogovima.
17 Yehova Mulungu wathu ndiye amene anatitulutsa ife ndi makolo athu mu ukapolo, mʼdziko la Igupto. Tinaona ndi maso athu zizindikiro zozizwitsa zimene anachita. Iye anatiteteza pa ulendo wathu wonse ndi pakati pa mitundu yonse imene tinkakumana nayo.
Jer Gospod Bog naš, on je izveo nas i oce naše iz zemlje Misirske, iz doma ropskoga, i on je uèinio pred našim oèima one znake velike, i èuvao nas cijelijem putem kojim idosmo, i po svijem narodima kroz koje proðosmo.
18 Ife tikufika Iye anapirikitsa anthu onse pamodzi ndi Aamori amene ankakhala mʼdzikoli. Ifenso tidzatumikira Yehova chifukwa Iye ndiye Mulungu.”
I Gospod je istjerao ispred nas sve narode i Amoreje, koji življahu u ovoj zemlji; i mi æemo služiti Gospodu, jer je Bog naš.
19 Koma Yoswa anati kwa anthuwo, “Inutu simungathe kutumikira Yehova. Iye ndi Mulungu woyera, salola kupikisana naye. Sadzakukhululukirani ngati mumuwukira ndi kumuchimwira.
A Isus reèe narodu: ne možete služiti Gospodu, jer je svet Bog, Bog revnitelj, neæe podnositi vaše nevjere i vaših grijeha.
20 Ngati inu musiya Yehova ndi kutumikira milungu yachilendo, adzakufulatirani. Iye adzakulangani ndi kukuwonongani ngakhale kuti poyamba anakuchitirani zabwino.”
Kad ostavite Gospoda i stanete služiti tuðim bogovima, okrenuæe se i zlo æe vam uèiniti, i istrijebiæe vas, pošto vam je dobro èinio.
21 Koma anthuwo anati kwa Yoswa, “Ayi! Ife tidzatumikira Yehova.”
A narod reèe Isusu: ne, nego æemo Gospodu služiti.
22 Kenaka Yoswa anati, “Inu mukudzichitira nokha umboni kuti mwasankha kutumikira Yehova.” Iwo anayankha kuti, “Inde ife ndife mboni.”
A Isus reèe narodu: sami ste sebi svjedoci da ste izabrali sebi Gospoda da mu služite. I oni rekoše: svjedoci smo.
23 Yoswa anati, “Tsono chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu ndipo perekani mitima yanu kwa Yehova Mulungu wa Israeli.”
Povrzite dakle bogove tuðe što su meðu vama, i privijte srce svoje ka Gospodu Bogu Izrailjevu.
24 Ndipo anthuwo anati kwa Yoswa, “Ife tidzatumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera Iye.”
A narod reèe Isusu: Gospodu Bogu svojemu služiæemo i glas njegov slušaæemo.
25 Choncho pa tsiku limenelo Yoswa anachita pangano mʼmalo mwa anthuwo, ndipo pa Sekemu pomwepo iye anapereka malamulo ndi malangizo kwa anthu aja.
Tako uèini Isus zavjet s narodom onaj dan i postavi im uredbe i zakone u Sihemu.
26 Ndipo Yoswa analemba zinthu izi mʼbuku la malamulo a Mulungu. Kenaka iye anatenga mwala waukulu nawuyimika pansi pa mtengo wa thundu pa malo wopatulika a Yehova.
I zapisa Isus ove rijeèi u knjigu zakona Božijega; i uzevši kamen velik podiže ga ondje pod hrastom koji bijaše kod svetinje Gospodnje.
27 Yoswa anati kwa anthu onse, “Tamvani! Mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa. Mwalawu wamva mawu onse amene Yehova wayankhula kwa ife. Udzakhala mboni yotitsutsa ngati mukhala osakhulupirika kwa Mulungu wanu.”
I reèe Isus svemu narodu: evo, kamen ovaj neka vam bude svjedoèanstvo; jer je èuo sve rijeèi Gospodnje, koje nam je govorio; i neka vam bude svjedoèanstvo da ne biste slagali Bogu svojemu.
28 Kenaka Yoswa analola anthu kuti apite, aliyense ku dera lake.
Potom raspusti Isus narod, svakoga na njegovo našljedstvo.
29 Zitatha zinthu izi, Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110,
A poslije ovijeh stvari umrije Isus sin Navin sluga Gospodnji, kad mu bijaše sto i deset godina.
30 ndipo anamuyika mʼmanda mʼdziko lake, ku Timnati-Sera dziko lamapiri la ku Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
I pogreboše ga u meðama našljedstva njegova u Tamnat-Sarahu, koji je u gori Jefremovoj sa sjevera gori Gasu.
31 Israeli anatumikira Yehova pa nthawi yonse imene Yoswa anali ndi moyo ndiponso pa nthawi ya akuluakulu amene anali moyo Yoswa atamwalira, anthu amene ankadziwa zonse zimene Yehova anachitira Israeli.
I služi Izrailj Gospodu svega vijeka Isusova i svega vijeka starješina, koje dugo živješe iza Isusa i koje znahu sva djela Gospodnja, koja uèini Izrailju.
32 Ndipo mafupa a Yosefe amene Aisraeli anawatulutsa ku Igupto anawayika mʼmanda a ku Sekemu pa malo amene Yakobo anagula ndi ndalama zasiliva 100 kwa ana a Hamori, abambo a Sekemu. Malo awa anakhala cholowa cha adzukulu a Yosefe.
I kosti Josifove, koje donesoše sinovi Izrailjevi iz Misira, pogreboše u Sihemu, u dijelu polja koje je kupio Jakov od sinova Emora oca Sihemova za sto novaca; i biše u sinova Josifovijeh u našljedstvu njihovu.
33 Ndipo Eliezara mwana wa Aaroni anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda ku Gibeya, malo amene anapatsidwa kwa Finehasi mwana wake, mʼdziko lamapiri la Efereimu.
I Eleazar sin Aronov umrije, i pogreboše ga na brdu Finesa sina njegova, koje mu bješe dano u gori Jefremovoj.

< Yoswa 24 >